< Maliro 3 >

1 Ine ndine munthu amene ndaona masautso ndi ndodo ya ukali wake.
I am the man who has seen affliction by the rod of his wrath.
2 Wandipititsa kutali ndipo wandiyendetsa mu mdima osati mʼkuwala;
He has led me and caused me to walk in darkness, and not in light.
3 zoonadi anandikantha ndi dzanja lake mobwerezabwereza tsiku lonse.
Surely he turns his hand against me, again and again all the day.
4 Wakalambitsa khungu langa ndi mnofu wanga, ndipo waphwanya mafupa anga.
He has made my flesh and my skin old. He has broken my bones.
5 Wandizinga ndi kundizungulira ndi zowawa ndi zolemetsa.
He has built against me, and encompassed me with gall and travail.
6 Wandikhazika mu mdima ngati amene anafa kale.
He has made me to dwell in dark places, as those who have long been dead.
7 Wandimangira khoma kotero kuti sindingathawe, wandimanga ndi maunyolo.
He has walled me around, that I cannot go forth. He has made my chain heavy.
8 Ngakhale pamene ndifuwula kapena kupempha chithandizo, amakana pemphero langa.
Yea, when I cry, and call for help, he shuts out my prayer.
9 Wanditsekera njira yanga ndi miyala yosema; ndipo wakhotetsa tinjira tanga.
He has walled up my ways with hewn stone. He has made my paths crooked.
10 Wandidikirira ngati chimbalangondo, wandibisalira ngati mkango.
He is to me as a bear lying in wait, as a lion in concealed places.
11 Wandikokera pambali ndi kundingʼambangʼamba, ndipo wandisiya wopanda thandizo.
He has turned aside my ways, and pulled me in pieces. He has made me desolate.
12 Wakoka uta wake ndipo walunjikitsa mivi yake pa ine.
He has bent his bow, and set me as a mark for the arrow.
13 Walasa mtima wanga ndi mivi ya mʼphodo mwake.
He has caused the shafts of his quiver to enter into my reins.
14 Ndinakhala choseketsa cha anthu anga onse; amandinyodola mʼnyimbo zawo tsiku lonse.
I have become a derision to all my people, and their song all the day.
15 Wandidyetsa zowawa ndipo wandimwetsa ndulu.
He has filled me with bitterness. He has sated me with wormwood.
16 Wathyola mano anga ndi miyala; wandiviviniza mʼfumbi;
He has also broken my teeth with gravel stones. He has covered me with ashes.
17 Wandichotsera mtendere; ndayiwala kuti kupeza bwino nʼchiyani.
And thou have removed my soul far off from peace. I forgot prosperity.
18 Choncho ndikuti, “Ulemerero wanga wachoka ndi zonse zimene ndimayembekeza kwa Yehova.”
And I said, My strength is perished, and my expectation from Jehovah.
19 Kukumbukira masautso anga ndi kusowa pokhala, zili ngati zowawa ndi ndulu.
Remember my affliction and my misery, the wormwood and the gall.
20 Ine ndikuzikumbukira bwino izi, ndipo moyo wanga wathedwa mʼkati mwanga.
My soul still has them in remembrance, and is bowed down within me.
21 Komabe ndimakumbukira zimenezi, nʼchifukwa chake ndili ndi chiyembekezo.
This I recall to my mind, therefore I have hope:
22 Ife sitinawonongekeretu chifukwa chikondi cha Yehova ndi chachikulu, ndi chifundo chake ndi chosatha.
It is of Jehovah's loving kindnesses that we are not consumed, because his compassions do not fail.
23 Zimaoneka zatsopano mmawa uliwonse; kukhulupirika kwanu nʼkwakukulu.
They are new every morning. Great is thy faithfulness.
24 Mu mtima mwanga ndimati, “Yehova ndiye zanga zonse; motero ndimamuyembekezera.”
Jehovah is my portion, says my soul, therefore I will hope in him.
25 Yehova ndi wabwino kwa amene amayembekezera Iye, kwa munthu amene amafunafuna Iyeyo;
Jehovah is good to those who wait for him, to the soul who seeks him.
26 nʼkwabwino kudikira chipulumutso cha Yehova modekha.
It is good that a man should hope and quietly wait for the salvation of Jehovah.
27 Nʼkwabwino kuti munthu asenze goli pamene ali wamngʼono.
It is good for a man that he bear the yoke in his youth.
28 Akhale chete pa yekha, chifukwa Yehova wamusenzetsa golilo.
Let him sit alone and keep silence, because he has laid it upon him.
29 Abise nkhope yake mʼfumbi mwina chiyembekezo nʼkukhalapobe.
Let him put his mouth in the dust, if so be there may be hope.
30 Apereke tsaya lake kwa iye amene angamumenye, ndipo amuchititse manyazi.
Let him give his cheek to him who smites him. Let him be filled full with reproach.
31 Chifukwa Ambuye satayiratu anthu nthawi zonse.
For the Lord will not cast off forever.
32 Ngakhale amabweretsa zowawa, Iye adzawachitira chifundo, chifukwa chikondi chake ndi chosatha.
For though he causes grief, yet he will have compassion according to the multitude of his loving kindnesses.
33 Pakuti sabweretsa masautso mwadala, kapena zowawa kwa ana a anthu.
For he does not afflict willingly, nor grieve the sons of men.
