< Hoseya 14 >

1 Iwe Israeli bwerera kwa Yehova Mulungu wako. Machimo anu ndi amene akugwetsani!
O Israel, return to Jehovah thy God, for thou have fallen by thine iniquity.
2 Bweretsani zopempha zanu ndipo bwererani kwa Yehova. Munene kwa Iye kuti, “Tikhululukireni machimo athu onse ndi kutilandira mokoma mtima, kuti tithe kukuyamikani ndi mawu a pakamwa pathu.
Take with you words, and return to Jehovah. Say to him, Take away all iniquity, and accept that which is good. So we will render as bullocks the offering of our lips.
3 Asiriya sangatipulumutse; ife sitidzakwera pa akavalo ankhondo, sitidzanenanso kuti, ‘Milungu yathu’ kwa zimene manja athu omwe anazipanga, pakuti ndinu amene mumachitira chifundo ana amasiye.”
Assyria shall not save us. We will not ride upon horses, nor will we say any more to the work of our hands, Our gods. For in thee the fatherless finds mercy.
4 Ine ndidzachiza kusakhulupirika kwawo ndipo ndidzawakonda mwaufulu pakuti ndaleka kuwakwiyira.
I will heal their backsliding. I will love them freely. For my anger is turned away from him.
5 Ndidzakhala ngati mame kwa Israeli Ndipo iye adzachita maluwa ngati kakombo. Adzazika mizu yake pansi ngati mkungudza wa ku Lebanoni;
I will be as the dew to Israel. He shall blossom as the lily, and cast forth his roots as Lebanon.
6 mphukira zake zidzakula. Kukongola kwake kudzakhala ngati mtengo wa olivi, kununkhira kwake ngati mkungudza wa ku Lebanoni.
His branches shall spread, and his beauty shall be as the olive tree, and his smell as Lebanon.
7 Anthu adzakhalanso mu mthunzi wake. Iye adzakula bwino ngati tirigu. Adzachita maluwa ngati mphesa ndipo kutchuka kwake kudzakhala ngati vinyo wochokera ku Lebanoni.
Those who dwell under his shadow shall return. They shall revive as the grain, and blossom as the vine. The scent of it shall be as the wine of Lebanon.
8 Efereimu adzati, “Ndidzachita nawonso chiyani mafano? Ine ndidzamuyankha ndi kumusamalira. Ine ndili ngati mtengo wa payini wobiriwira; zipatso zako zimachokera kwa Ine.”
Ephraim shall say, What have I to do any more with idols? I have answered, and will regard him. I am like a green fir tree. From me thy fruit is found.
9 Ndani ali ndi nzeru? Adzazindikire zinthu izi. Ndani amene amamvetsa zinthu? Adzamvetse izi. Njira za Yehova ndi zolungama; anthu olungama amayenda mʼmenemo, koma anthu owukira amapunthwamo.
Who is wise, that he may understand these things, prudent, that he may know them? For the ways of Jehovah are right, and the just shall walk in them. But transgressors shall fall therein.

< Hoseya 14 >