< Maliro 1 >

1 Haa! Mzinda uja wasiyidwa wokhawokha, umene kale unali wodzaza ndi anthu! Kale unali wotchuka pakati pa mitundu ya anthu! Tsopano wasanduka ngati mkazi wamasiye. Kale unali mfumukazi ya onse pa dziko lapansi, tsopano wasanduka kapolo.
How the city sits solitary, that was full of people! She has become as a widow, who was great among the nations! She who was a princess among the provinces has become tributary!
2 Ukulira mowawidwa mtima usiku wonse, misozi ili pa masaya pake. Mwa abwenzi ake onse, palibe ndi mmodzi yemwe womutonthoza. Abwenzi ake onse amuchitira chiwembu; onse akhala adani ake.
She weeps bitterly in the night, and her tears are on her cheeks. Among all her loved ones she has none to comfort her. All her friends have dealt treacherously with her, they have become her enemies.
3 Yuda watengedwa ku ukapolo, kukazunzika ndi kukagwira ntchito yolemetsa. Iye akukhala pakati pa anthu a mitundu ina; ndipo alibe malo opumulira. Onse omuthamangitsa iye amupitirira, ndipo alibe kwina kothawira.
Judah has gone into captivity because of affliction. And because of great servitude she dwells among the nations. She finds no rest. All her persecutors overtook her in the distress.
4 Misewu yopita ku Ziyoni ikulira, chifukwa palibe ndi mmodzi yemwe akubwera ku maphwando ake. Zipata zake zonse zili pululu, ansembe akubuwula. Anamwali ake akulira, ndipo ali mʼmasautso woopsa.
The ways of Zion mourn, because none come to the solemn assembly. All her gates are desolate. Her priests sigh. Her virgins are afflicted, and she herself is in bitterness.
5 Adani ake asanduka mabwana ake; odana naye akupeza bwino. Yehova wamubweretsera mavuto chifukwa cha machimo ake ambiri. Ana ake atengedwa ukapolo pamaso pa mdani.
Her adversaries have become the head. Her enemies prosper. For Jehovah has afflicted her for the multitude of her transgressions. Her young sons have gone into captivity before the adversary.
6 Ulemerero wonse wa mwana wamkazi wa Ziyoni wachokeratu. Akalonga ake ali ngati mbawala zosowa msipu; alibe mphamvu zothawira owathamangitsa.
And from the daughter of Zion all her majesty is departed. Her rulers have become like harts that find no pasture. And they have gone without strength before the pursuer.
7 Pa masiku a masautso ndi kuzunzika kwake, Yerusalemu amakumbukira chuma chonse chimene mʼmasiku amakedzana chinali chake. Anthu ake atagwidwa ndi adani ake, panalibe aliyense womuthandiza. Adani ake ankamuyangʼana ndi kumuseka chifukwa cha kuwonongeka kwake.
Jerusalem remembers in the days of her affliction and of her miseries all her pleasant things that were from the days of old. When her people fell into the hand of the adversary, and none helped her, the adversaries saw her; they mocked at her desolations.
8 Yerusalemu wachimwa kwambiri ndipo potero wakhala wodetsedwa. Onse amene ankamulemekeza pano akumunyoza, chifukwa aona umaliseche wake. Iye mwini akubuwula ndipo akubisa nkhope yake.
Jerusalem has grievously sinned, therefore she has become as an unclean thing. All who honored her despise her, because they have seen her nakedness. Yea, she sighs, and turns backward.
9 Uve wake umaonekera pa zovala zake; iye sanaganizire za tsogolo lake. Nʼchifukwa chake kugwa kwake kunali kwakukulu; ndipo analibe womutonthoza. “Inu Yehova, taonani masautso anga, pakuti mdani wapambana.”
Her filthiness was in her skirts. She did not think of her latter end. Therefore she has come down astonishingly. She has no comforter. Behold, O Jehovah, my affliction, for the enemy has magnified himself.
10 Adani amulanda chuma chake chonse; iye anaona mitundu ya anthu achikunja ikulowa mʼmalo ake opatulika, amene Inu Mulungu munawaletsa kulowa mu msonkhano wanu.
The adversary has spread out his hand upon all her pleasant things. For she has seen that the nations have entered into her sanctuary, concerning whom thou commanded that they should not enter into thine assembly.
11 Anthu ake onse akubuwula pamene akufunafuna chakudya; asinthanitsa chuma chawo ndi chakudya kuti akhale ndi moyo. “Inu Yehova, taonani ndipo ganizirani, chifukwa ine ndanyozeka.”
All her people sigh. They seek bread. They have given their pleasant things for food to refresh the soul. See, O Jehovah, and, behold, for I have become abject.