34 Kuphwanya ndi phazi a mʼndende onse a mʼdziko,
To crush under foot all the prisoners of the earth,
35 kukaniza munthu ufulu wake pamaso pa Wammwambamwamba,
to turn aside the right of a man before the face of the Most High,
36 kumana munthu chiweruzo cholungama— kodi Ambuye saona zonsezi?
to subvert a man in his cause, the Lord does not approve.
37 Kodi ndani angayankhule zinthu nʼkuchitika ngati Ambuye sanavomereze?
Who is he that says, and it comes to pass, when the Lord does not command it?
38 Kodi zovuta ndi zabwino sizituluka mʼkamwa mwa Wammwambamwamba?
Out of the mouth of the Most High does there not come evil and good?
39 Kodi nʼchifukwa chiyani munthu aliyense wamoyo amadandaula akalangidwa chifukwa cha machimo ake?
Why does a living man complain, a man for the punishment of his sins?
40 Tiyeni tisanthule ndi kuyesa njira zathu, ndipo tiyeni tibwerere kwa Yehova.
Let us search and try our ways, and turn again to Jehovah.
41 Tiyeni tikweze mitima yathu ndi manja athu kwa Mulungu kumwamba ndipo tinene kuti:
Let us lift up our heart with our hands to God in the heavens.
42 “Ife tachimwa ndi kuwukira ndipo inu simunakhululuke.
We have transgressed and have rebelled. Thou have not pardoned.
43 “Mwadzikuta ndi mkwiyo ndi kutilondola ndipo mwatitha mopanda chifundo.
Thou have covered with anger and pursued us. Thou have slain; thou have not pitied.
44 Mwadzikuta mu mtambo kotero mapemphero athu sakukufikani.
Thou have covered thyself with a cloud, so that no prayer can pass through.
45 Mwatisandutsa zinyatsi ndi zinyalala pakati pa mitundu ya anthu.
Thou have made us an off-scouring and refuse in the midst of the peoples.
46 “Adani anthu atitsekulira pakamwa.
All our enemies have opened their mouth wide against us.
47 Ife tadzazidwa ndi mantha pakuti tagwa mʼdzenje, tapasuka ndi kuwonongedwa.”
Fear and the pit have come upon us, devastation and destruction.
48 Misozi mʼmaso mwanga ikungoti mbwembwembwe chifukwa anthu anga akuwonongedwa.
My eye runs down with streams of water, for the destruction of the daughter of my people.
49 Misozi idzatsika kosalekeza, ndipo sidzasiya,
My eye pours down, and does not cease, without any intermission,
50 mpaka Yehova ayangʼane pansi kuchokera kumwamba ndi kuona.
till Jehovah looks down, and beholds from heaven.
51 Mtima wanga ukupweteka poona zimenezi chifukwa cha akazi onse a mu mzinda.
My eye stirs my soul, because of all the daughters of my city.
52 Akundisaka ngati mbalame, amene anali adani anga, popanda chifukwa.
They have chased me grievously like a bird, those who are my enemies without cause.
53 Ayesa kundipha pondiponya mʼdzenje ndi kundiponya miyala;
They have cut off my life in the dungeon, and have cast a stone upon me.
54 madzi anamiza mutu wanga ndipo ndinkaganiza kuti imfa yayandikira.
Waters flowed over my head. I said, I am cut off.
55 Ndinayitana dzina lanu Inu Yehova, kuchokera mʼdzenje lozama.
I called upon thy name, O Jehovah, out of the lowest dungeon.
56 Inu munamva kudandaula kwanga. “Mundimvere kulira kwanga kopempha thandizo.”
Thou heard my voice. Hide not thine ear at my breathing, at my cry.
57 Munafika pafupi pamene ndinakuyitanani, ndipo munati, “Usaope.”
Thou drew near in the day that I called upon thee. Thou said, Fear not.
58 Inu Ambuye munandiwombola ku mlandu wanga; munapulumutsa moyo wanga.
O Lord, thou have pleaded the causes of my soul. Thou have redeemed my life.
59 Yehova, mwaona zoyipa zimene andichitira. Mundiweruzire ndinu!
O Jehovah, thou have seen my wrong. Judge thou my cause.
60 Mwaona kuzama kwa kubwezera kwawo, chiwembu chawo chonse pa ine.
Thou have seen all their vengeance and all their devices against me.
61 Inu Yehova mwamva kunyoza kwawo, chiwembu chawo chonse pa ine,
Thou have heard their reproach, O Jehovah, and all their devices against me,
62 manongʼonongʼo a adani anga ondiwukira ine tsiku lonse.
the lips of those who rose up against me, and their device against me all the day.
63 Tawaonani! Kaya ali pansi kapena kuyimirira, akundinyoza mu nyimbo zawo.
Behold thou their sitting down, and their rising up. I am their song.
64 Inu Yehova, muwabwezere chowayenera, chifukwa cha zimene manja awo achita.
Thou will render to them a recompense, O Jehovah, according to the work of their hands.
65 Phimbani mitima yawo, ndipo matemberero anu akhale pa iwo!
Thou will give them hardness of heart, thy curse to them.
66 Muwalondole mwaukali ndipo muwawonongeretu pa dziko lapansi.
Thou will pursue them in anger, and destroy them from under the heavens of Jehovah.

< Maliro 3 >