< Malaki 2 >

1 “Tsono chenjezo ili ndi la inu, inu ansembe.”
And now, O ye priests, this commandment is for you.
2 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ngati simumvera, ndipo ngati simulemekeza dzina langa mʼmitima mwanu, ndidzakutembererani ndipo madalitso onse munawalandira ndidzawatemberera. Ndithu, ndawatemberera kale, chifukwa simunalemekeze Ine mʼmitima mwanu.”
If ye will not hear, and if ye will not lay it to heart, to give glory to my name, says Jehovah of hosts, then I will send the curse upon you, and I will curse your blessings. Yea, I have cursed them already, because ye do not lay it to heart.
3 “Ine ndidzalanga zidzukulu zanu chifukwa cha inu; ndidzakupakani kumaso ndowe za nsembe zanu zachikondwerero, ndipo ndidzakutayani pamodzi ndi ndowezo.”
Behold, I will rebuke your seed, and will spread dung upon your faces, even the dung of your feasts, and ye shall be taken away with it.
4 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Apo mudzadziwa kuti Ine ndatumiza chenjezoli kuti pangano langa ndi Levi lipitirire.
And ye shall know that I have sent this commandment to you, that my covenant may be with Levi, says Jehovah of hosts.
5 Ine ndinali naye pa pangano, pangano lopatsa moyo ndi mtendere, ndipo ndinamupatsa zimenezi kuti azindiopa, ndipo anandiopadi ndi kulemekeza dzina langa.
My covenant of life and peace was with him. And I gave them to him that he might fear, and he feared me, and stood in awe of my name.
6 Pakamwa pake pankatuluka malangizo woona, ndipo pa milomo yake sipanapezeke chinyengo. Iye anayenda nane mwamtendere ndi molungama mtima, ndipo anabweza anthu ambiri mʼnjira zawo zauchimo.
The law of truth was in his mouth, and unrighteousness was not found in his lips. He walked with me in peace and uprightness, and turned many away from iniquity.
7 “Pakuti wansembe ayenera kukhala ndi chidziwitso, ndipo anthu ayenera kufunafuna malangizo kuchokera kwa iye, popeza iye ndi mthenga wa Yehova Wamphamvuzonse.
For the priest's lips should keep knowledge, and they should seek the law at his mouth. For he is the messenger of Jehovah of hosts.
8 Koma inu mwasiya njira yanga ndipo mwapunthwitsa anthu ambiri ndi ziphunzitso zanu; mwayipitsa pangano langa ndi Levi,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
But ye are turned aside out of the way. Ye have caused many to stumble in the law. Ye have corrupted the covenant of Levi, says Jehovah of hosts.
9 “Choncho Ine ndachititsa kuti munyozedwe ndi kuchititsidwa manyazi pamaso pa anthu onse, chifukwa simunatsate njira zanga koma mwakhala mukuonetsa kukondera pa nkhani za malamulo.”
Therefore I also have made you contemptible and base before all the people, according as ye have not kept my ways, but have had respect of persons in the law.
10 Kodi sitili naye Atate mmodzi tonsefe? Kodi anatilenga si Mulungu mmodzi? Chifukwa chiyani tikudetsa pangano la makolo athu posamakhulupirirana wina ndi mnzake?
Have we not all one father? Has not one God created us? Why do we deal treacherously every man against his brother, profaning the covenant of our fathers?
11 Yuda waleka kukhulupirika. Chinthu chonyansa chachitika mu Israeli ndi mu Yerusalemu: Yuda wayipitsa malo opatulika amene Yehova amawakonda, pokwatira mkazi wopembedza mulungu wachilendo.
Judah has dealt treacherously, and an abomination is committed in Israel and in Jerusalem. For Judah has profaned the holiness of Jehovah which he loves, and has married the daughter of a foreign god.
12 Ndipo wina aliyense wochita zimenezi, kaya munthuyo ndi wotani, Yehova amuchotse ku banja la Yakobo, ngakhale atabweretsa zopereka kwa Yehova Wamphamvuzonse.
Jehovah will cut off out of the tents of Jacob, the man who does this: him who wakes, and him who answers, and him who offers an offering to Jehovah of hosts.
13 China chimene mumachita ndi ichi: Mumakhathamiritsa guwa lansembe la Yehova ndi misozi. Mumalira ndi kufuwula kwambiri chifukwa Iye amakana kuyangʼana nsembe zanu, kapena kulandira mokondwera nsembe za mʼmanja mwanu.
And this again ye do: Ye cover the altar of Jehovah with tears, with weeping, and with sighing, insomuch that he does not regard the offering any more, nor receives it with good will at your hand.
14 Inu mukufunsa kuti, “Chifukwa chake nʼchiyani?” Chifukwa chake nʼchakuti Yehova ndi mboni ya pangano limene unachita ndi mkazi wa unyamata wako, chifukwa sunakhulupirike kwa iye, ngakhale kuti iyeyo ndiye mnzako, ndi mkazi wako mwapangano.
Yet ye say, Why? Because Jehovah has been witness between thee and the wife of thy youth, against whom thou have dealt treacherously, though she is thy companion, and the wife of thy covenant.
15 Kodi Yehova sanawalenge iwo ngati munthu mmodzi? Ndi ake mʼthupi ndi mu mzimu. Nʼchifukwa chiyani ali mmodzi? Chifukwa Iye amafuna ana opembedza Mulungu. Motero samala moyo wako wauzimu, ndipo usakhale wosakhulupirika kwa mkazi wa unyamata wako.
And did he not make one, although he had the residue of the Spirit? And why one? He sought a godly seed. Therefore take heed to your spirit, and let none deal treacherously against the wife of his youth.
16 Yehova Mulungu wa Israeli akuti, “Ndimadana ndi kulekana ukwati. Ndimadana ndi munthu wochita zankhanza zotere kwa mkazi wake,” akutero Yehova Wamphamvuzonse. Choncho tetezani mzimu wanu, ndipo musakhale osakhulupirika.
For I hate putting away, says Jehovah, the God of Israel, and him who covers his garment with violence, says Jehovah of hosts. Therefore take heed to your spirit, that ye deal not treacherously.
17 Mwamutopetsa Yehova ndi zoyankhula zanu. Inu mukufunsa kuti, “Kodi tamutopetsa bwanji?” Mwamutopetsa ponena kuti, “Aliyense amene amachita zoyipa ndi wabwino pamaso pa Yehova ndipo iye amakondwera naye” kapena pofunsa kuti, “Ali kuti Mulungu woweruza mwachilungamo?”
Ye have wearied Jehovah with your words. Yet ye say, How have we wearied him? In that ye say, Everyone who does evil is good in the sight of Jehovah, and he delights in them, or Where is the God of justice?

< Malaki 2 >