< Maliro 2 >

1 Haa, Ambuye waphimba mwana wamkazi wa Ziyoni ndi mtambo wa mkwiyo wake! Iye wataya pansi ulemerero wa Israeli kuchoka kumwamba. Pa tsiku la mkwiyo wake Iye sanakumbukirenso popondapo mapazi ake.
How the Lord has covered the daughter of Zion with a cloud in his anger! He has cast down the beauty of Israel from heaven to the earth, and has not remembered his footstool in the day of his anger.
2 Ambuye anawononga midzi yonse ya Yakobo mopanda chifundo; mu mkwiyo wake anagwetsa malinga a mwana wamkazi wa Yuda. Anagwetsa pansi mochititsa manyazi maufumu ndi akalonga ake.
The Lord has swallowed up all the habitations of Jacob, and has not pitied. In his wrath he has thrown down the strongholds of the daughter of Judah. He has brought them down to the ground. He has profaned the kingdom and the rulers thereof.
3 Atakwiya kwambiri, Ambuye anathyola nyanga iliyonse ya Israeli. Anabweza dzanja lake lamanja pamene mdani anamuyandikira. Ambuye anatentha fuko la Yakobo ngati moto wonyeketsa umene umawononga zinthu zonse zomwe zili pafupi.
In fierce anger he has cut off all the horn of Israel. He has drawn back his right hand from before the enemy. And he has burned up Jacob like a flaming fire which devours round about.
4 Wakokera uta wake pa ife ngati ndife adani; wayimiritsa dzanja lake pa ife ngati ndife adani, ndipo anapha onse amene tinkawayangʼana monyadira. Ukali wake ukuyaka ngati moto pa tenti ya mwana wamkazi wa Ziyoni.
He has bent his bow like an enemy. He has stood with his right hand as an adversary, and has slain all who were pleasant to the eye. He has poured out his wrath like fire in the tent of the daughter of Zion.
5 Ambuye ali ngati mdani; wawonongeratu Israeli; wawonongeratu nyumba zake zonse zaufumu ndipo wawononga malinga ake. Iye wachulukitsa kubuma ndi kulira kwa mwana wamkazi wa Yuda.
The Lord has become as an enemy. He has swallowed up Israel. He has swallowed up all her palaces. He has destroyed his strongholds. And he has multiplied mourning and lamentation in the daughter of Judah.
6 Wagwetsa malo ake okhalamo ngati khumbi la mʼmunda; wawononga malo ake a msonkhano. Yehova wayiwalitsa Ziyoni maphwando ake oyikika ndi masabata ake. Mokwiya kwambiri, Iye ananyoza mfumu ndi wansembe.
And he has taken away his tabernacle violently, as a garden. He has destroyed his place of assembly. Jehovah has caused solemn assembly and sabbath to be forgotten in Zion. And in the indignation of his anger has despised the king and the priest.
7 Ambuye wakana guwa lake la nsembe ndipo wasiya malo ake opatulika. Iye wapereka makoma a nyumba zake zaufumu kwa mdani wake; adaniwo anafuwula mʼnyumba ya Yehova ngati kuti ndi pa tsiku la chikondwerero.
The Lord has cast off his altar. He has abhorred his sanctuary. He has given up the walls of her palaces into the hand of the enemy. They have made a noise in the house of Jehovah, as in the day of a solemn assembly.
8 Yehova anatsimikiza kugwetsa makoma a mwana wamkazi wa Ziyoni. Anawayesa ndi chingwe ndipo sanafune kuleka kuwagwetsa. Analiritsa malinga ndi makoma; onse anawonongeka pamodzi.
Jehovah has purposed to destroy the wall of the daughter of Zion. He has stretched out the line. He has not withdrawn his hand from destroying. And he has made the rampart and wall to lament, they languish together.
9 Zipata za Yerusalemu zalowa pansi; wathyola ndi kuwononga mipiringidzo yake. Mfumu ndi akalonga ake agwidwa ukapolo pakati pa mitundu ya anthu, palibenso lamulo, ndipo aneneri ake sakupeza masomphenya kuchokera kwa Yehova.
Her gates are sunk into the ground. He has destroyed and broken her bars. Her king and her rulers are among the nations where the law is not. Yea, her prophets find no vision from Jehovah.
10 Akuluakulu a mwana wamkazi wa Ziyoni akhala chete pansi; awaza fumbi pa mitu yawo ndipo avala ziguduli. Anamwali a Yerusalemu aweramitsa mitu yawo pansi.
The elders of the daughter of Zion sit upon the ground. They keep silence. They have cast up dust upon their heads. They have girded themselves with sackcloth. The virgins of Jerusalem hang down their heads to the ground.
11 Maso anga atopa ndi kulira, ndazunzika mʼmoyo mwanga, mtima wanga wadzaza ndi chisoni chifukwa anthu anga akuwonongeka, chifukwa ana ndi makanda akukomoka mʼmisewu ya mu mzinda.
My eyes fail with tears, my heart is troubled, my liver is poured upon the earth, because of the destruction of the daughter of my people, because the young sons and the sucklings faint in the streets of the city.