12 “Kodi zimenezi mukuziyesa zachabe, inu nonse mukudutsa? Yangʼanani ndipo muone. Kodi pali mavuto ofanana ndi amene andigwerawa, amene Ambuye anandibweretsera pa tsiku la ukali wake?
Is it nothing to you, all ye who pass by? Behold, and see if there is any sorrow like my sorrow, which is brought upon me. Therewith Jehovah has afflicted in the day of his fierce anger.
13 “Anatumiza moto kuchokera kumwamba, unalowa mpaka mʼmafupa anga. Anayala ukonde kuti ukole mapazi anga ndipo anandibweza. Anandisiya wopanda chilichonse, wolefuka tsiku lonse.
From on high he has sent fire into my bones, and it prevails against them. He has spread a net for my feet. He has turned me back. He has made me desolate and faint all the day.
14 “Wazindikira machimo anga onse ndipo ndi manja ake anawaluka pamodzi. Machimowa afika pakhosi panga, ndipo Ambuye wandithetsa mphamvu. Iye wandipereka kwa anthu amene sindingalimbane nawo.
The yoke of my transgressions is bound by his hand. They are knit together. They have come up upon my neck. He has made my strength to fail. The Lord has delivered me into their hands, against whom I am not able to stand.
15 “Ambuye wakana anthu anga onse amphamvu omwe ankakhala nane: wasonkhanitsa gulu lankhondo kuti lilimbane nane, kuti litekedze anyamata anga; mʼmalo ofinyira mphesa Ambuye wapondereza anamwali a Yuda.
The Lord has trodden under foot all my mighty men in the midst of me. He has called a solemn assembly against me to crush my young men. The Lord has trodden the virgin daughter of Judah as in a winepress.
16 “Chifukwa cha zimenezi ndikulira ndipo maso anga adzaza ndi misozi. Palibe aliyense pafupi woti anditonthoze, palibe aliyense wondilimbitsa mtima. Ana anga ali okhaokha chifukwa mdani watigonjetsa.
For these things I weep. My eye, my eye runs down with water, because the comforter who should refresh my soul is far from me. My sons are desolate, because the enemy has prevailed.
17 “Ziyoni wakweza manja ake, koma palibe aliyense womutonthoza. Yehova walamula kuti abale ake a Yakobo akhale adani ake; Yerusalemu wasanduka chinthu chodetsedwa pakati pawo.
Zion spreads forth her hands. There is none to comfort her. Jehovah has commanded concerning Jacob, that those who are round about him should be his adversaries. Jerusalem is among them as an unclean thing.
18 “Yehova ndi wolungama, koma ndine ndinawukira malamulo ake. Imvani inu anthu a mitundu yonse; onani masautso anga. Anyamata ndi anamwali anga agwidwa ukapolo.
Jehovah is righteous, for I have rebelled against his commandment. Hear, I pray you, all ye peoples, and behold my sorrow. My virgins and my young men have gone into captivity.
19 “Ndinayitana abwenzi anga koma anandinyenga. Ansembe ndi akuluakulu anga anafa mu mzinda pamene ankafunafuna chakudya kuti akhale ndi moyo.
I called for my loved ones, but they deceived me. My priests and my elders gave up the spirit in the city, while they sought food for themselves to refresh their souls.
20 “Inu Yehova, onani mmene ine ndavutikira! Ndikuzunzika mʼkati mwanga, ndipo mu mtima mwanga ndasautsidwa chifukwa ndakhala osamvera. Mʼmisewu anthu akuphedwa, ndipo ku mudzi kuli imfa yokhayokha.
Behold, O Jehovah, for I am in distress. My heart is troubled. My heart is turned within me. For I have grievously rebelled. Abroad the sword bereaves; at home there is as death.
21 “Anthu amva kubuwula kwanga, koma palibe wonditonthoza. Adani anga onse amva masautso anga; iwo akusangalala pa zimene Inu mwachita. Lifikitseni tsiku limene munalonjeza lija kuti iwonso adzakhale ngati ine.
They have heard that I sigh. There is none to comfort me. All my enemies have heard of my trouble. They are glad that thou have done it. Thou will bring the day that thou have proclaimed, and they shall be like me.
22 “Lolani kuti ntchito zawo zoyipa zifike pamaso panu; muwalange ngati mmene mwandilangira ine chifukwa cha machimo anga onse. Ndikubuwula kwambiri ndipo mtima wanga walefuka.”
Let all their wickedness come before thee, and do to them, as thou have done to me for all my transgressions. For my sighs are many, and my heart is faint.

< Maliro 1 >