< Levitiko 2 >

1 “‘Munthu wina aliyense akabwera ndi nsembe ya chakudya kwa Yehova, chopereka chake chizikhala ufa wosalala. Ufawo ausakanize ndi mafuta ndi lubani,
And when anyone offers an oblation of a meal offering to Jehovah, his oblation shall be of fine flour, and he shall pour oil upon it, and put frankincense on it.
2 ndipo apite nawo kwa ansembe, ana a Aaroni. Atapeko modzazitsa dzanja ufa wosalala uja kuti ukhale wachikumbutso pamodzi ndi mafuta ndi lubani ndipo atenthe zonsezi pa guwa lansembe kuti zilandiridwe ndi Yehova mʼmalo mwa chopereka chonse. Iyi ndi nsembe yotentha pa moto ndiponso fungo lokomera Yehova.
And he shall bring it to Aaron's sons the priests, and he shall take out of it his handful of the fine flour of it, and of the oil of it, with all the frankincense of it. And the priest shall burn the memorial of it upon the altar, an offering made by fire, of a sweet savor to Jehovah.
3 Zotsala za nsembe ya chakudyazo ndi za Aaroni pamodzi ndi ana ake. Chimenechi ndi chigawo chopatulika kwambiri chifukwa chatapidwa pa chopereka chotentha pa moto cha Yehova.
And that which is left of the meal offering shall be Aaron's and his sons'. It is a thing most holy of the offerings of Jehovah made by fire.
4 “‘Ukabweretsa nsembe ya chakudya chophika mu uvuni, ikhale ya buledi wa ufa wosalala wopanda yisiti koma wosakaniza ndi mafuta, kapena timitanda ta buledi topyapyala, topanda yisiti koma topaka mafuta.
And when thou offer an oblation of a meal offering baked in the oven, it shall be unleavened cakes of fine flour mingled with oil, or unleavened wafers anointed with oil.
5 Ngati nsembe yako yachakudya ndi yophika pa chitsulo chamoto, ikhale ya buledi wa ufa wosalala wopanda yisiti koma wosakaniza ndi mafuta.
And if thy oblation be a meal offering of the baking-pan, it shall be of fine flour unleavened, mingled with oil.
6 Umuduledule bulediyo ndi kumupaka mafuta; imeneyo ndi nsembe yachakudya.
Thou shall part it in pieces, and pour oil in it. It is a meal offering.
7 Ngati nsembe yako yachakudya ndi yophikidwa pa chiwaya, ikhale ya buledi wa ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta.
And if thy oblation be a meal offering of the frying-pan, it shall be made of fine flour with oil.
8 Munthu azibwera ndi nsembe za chakudya zimene wapanga ndi zinthu zimenezi. Atachipereka kwa wansembe, iyeyu adzipita nacho ku guwa.
And thou shall bring the meal offering that is made of these things to Jehovah, and it shall be presented to the priest, and he shall bring it to the altar.
9 Wansembeyo atengeko gawo lina la nsembeyo kukhala ufa wachikumbutso kuti ilandiridwe ndi Yehova mʼmalo mwa nsembe yonse ndipo ayitenthe pa moto monga nsembe yopsereza ya fungo lokomera Yehova.
And the priest shall take up from the meal offering the memorial of it, and shall burn it upon the altar, an offering made by fire, of a sweet savor to Jehovah.
10 Zotsala za nsembe ya chakudyayo zikhale za Aaroni ndi ana ake. Chimenechi ndi chigawo chopatulika kwambiri chifukwa chatapidwa pa chopereka chotentha pa moto cha Yehova.
And that which is left of the meal offering shall be Aaron's and his sons'. It is a thing most holy of the offerings of Jehovah made by fire.
11 “‘Nsembe ya chakudya chilichonse imene ubweretsa kwa Yehova ikhale yopanda yisiti, pakuti suyenera kupereka kwa Yehova nsembe yotentha pa moto imene ili ndi yisiti kapena uchi.
No meal offering, which ye shall offer to Jehovah, shall be made with leaven, for ye shall burn no leaven, nor any honey, as an offering made by fire to Jehovah.
12 Ziwirizi ungathe kubwera nazo kwa Yehova ngati chopereka cha zokolola zoyambirira. Koma usazitenthe pa guwa kuti zikhale fungo lokomera Yehova.
As an oblation of first-fruits ye shall offer them to Jehovah, but they shall not come up for a sweet savor on the altar.
13 Zopereka zako zonse zachakudya uzithire mchere. Usayiwale kuthira mchere pa chopereka chako popeza mcherewo ukusonyeza pangano pakati pa iwe ndi Mulungu wako. Tsono uzinthira mchere pa chopereka chako chilichonse.
And every oblation of thy meal offering thou shall season with salt, nor shall thou allow the salt of the covenant of thy God to be lacking from thy meal offering. With all thine oblations thou shall offer salt.
14 “‘Mukamapereka kwa Yehova chopereka cha chakudya choyamba kucha, choperekacho chikhale cha chipatso chatsopano chokazinga pa moto ndi chopunthapuntha.
And if thou offer a meal offering of first-fruits to Jehovah, thou shall offer for the meal offering of thy first-fruits grain in the ear parched with fire, crushed grain of the fresh ear.
15 Uchithire mafuta ndi lubani pakuti ndi chopereka cha chakudya.
And thou shall put oil upon it, and lay frankincense on it. It is a meal offering.
16 Tsono wansembe atenthe gawo la chopereka chopunthapuntha chija kuti chikhala ufa wachikumbutso ndi cha mafuta pamodzi ndi lubani yense kuti Yehova alandire mʼmalo mwa zopereka zonse. Ichi ndi chopereka chotentha pa moto cha Yehova.
And the priest shall burn the memorial of it, part of the crushed grain of it, and part of the oil of it, with all the frankincense of it. It is an offering made by fire to Jehovah.

< Levitiko 2 >