< Levitiko 1 >

1 Yehova anayitana Mose mu tenti ya msonkhano. Iye anati,
And Jehovah called to Moses, and spoke to him out of the tent of meeting, saying,
2 “Aliyense wa inu ngati abwera ndi nsembe kwa Yehova kuchokera pa ziweto zake, choperekacho chikhale ngʼombe, nkhosa kapena mbuzi.
Speak to the sons of Israel, and say to them, When any man of you offers an oblation to Jehovah, ye shall offer your oblation of the cattle, even of the herd and of the flock.
3 “‘Ngati munthu apereka nsembe yopsereza ya ngʼombe, ikhale yayimuna yopanda chilema. Aziyipereka pa khomo la tenti ya msonkhano, kuti Yehova alandire.
If his oblation be a burnt offering of the herd, he shall offer it a male without blemish. He shall offer it at the door of the tent of meeting, that he may be accepted before Jehovah.
4 Munthuyo asanjike dzanja lake pa mutu pa nsembe yopserezayo, ndipo idzalandiridwa kuti ikhale yopepesera machimo ake.
And he shall lay his hand upon the head of the burnt offering, and it shall be accepted for him to make atonement for him.
5 Pambuyo pake aphe ngʼombeyo pamaso pa Yehova, ndipo ansembe, ana a Aaroni, atenge magazi ake ndi kuwawaza mbali zonse za guwa lansembe limene lili pa khomo la tenti ya msonkhano.
And he shall kill the bullock before Jehovah, and Aaron's sons, the priests, shall present the blood, and sprinkle the blood round about upon the altar that is at the door of the tent of meeting.
6 Munthuyo asende nsembe yopserezayo ndi kuyidula nthulinthuli.
And he shall skin the burnt offering, and cut it into its pieces.
7 Ndipo ana a Aaroni, wansembe uja asonkhe moto pa guwa ndi kuyalapo nkhuni pa motopo.
And the sons of Aaron the priest shall put fire upon the altar, and lay wood in order upon the fire.
8 Kenaka ana a Aaroni, wansembe uja, ayike nthuli za nyamayo, mutu wake pamodzi ndi mafuta omwe pa nkhuni zimene zili paguwapo.
And Aaron's sons, the priests, shall lay the pieces, the head, and the fat, in order upon the wood that is on the fire which is upon the altar,
9 Munthuyo atsuke zamʼkati mwa nyamayo pamodzi ndi miyendo yake yomwe, ndipo wansembe awotche nyama yonse paguwapo. Iyi ndi nsembe yopsereza, chopereka chowotcha pa moto, cha fungo lokomera Yehova.
but its innards and its legs he shall wash with water. And the priest shall burn the whole on the altar, for a burnt offering, an offering made by fire, of a sweet savor to Jehovah.
10 “‘Koma ngati chopereka cha nsembe yopserezayo ndi nkhosa kapena mbuzi kuchokera pa ziweto zake, munthuyo apereke yayimuna yopanda chilema.
And if his oblation be of the flock, of the sheep, or of the goats, for a burnt offering, he shall offer it a male without blemish.
11 Ayiphere kumpoto kwa guwa, pamaso pa Yehova, ndipo ana a Aaroni amene ndi ansembe, awaze magazi ake mbali zonse za guwalo.
And he shall kill it on the side of the altar northward before Jehovah, and Aaron's sons, the priests, shall sprinkle its blood upon the altar round about.
12 Kenaka ayidule nyamayo nthulinthuli, ndipo wansembe ayike nthulizo pa guwa, atengenso mutu ndi mafuta omwe, ndipo ayike zonsezi pa nkhuni zimene zikuyaka pa guwa.
And he shall cut it into its pieces, with its head and its fat, and the priest shall lay them in order on the wood that is on the fire which is upon the altar,
13 Munthuyo atsuke zamʼkati mwa nyamayo pamodzi ndi miyendo yake yomwe, ndipo wansembe abwere nazo zonse ndi kuzitentha pa guwa. Iyi ndi nsembe yopsereza, chopereka chotentha pa moto, fungo lokomera Yehova.
but the innards and the legs he shall wash with water. And the priest shall offer the whole, and burn it upon the altar. It is a burnt offering, an offering made by fire, of a sweet savor to Jehovah.
14 “‘Koma ngati chopereka kwa Yehova ndi nsembe yopsereza ya mbalame, ndiye ikhale njiwa kapena mawunda.
And if his oblation to Jehovah be a burnt offering of birds, then he shall offer his oblation of turtle-doves, or of young pigeons.
15 Wansembe abwere nayo ku guwa, ayidule mutu moyipotola ndi kutentha mutuwo pa guwa. Magazi ake awathire pansi kuti ayenderere pambali pa guwa.
And the priest shall bring it to the altar, and wring off its head, and burn it on the altar. And the blood of it shall be drained out on the side of the altar.
16 Iye achotse chithokomiro pamodzi ndi nthenga zake zomwe ndi kuzitaya ku malo wotayirako phulusa, kummawa kwa guwalo.
And he shall take away its crop with the filth of it, and cast it beside the altar on the east part, in the place of the ashes.
17 Kenaka ayingʼambe pakati, koma asachotse mapiko. Ndipo wansembe ayiwotche pa nkhuni zimene zikuyaka pa guwa. Imeneyi ndi nsembe yopsereza, yowotcha pa moto ndiponso ya fungo lokomera Yehova.
And he shall rend it by the wings of it, but shall not divide it apart, and the priest shall burn it upon the altar, upon the wood that is upon the fire. It is a burnt offering, an offering made by fire, of a sweet savor to Jehovah.

< Levitiko 1 >