< Ezekieli 3 >

1 Tsono Mulungu anandiwuza kuti, “Mwana wa munthu, idya chimene ndikukupatsachi. Idya kenaka upite ukayankhule ndi Aisraeli.”
And he said to me, Son of man, eat that which thou find. Eat this roll, and go, speak to the house of Israel.
2 Choncho ndinayasama ndipo anandipatsa mpukutuwo kuti ndidye.
So I opened my mouth, and he caused me to eat the roll.
3 Kenaka Iye anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, idya mpukutu umene ndikukupatsa kuti ukhute.” Choncho ndinadya, ndipo unkatsekemera ngati uchi mʼkamwa mwanga.
And he said to me, Son of man, cause thy belly to eat, and fill thy bowels with this roll that I give thee. Then I ate it, and it was in my mouth as honey for sweetness.
4 Pamenepo Iye anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, pita tsopano kwa Aisraeli ndipo ukawawuze mawu anga.
And he said to me, Son of man, go, get thee to the house of Israel, and speak to them with my words.
5 Sindikukutuma kwa anthu oyankhula chiyankhulo chachilendo ndi chovuta, koma kwa Aisraeli.
For thou are not sent to a people of a strange speech and of a hard language, but to the house of Israel,
6 Sindikukutuma kwa mitundu yambiri ya anthu oyankhula chiyankhulo chachilendo ndi chovuta, amene mawu ake sungawamvetse. Ndithu ndikanakutuma kwa iwowa, bwenzi iwo atakumvera.
not to many peoples of a strange speech, and of a hard language, whose words thou cannot understand. Surely, if I sent thee to them, they would hearken to thee.
7 Koma Aisraeli sadzakumvera chifukwa iwo sakufuna kumvera Ine. Paja Aisraeli onse ndi okanika ndiponso a mtima wowuma.
But the house of Israel will not hearken to thee, for they will not hearken to me. For all the house of Israel are of a hard forehead and of a stiff heart.
8 Tsono ine ndakhwimitsa nkhope yako mofanana ndi nkhope zawo. Ndalimbitsanso mutu wako mofanana ndi mitu yawo.
Behold, I have made thy face hard against their faces, and thy forehead hard against their foreheads.
9 Ine ndidzakusandutsa wolimba ngati mwala wa dayimondi umene uposa thanthwe lina lililonse kulimba kwake. Usachite nawo mantha kapena kuopsedwa nawo. Paja anthuwa ndi awupandu.”
As an adamant, harder than flint, I have made thy forehead. Fear them not, nor be dismayed at their looks, though they are a rebellious house.
10 Anatinso, “Iwe mwana wa munthu, umvetsetse bwino zimene ndikukuwuzazi ndipo mawu angawa uwasunge bwino mu mtima mwako.
Moreover he said to me, Son of man, all my words that I shall speak to thee, receive in thy heart, and hear with thine ears.
11 Tsopano upite kwa Aisraeli anzako amene ali ku ukapolo ndipo ukayankhule nawo. ‘Kaya akamvera kaya sakamvera,’ koma uzikawawuza kuti, Ambuye Wamphamvuzonse akuti zakutizakuti.”
And go, get thee to those of the captivity, to the sons of thy people, and speak to them, and tell them, Thus says the lord Jehovah, whether they will hear, or whether they will forbear.
12 Pamenepo Mzimu unandinyamula ndipo kumbuyo kwanga ndinamva liwu lamphamvu ngati chivomerezi chachikulu, lonena kuti, “Utamandike ulemerero wa Yehova kumene Iye amakhala!”
Then the Spirit lifted me up, and I heard behind me the voice of a great rushing, saying, Blessed be the glory of Jehovah from his place.
13 Phokoso ndinkalimvalo linali la kugundana kwa mapiko a zamoyo ndiponso phokoso la mikombero ya pambali pake ija, limene linkamveka ngati chivomerezi chachikulu.
And I heard the noise of the wings of the living creatures as they touched each other, and the noise of the wheels beside them, even the noise of a great rushing.
14 Mzimu wa Yehova unandikweza ndi kundinyamula ndipo ndinachokapo ndili wowawidwa ndi wonyuka mu mtima. Ndipo dzanja la Yehova linali pa ine mwa mphamvu.
So the Spirit lifted me up, and took me away. And I went in bitterness, in the heat of my spirit, and the hand of Jehovah was strong upon me.
15 Choncho ndinafika kwa amene anali mu ukapolo ku Telabibu pafupi ndi mtsinje wa Kebara. Ndinakhala pansi pakati pawo masiku asanu ndi awiri, ndili wothedwa nzeru kwambiri.
Then I came to those of the captivity at Tel-abib, who dwelt by the river Chebar, and to where they dwelt. And I sat there overwhelmed among them seven days.
