< Malaki 3 >

1 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ine ndidzatuma mthenga wanga amene adzakonza njira pamaso panga. Kenaka mwadzidzidzi Ambuye amene mukumufunafuna adzafika ku Nyumba yake. Mthenga wapangano amene mukumuyembekezera adzabwera.”
Behold, I send my agent, and he shall prepare the way before me. And the Lord, whom ye seek, will suddenly come to his temple. And the messenger of the covenant, whom ye desire, behold, he comes, says Jehovah of hosts.
2 Koma ndani adzatha kupirira pa tsiku la kubwera kwake? Ndani adzatha kuyima pamene Iye wafika? Pakuti adzakhala ngati moto wa mmisiri wa pa ngʼanjo, kapenanso ngati sopo wa munthu wochapa.
But who can abide the day of his coming? And who shall stand when he appears? For he is like a refiner's fire, and like fuller's soap.
3 Iye adzachita kukhalira pansi ngati mmisiri woyenga ndi woyeretsa siliva. Iye adzayeretsa Alevi ndi kuwayenga ngati golide ndi siliva. Pamenepo Yehova adzakhala ndi anthu amene azidzabweretsa zopereka mwachilungamo,
And he will sit as a refiner and purifier of silver. And he will purify the sons of Levi, and refine them as gold and silver. And they shall offer to Jehovah offerings in righteousness.
4 ndipo Yehova adzalandira zopereka za Yuda ndi Yerusalemu, ngati masiku akale, masiku amakedzana.
Then the offering of Judah and Jerusalem shall be pleasant to Jehovah, as in the days of old, and as in ancient years.
5 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Tsono ndidzakuyandikirani kuti ndikuweruzeni. Mosataya nthawi ndidzanena mawu otsutsa mfiti, achigololo, a umboni wonama, amene salipira bwino antchito awo, amene amazunza akazi ndi ana amasiye, amene saweruza alendo mwachilungamo, komanso amene sandiopa Ine.”
And I will come near to you to judgment, and I will be a swift witness against the sorcerers, and against the adulterers, and against the false swearers, and against those who oppress the hireling in his wages, the widow, and the fatherless, and who turn aside the sojourner, and do not fear me, says Jehovah of hosts.
6 “Ine ndine Yehova, ndipo sindisintha. Choncho inu zidzukulu za Yakobo, simunawonongedwe.
For I, Jehovah, do not change. Therefore ye, O sons of Jacob, are not consumed.
7 Kuyambira nthawi ya makolo anu mwakhala mukuphwanya malamulo anga ndipo simunawatsatire. Bwererani kwa Ine, ndipo Ine ndidzabwerera kwa inu,” akutero Yehova Wamphamvuzonse. “Koma inu mukufunsa kuti, ‘Tibwerere motani kwa Yehova?’
From the days of your fathers ye have turned aside from my ordinances, and have not kept them. Return to me, and I will return to you, says Jehovah of hosts. But ye say, How shall we return?
8 “Kodi munthu angathe kuba za Mulungu? Komatu inu mumandibera. “Koma inu mukufunsa kuti, ‘Kodi timakuberani motani?’ “Pa zakhumi ndi pa zopereka.
Will a man rob God? Yet ye rob me. But ye say, How have we robbed thee? In tithes and offerings.
9 Mtundu wanu wonse ndinu otembereredwa, chifukwa mukundibera.
Ye are cursed with the curse, for ye rob me, even this whole nation.
10 Bweretsani chakhumi chathunthu ku nyumba yosungira, kuti mukhale chakudya mʼnyumba mwanga.” Akutero Yehova Wamphamvuzonse, “Tandiyesani, ndipo muone ngati sindidzatsekula zipata zakumwamba, ndi kukugwetserani madalitso ochuluka amene mudzasowe malo owayikamo.
Bring ye the whole tithe into the storehouse, that there may be food in my house, and prove me now with this, says Jehovah of hosts, if I will not open to you the windows of heaven, and pour you out a blessing, that there shall not be room enough for it.
11 Ndidzaletsa tizirombo kuti tisawononge mbewu zanu, ndipo mpesa wa mʼminda mwanu zipatso zake sizidzayoyoka,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
And I will rebuke the devourer for your sakes, and he shall not destroy the fruits of your ground, nor shall your vine cast its fruit before the time in the field, says Jehovah of hosts.
12 “Motero anthu amitundu yonse adzakutchulani odala, pakuti dziko lanu lidzakhala lokondweretsa,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
And all nations shall call you blessed, for ye shall be a delightful land, says Jehovah of hosts.
13 Yehova akuti, “Mwayankhula mawu owawa onena za Ine. “Komabe inu mukufunsa kuti, ‘Kodi tanena chiyani chotsutsana nanu?’
Your words have been stout against me, says Jehovah. Yet ye say, What have we spoken against thee?
14 “Mwanena kuti, ‘Kutumikira Mulungu nʼkosapindulitsa. Kodi timapindulanji pochita zofuna zake, ndi kumayenda ngati anamfedwa pamaso pa Yehova Wamphamvuzonse?
Ye have said, It is vain to serve God, and what profit is it that we have kept his charge, and that we have walked mournfully before Jehovah of hosts?
15 Koma tsono ife timati anthu odzikuza ndiye odalitsika. Kunena zoona anthu oyipa ndiye amapeza bwino, ngakhale amene amanyoza Mulungu amapulumuka.’”
And now we call the proud happy. Yea, those who work wickedness are built up. Yea, they challenge God, and escape.
16 Ndipo woopa Yehova anayamba kukambirana, ndipo Yehova anamvetsera. Buku la chikumbutso linalembedwa pamaso pake, lonena za amene amaopa Yehova ndi kulemekeza dzina lake.
Then those who feared Jehovah spoke one with another, and Jehovah hearkened, and heard, and a book of remembrance was written before him, for those who feared Jehovah, and who thought upon his name.
17 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Anthu amenewo adzakhala anga, tsiku limene Ine ndidzachita izi, adzakhala angaanga. Ndidzawaleka osawalanga monga mmene munthu amachitira chifundo mwana wake amene amamutumikira.
And they shall be mine, says Jehovah of hosts, my own possession, in the day that I make. And I will spare them, as a man spares his own son who serves him.
18 Pamenepo mudzaonanso kusiyana pakati pa anthu olungama ndi oyipa, pakati pa amene amatumikira Mulungu ndi amene satumikira Mulungu.”
Then ye shall return and discern between the righteous man and the wicked man, between him who serves God and him who does not serve him.

< Malaki 3 >