< Yoweli 1 >

1 Yehova anayankhula ndi Yoweli mwana wa Petueli.
The word of Jehovah that came to Joel the son of Pethuel.
2 Inu akuluakulu, imvani izi; mvetserani, nonse amene mumakhala mʼdziko. Kodi zinthu zokhala ngati izi zinayamba zaonekapo mʼnthawi yanu, kapena mʼnthawi ya makolo anu?
Hear this, ye old men, and give ear, all ye inhabitants of the land. Has this been in your days, or in the days of your fathers?
3 Muwafotokozere ana anu, ndipo ana anuwo afotokozere ana awo, ndipo ana awo adzafotokozere mʼbado winawo.
Tell ye your sons of it, and let your sons tell their sons, and their sons another generation.
4 Chimene dzombe losamera mapiko lasiya dzombe lowuluka ladya; chimene dzombe lowuluka lasiya dzombe lalingʼono ladya; chimene dzombe lalingʼono lasiya chilimamine wadya.
That which the palmer-worm has left the locust has eaten, and that which the locust has left the canker-worm has eaten, and that which the canker-worm has left the caterpillar has eaten.
5 Dzukani, inu zidakwa ndipo mulire! Lirani mofuwula, inu nonse amene mumamwa vinyo; lirani mofuwula chifukwa cha vinyo watsopano, pakuti wachotsedwa pakamwa panu.
Awake, ye drunkards, and weep, and wail, all ye drinkers of wine, because of the sweet wine, for it is cut off from your mouth.
6 Mtundu wa anthu wathira nkhondo dziko langa, wamphamvu ndi wosawerengeka; uli ndi mano a mkango, zibwano za mkango waukazi.
For a nation has come up upon my land, strong, and without number. His teeth are the teeth of a lion, and he has the jaw-teeth of a lioness.
7 Wawononga mphesa zanga ndipo wathyola mitengo yanga ya mkuyu. Wakungunula makungwa ake ndi kuwataya, kusiya nthambi zake zili mbee.
He has laid my vine waste, and barked my fig tree. He has made it clean bare, and cast it away. The branches of it are made white.
8 Lirani ngati namwali wovala chiguduli, chifukwa cha mwamuna wa utsikana wake.
Lament like a virgin girded with sackcloth for the husband of her youth.
9 Chopereka cha chakudya ndi cha chakumwa sizikuperekedwa ku nyumba ya Yehova. Ansembe akulira, amene amatumikira pamaso pa Yehova.
The meal offering and the drink offering are cut off from the house of Jehovah. The priests, Jehovah's ministers, mourn.
10 Minda yaguga, nthaka yauma; tirigu wawonongeka, vinyo watsopano watha, mitengo ya mafuta yauma.
The field is laid waste; the land mourns. For the grain is destroyed, the new wine is dried up, the oil languishes.
11 Khalani ndi nkhawa, inu alimi, lirani mofuwula inu alimi a mphesa; imvani chisoni chifukwa cha tirigu ndi barele, pakuti zokolola za mʼmunda zawonongeka.
Be confounded, O ye husbandmen. Wail, O ye vinedressers, for the wheat and for the barley, for the harvest of the field is perished.
12 Mpesa wauma ndipo mtengo wamkuyu wafota; makangadza, kanjedza ndi mitengo ya apulosi, mitengo yonse ya mʼmunda yauma. Ndithudi chimwemwe cha anthu chatheratu.
The vine is withered, and the fig tree languishes. The pomegranate tree, the palm tree also, and the apple tree, even all the trees of the field are withered. For joy has withered away from the sons of men.
13 Inu ansembe, valani ziguduli ndipo lirani; lirani mofuwula, inu amene mumatumikira pa guwa lansembe. Bwerani, fundani ziguduli usiku wonse, inu amene mumatumikira pamaso pa Mulungu wanga; pakuti chopereka cha chakudya ndi cha chakumwa sizikupezekanso mʼnyumba ya Mulungu wanu.
Gird yourselves with sackcloth, and lament, ye priests. Wail, ye ministers of the altar. Come, lie all night in sackcloth, ye ministers of my God. For the meal offering and the drink offering are withheld from the house of your God.
14 Lengezani tsiku lopatulika losala zakudya, itanani msonkhano wopatulika. Sonkhanitsani akuluakulu ndi anthu onse okhala mʼdziko ku nyumba ya Yehova Mulungu wanu ndipo alirire Yehova.
Sanctify a fast. Call a solemn assembly. Gather the old men and all the inhabitants of the land to the house of Jehovah your God, and cry to Jehovah.
15 Kalanga ine tsikulo! Pakuti tsiku la Yehova layandikira; lidzabwera ngati chiwonongeko chochokera kwa Wamphamvuzonse.
Alas for the day! For the day of Jehovah is at hand, and it shall come as destruction from the Almighty.
16 Kodi chakudya chathu sichachotsedwa ife tikuona? Kodi mʼnyumba ya Mulungu wathu simulibe chimwemwe ndi chisangalalo?
Is not the food cut off before our eyes, yea, joy and gladness from the house of our God?
17 Mbewu zikunyala poti pansi ndi powuma. Nyumba zosungiramo zinthu zawonongeka; nkhokwe zapasuka popeza tirigu wauma.
The seeds rot under their clods. The garners are laid desolate. The barns are broken down. For the grain is withered.
18 Taonani mmene zikulirira ziweto; ngʼombe zikungoyenda uku ndi uku chifukwa zilibe msipu; ngakhalenso nkhosa zikusauka.
How do the beasts groan! The herds of cattle are perplexed because they have no pasture, yea, the flocks of sheep are made desolate.
19 Kwa Inu Yehova ndilirira, pakuti moto wapsereza msipu wakuthengo, malawi amoto apsereza mitengo yonse ya mʼtchire.
O Jehovah, to thee do I cry. For the fire has devoured the pastures of the wilderness, and the flame has burned all the trees of the field.
20 Ngakhale nyama zakuthengo zikulirira Inu; timitsinje tonse taphwa ndipo moto wapsereza msipu wa kuthengo.
Yea, the beasts of the field pant to thee, for the water brooks are dried up, and the fire has devoured the pastures of the wilderness.

< Yoweli 1 >