< Habakuku 1 >

1 Uthenga umene mneneri Habakuku analandira mʼmasomphenya.
The burden which Habakkuk the prophet saw.
2 Kodi inu Yehova, ndidzakhala ndikukupemphani thandizo kwa nthawi yayitali motani, koma wosayankha? Kapena kufuwulira kwa inu kuti, “Chiwawa kuno!” koma wosatipulumutsa?
O Jehovah, how long shall I cry, and thou will not hear? I cry out to thee of violence, and thou will not save.
3 Chifukwa chiyani mukundionetsa zinthu zoyipa? Chifukwa chiyani mukundionetsa mavutowa? Ndikuona chiwonongeko ndi chiwawa; pali ndewu ndi kukangana kwambiri.
Why do thou show me iniquity, and look upon perverseness? For destruction and violence are before me, and there is strife, and contention rises up.
4 Kotero malamulo anu atha mphamvu, ndipo chilungamo sichikugwira ntchito. Anthu oyipa aposa olungama, kotero apotoza chilungamo.
Therefore the law is slacked, and justice never goes forth. For the wicked man surrounds the righteous man, therefore justice goes forth perverted.
5 “Yangʼanani pakati pa mitundu ya anthu, ndipo penyetsetsani, ndipo muthedwe nazo nzeru. Pakuti ndidzachitadi zinthu pa nthawi yanu zimene inu simudzazikhulupirira, ngakhale wina atakufotokozerani.
Behold ye scoffers, and look, and wonder marvelously. For I am working a work in your days, which ye will not believe though it be told you.
6 Pakuti taonani, Ine ndikuwutsa Ababuloni, anthu ankhanza ndiponso amphamvu, amene amapita pa dziko lonse lapansi kukalanda malo amene si awo.
For, lo, I raise up the Chaldeans, that bitter and hasty nation, who march through the breadth of the earth to possess dwelling-places that are not theirs.
7 Iwowa ndi anthu ochititsa mantha, ndipo ndi owopsa; amadzipangira okha malamulo ndi kudzipezera okha ulemu.
They are fearful and dreadful. Their judgment and their dignity proceed from themselves.
8 Akavalo awo ndi aliwiro kwambiri kupambana akambuku ndi owopsa kupambana mimbulu yolusa nthawi ya madzulo. Okwerapo awo akuthamanga molunjika; a pa akavalo awo ndi ochokera kutali, akuwuluka ngati chiwombankhanga chofuna kugwira nyama;
Their horses also are swifter than leopards, and are more fierce than the evening wolves. And their horsemen press proudly on. Yea, their horsemen come from far. They fly as an eagle that hastens to devour.
9 onse akubwera atakonzekera zachiwawa. Gulu la ankhondo likubwera ngati mphepo ya mʼchipululu ndi kugwira akapolo ochuluka ngati mchenga.
They come all of them for violence. The set of their faces is forwards, and they gather captives as the sand.
10 Akunyoza mafumu ndiponso kuchitira chipongwe olamulira. Akupeputsa mizinda yonse yotetezedwa; akumanga mitumbira ndi kulanda mizindayo.
Yea, he scoffs at kings, and rulers are a derision to him. He derides every stronghold, for he heaps up dust, and takes it.
11 Kenaka amasesa mofulumira ngati mphepo nʼkumangopitirirabe, anthu ochimwa, amene mphamvu zawo ndiye mulungu wawo.”
Then he shall sweep by as a wind, and shall pass over, and be guilty; he whose might is his god.
12 Inu Yehova, kodi sindinu wachikhalire? Mulungu wanga, Woyera wanga, ife sitidzafa. Inu Yehova, munawasankha anthuwo kuti abweretse chiweruzo; Inu Thanthwe, munawayika iwowo kuti atilange.
Are not thou from everlasting, O Jehovah my God, my Holy One? We shall not die. O Jehovah, thou have ordained him for judgment, and thou, O Rock, have established him for correction.
13 Maso anu ndi oyera kwambiri safuna kuona choyipa; Inu simulekerera cholakwa. Chifukwa chiyani nanga mukulekerera anthu ochita zachinyengowa? Chifukwa chiyani muli chete pamene anthu oyipa akuwononga anthu olungama kupambana iwowo?
Thou who are of purer eyes than to behold evil, and who cannot look on perverseness, why do thou look upon those who deal treacherously, and hold thy peace when the wicked man swallows up the man who is more righteous than he,
14 Mwasandutsa anthu kukhala ngati nsomba zamʼnyanja, ngati zolengedwa zamʼnyanja zimene zilibe wolamulira.
and makes men as the fishes of the sea, as the creeping things, that have no ruler over them?
15 Mdani wawo woyipa amakoka anthu onse ndi mbedza, amawakola mu ukonde wake, amawasonkhanitsa mu khoka lake; kotero iyeyo amakondwa ndi kusangalala.
He takes all of them up with the hook. He catches them in his net, and gathers them in his drag. Therefore he rejoices and is glad.
16 Choncho iye amaperekera nsembe ukonde wake ndiponso kufukizira lubani khoka lake, popeza ukonde wakewo ndiye umamubweretsera moyo wapamwamba ndipo amadya chakudya chabwino kwambiri.
Therefore he sacrifices to his net, and burns incense to his drag, because by them his portion is fat, and his food plentiful.
17 Kodi iye azipitirabe kugwiritsa ntchito makoka akewo, kuwononga mitundu ya anthu mopanda chifundo?
Shall he therefore empty his net, and not spare to kill the nations continually?

< Habakuku 1 >