16 Atatha masiku asanu ndi awiriwo, Yehova anandiwuza kuti,
And it came to pass at the end of seven days, that the word of Jehovah came to me, saying,
17 “Iwe mwana wa munthu, Ine ndakuyika kuti ukhale mlonda wa Aisraeli. Uziti ukamva mawu anga, ndiye uzikawachenjeza.
Son of man, I have made thee a watchman to the house of Israel. Therefore hear the word at my mouth, and give them warning from me.
18 Ndikawuza munthu woyipa kuti, ‘Iwe udzafa ndithu,’ koma iwe osamuchenjeza kapena kumuyankhula kuti aleke njira zake zoyipa ndi kuti akhale ndi moyo, munthu woyipayo adzafa mu uchimo wake, koma Ine ndidzakuyimba mlandu chifukwa cha imfa yake.
When I say to a wicked man, Thou shall surely die, and thou give him no warning, nor speak to warn the wicked man from his wicked way, to save his life, the same wicked man shall die in his iniquity, but I will require his blood at thy hand.
19 Koma ukamuchenjeza munthu woyipa koma iye osatembenuka mtima kuleka zoyipa zake kapena kusiya njira zake zoyipa, munthuyo adzafa chifukwa cha uchimo wake koma iwe udzapulumutsa moyo wako.
Yet if thou warn the wicked man, and he does not turn from his wickedness, nor from his wicked way, he shall die in his iniquity, but thou have delivered thy soul.
20 “Ngati munthu wolungama asiya chilungamo chake ndi kuchita uchimo ndipo Ine nʼkumuyika mʼzoopsa, munthuyo adzafa ndithu. Popeza iwe sunamuchenjeze, adzafadi chifukwa cha tchimo ndipo chilungamo chake sichidzakumbukiridwa, koma ndidzakuyimba mlandu chifukwa cha imfa yake.
Again, when a righteous man turns from his righteousness, and commits iniquity, and I lay a stumbling block before him, he shall die. Because thou have not given him warning, he shall die in his sin, and his righteous deeds which he has done shall not be remembered, but I will require his blood at thy hand.
21 Koma ngati umuchenjeza munthu wolungama kuti asachimwe ndipo iye nʼkuleka kuchimwa adzakhala ndi moyo ndithu chifukwa anamvera chenjezo, ndipo iwe udzapulumutsa moyo wako.”
Nevertheless if thou warn the righteous man, that the righteous man not sin, and he does not sin, he shall surely live, because he took warning, and thou have delivered thy soul.
22 Nthawi ina dzanja la Yehova linali pa ine ndipo anandiwuza kuti, “Nyamuka upite ku chigwa, kumeneko ndikayankhula nawe.”
And the hand of Jehovah was there upon me, and he said to me, Arise, go forth into the plain, and I will talk with thee there.
23 Choncho ndinanyamuka kupita ku chigwa. Ndipo ndinaona ulemerero wa Yehova kumeneko, ngati ulemerero umene ndinaona mʼmbali mwa mtsinje wa Kebara ndipo ndinagwa pansi chafufumimba.
Then I arose, and went forth into the plain. And, behold, the glory of Jehovah stood there, as the glory which I saw by the river Chebar, and I fell on my face.
24 Koma Mzimu wa Mulungu unalowa mwa ine ndipo unandiyimiritsa. Tsono Yehova anandiyankhula nati: “Pita, kadzitsekere mʼnyumba mwako.
Then the Spirit entered into me, and set me upon my feet. And he spoke with me, and said to me, Go, shut thyself within thy house.
25 Ndipo iwe mwana wa munthu, adzakumanga ndi zingwe motero kuti sudzatha kuyendanso pakati pa anthu.
But thou, son of man, behold, they shall lay bands upon thee, and shall bind thee with them, and thou shall not escape from them.
26 Ndidzamatirira lilime lako kukhosi, kotero kuti udzakhala chete wosatha kuwadzudzula, chifukwa iwo ndi anthu aupandu.
And I will make thy tongue cling to the roof of thy mouth, that thou shall be mute, and shall not be a reprover to them, for they are a rebellious house.
27 Koma pamene ndidzayankhula kwa iwe, ndidzatsekula pakamwa pako ndipo udzawawuza kuti, ‘Ambuye Yehova akuti zakutizakuti.’ Aliyense wofuna kumva amve ndipo wokana kumva, muleke akane; pakuti iwo ndi anthu opanduka.”
But when I speak with thee, I will open thy mouth, and thou shall say to them, Thus says the lord Jehovah. He who hears, let him hear, and he who forbears, let him forbear, for they are a rebellious house.

< Ezekieli 3 >