12 Anawo akufunsa amayi awo kuti, “Kodi tirigu ndi vinyo zili kuti?” pamene akukomoka ngati anthu olasidwa mʼmisewu ya mʼmizinda, pamene miyoyo yawo ikufowoka mʼmanja mwa amayi awo.
They say to their mothers, Where is grain and wine? when they faint as the wounded in the streets of the city, when their soul is poured out into their mothers' bosom.
13 Ndinganene chiyani za iwe? Ndingakufanizire ndi chiyani, iwe mwana wamkazi wa Yerusalemu? Kodi ndingakufanizire ndi yani kuti ndikutonthoze, iwe namwali wa Ziyoni? Chilonda chako ndi chozama ngati nyanja, kodi ndani angakuchiritse?
What shall I testify to thee? What shall I liken to thee, O daughter of Jerusalem? What shall I compare to thee, that I may comfort thee, O virgin daughter of Zion? For thy breach is great like the sea; who can heal thee?
14 Masomphenya a aneneri ako anali abodza ndi achabechabe. Iwo sanakupulumutse kuti usapite ku ukapolo poyika poyera mphulupulu zako. Mauthenga amene anakupatsa anali achabechabe ndi osocheretsa.
Thy prophets have seen false and foolish visions for thee. And they have not uncovered thine iniquity, to bring back thy captivity, but have seen for thee false oracles and causes of banishment.
15 Onse oyenda mʼnjira yako akukuwombera mʼmanja; akugwedeza mitu yawo ndi kukunyodola iwe mwana wamkazi wa Yerusalemu: “Kodi mzinda uja ndi uwu umene unkatchedwa wokongola kotheratu, chimwemwe cha dziko lonse lapansi?”
All who pass by clap their hands at thee. They hiss and wag their head at the daughter of Jerusalem, saying, Is this the city that men called The perfection of beauty, The joy of the whole earth?
16 Adani ako onse akutsekulira pakamwa ndi kukunyoza; iwo akunyogodola ndi kukukuta mano awo, ndipo akuti, “Tamumeza. Tsiku ili ndi lomwe timayembekezera; tili ndi moyo kuti tilione.”
All thine enemies have opened their mouth wide against thee. They hiss and gnash the teeth. They say, We have swallowed her up. Certainly this is the day that we looked for. We have found, we have seen it.
17 Yehova wachita chimene anakonzeratu; wakwaniritsa mawu ake, amene anatsimikiza kale lomwe. Wakuwononga mopanda chifundo, walola mdani kuti akondwere chifukwa cha kugwa kwako, wakweza mphamvu za adani ako.
Jehovah has done that which he purposed. He has fulfilled his word that he commanded in the days of old. He has thrown down, and has not pitied. And he has caused the enemy to rejoice over thee. He has exalted the horn of thine adversaries.
18 Mitima ya anthu ikufuwulira Ambuye. Iwe khoma la mwana wamkazi wa Ziyoni, misozi yako itsike ngati mtsinje usana ndi usiku; usadzipatse wekha mpumulo, maso ako asaleke kukhetsa misozi.
Their heart cried to the Lord. O wall of the daughter of Zion, let tears run down like a river day and night. Give thyself no respite. Let not the apple of thine eye cease.
19 Dzuka, fuwula usiku, pamene alonda ayamba kulondera; khuthula mtima wako ngati madzi pamaso pa Ambuye. Kweza manja ako kwa Iye chifukwa cha miyoyo ya ana ako, amene akukomoka ndi njala mʼmisewu yonse ya mu mzinda.
Arise, cry out in the night, at the beginning of the watches. Pour out thy heart like water before the face of the Lord. Lift up thy hands toward him for the life of thy young sons, who faint for hunger at the head of every street.
20 Inu Yehova, onani, ndipo ganizirani: kodi ndani amene mwamuchitirapo zinthu ngati izi? Kodi amayi adye ana awo, amene amawasamalira? Kodi ansembe ndi aneneri awaphere mʼmalo opatulika a Ambuye?
See, O Jehovah, and behold to whom thou have done thus! Shall the women eat their fruit, the sons who are dandled in the hands? Shall the priest and the prophet be slain in the sanctuary of the Lord?
21 Anyamata ndi okalamba aligone pamodzi pa fumbi la mʼmisewu ya mu mzinda; anyamata anga ndi anamwali anga aphedwa ndi lupanga. Inu Yehova mwawapha pa tsiku la mkwiyo wanu; mwawapha mopanda chifundo.
The youth and the old man lie on the ground in the streets. My virgins and my young men have fallen by the sword. Thou have slain them in the day of thine anger. Thou have slaughtered, and not pitied.
22 Ngati momwe mumayitanira pa tsiku la phwando, chimodzimodzinso mwandiyitanira zoopsa mbali zonse. Pa tsiku limene Yehova wakwiya palibe amene angathawe ndi kukhala ndi moyo; mdani wanga wawononga onse amene ndinkawasamala ndi kuwalera.
Thou have called, as in the day of a solemn assembly, my terrors on every side. And there was none who escaped or remained in the day of Jehovah's anger. My enemy has consumed those whom I have dandled and brought up.

< Maliro 2 >