< Ezekieli 5 >

1 Tsiku lina Yehova anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, tsopano tenga lupanga lakuthwa ndipo uligwiritse ntchito ngati lumo lometera. Umete tsitsi ndi ndevu zako. Kenaka utenge sikelo ndipo ugawe tsitsilo patatu.
And thou, son of man, take thee a sharp sword. As a barber's razor thou shall take it to thee, and shall cause it to pass upon thy head and upon thy beard. Then take thee balances to weigh and divide the hair.
2 Kuzinga mzinda kuja kukatha, chimodzi cha zigawo zitatu za tsitsilo uchitenthe pakati pa mzinda. Chigawo chachiwiri uchiduledule ndi lupanga, poyenda muzungulire mzinda wonsewo. Chigawo chachitatu uchimwazire ku mphepo, ndidzachitsata nditasolola lupanga.
A third part thou shall burn in the fire in the midst of the city when the days of the siege are fulfilled, and thou shall take a third part, and smite with the sword round about it, and a third part thou shall scatter to the wind. And I will draw out a sword after them.
3 Koma utengeko tsitsi pangʼono, ulimange mu mpindiro wa mkanjo wako.
And thou shall take from it a few in number, and bind them in thy skirts.
4 Pa tsitsi limeneli utapepo lina, uliponye pa moto ndi kulitentha. Moto udzayambira pamenepo mpaka ku nyumba yonse ya Israeli.”
And of these again thou shall take, and cast them into the midst of the fire, and burn them in the fire. From there a fire shall come forth into all the house of Israel.
5 Ambuye Yehova akunena kuti, “Uyu ndi Yerusalemu amene ndamuyika pakati pa mitundu ya anthu, ndipo mayiko onse amuzungulira.
Thus says the lord Jehovah: This is Jerusalem. I have set her in the midst of the nations, and countries are round about her.
6 Koma anthu a Yerusalemu aphwanya malamulo anga pochita zoyipa kuposa anthu a mitundu ina. Iwo anandipandukira kupambana anthu ena amene awazungulira. Iwo anakana malamulo anga ndipo sanasunge malangizo anga.
And she has rebelled against my ordinances in doing wickedness more than the nations, and against my statutes more than the countries that are round about her, for they have rejected my ordinances, and as for my statutes, they have not walked in them.
7 “Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akuti: Popeza mwakhala osamvera kupambana anthu a mitundu ina amene akuzungulirani, popeza simunatsate malamulo anga kapena kusunga malangizo anga, mʼmalo mwake mwakhala mukutsata makhalidwe a anthu a mitundu ina amene akuzungulirani.
Therefore thus says the lord Jehovah: Because ye are more disorderly than the nations that are round about you, and have not walked in my statutes, nor have kept my ordinances, no, ye have not even done according to the ordinances of the nations that are round about you,
8 “Tsono Ambuye Yehova akuti: Ine mwini ndikutsutsana nawe, Yerusalemu, choncho Ine ndidzakulangani. Ine ndidzakulangani anthu a mitundu ina akuona.
therefore thus says the lord Jehovah: Behold, I, even I, am against thee, and I will execute judgments in the midst of thee in the sight of the nations.
9 Chifukwa cha ntchito zanu zonyansa ndidzakulangani ndi chilango chimene sindinakulangeni nacho nʼkale lomwe ndipo sindidzakulangani ndi chofanana nacho mʼtsogolomo.
And I will do in thee that which I have not done, and of which I will not do any more the like, because of all thine abominations.
10 Tsono pakati panu makolo adzadya ana awo, ndipo ana adzadya makolo awo. Ndidzakulanga ndipo otsala onse ndidzawabalalitsa ku mphepo zonse zinayi.
Therefore the fathers shall eat the sons in the midst of thee, and the sons shall eat their fathers. And I will execute judgments on thee, and I will scatter to all the winds the whole remnant of thee.
11 Ndithu, pali Ine, akutero Ambuye Yehova Wamoyo, pakuti mwayipitsa Nyumba yanga ndi mafano ano oyipa ndi miyambo yanu yonyansa, Inenso ndidzakulangani. Sindidzakulekererani kapena kukumverani chisoni.
Therefore, as I live, says the lord Jehovah, surely, because thou have defiled my sanctuary with all thy detestable things, and with all thine abominations, therefore I also will diminish thee, nor shall my eye spare. And I also will have no pity.
12 Chimodzi mwa zigawo zitatu za anthu ako chidzafa ndi mliri, kapena chidzawonongeka ndi njala; chigawo china chidzaphedwa ndi lupanga kunja kwa mzinda, ndipo chigawo china ndidzachibalalitsira ku mphepo zonse zinayi pochita kuchithamangitsa.
A third part of thee shall die with the pestilence, and they shall be consumed with famine in the midst of thee, and a third part shall fall by the sword round about thee, and a third part I will scatter to all the winds, and will draw out a sword after them.
13 “Ndi mmene udzachitire mkwiyo wanga. Ndikadzatsiriza kuwalanga, pamenepo mtima wanga udzakhala pansi. Adzadziwa kuti Ine Yehova ndinawayankhula mwa nsanje ndikadzawalanga.
Thus my anger shall be accomplished, and I will cause my wrath toward them to rest, and I shall be comforted. And they shall know that I, Jehovah, have spoken in my zeal, when I have accomplished my wrath upon them.
14 “Ndidzakusandutsa iwe bwinja ndi chinthu chonyozeka pakati pa anthu a mitundu ina amene akuzungulira, ndi kwa onse odutsapo
Moreover I will make thee a desolation and a reproach among the nations that are round about thee, in the sight of all who pass by.
15 Udzakhala chinthu chonyozeka ndi chonyogodoledwa. Udzakhala chenjezo ndi chinthu choopsa kwa anthu a mitundu ina amene akuzungulira ndikadzakulanga mokwiya ndi mwaukali ndi kugamula mlandu wako mokwiya. Ine Yehova ndayankhula.
So it shall be a reproach and a taunt, a lesson and an astonishment, to the nations that are round about thee, when I shall execute judgments on thee in anger and in wrath, and in wrathful rebukes-I, Jehovah, have spoken it-
16 Pamene ndidzakulasa ndi njala yolasa ngati mivi yoopsa ndi yosakaza ndidzatero nʼcholinga choti ndikuwonongeni. Ndidzagwetsa njalayo pa iwe mowirikiza pochepetsa chakudya chako cha tsiku ndi tsiku.
when I shall send upon them the evil arrows of famine that are for destruction, which I will send to destroy you. And I will increase the famine upon you, and will break your staff of bread.
17 Ndidzatumiza njala ndi zirombo za kuthengo, ndipo zidzakulanda ana ako. Mliri ndi kuphana zidzakhala pakati pako, ndipo ndidzakubweretsera nkhondo. Ine Yehova ndayankhula.”
And I will send upon you famine and evil beasts, and they shall bereave thee. And pestilence and blood shall pass through thee. And I will bring the sword upon thee. I, Jehovah, have spoken it.

< Ezekieli 5 >