< Amosi 1 >

1 Mawu a Amosi, mmodzi mwa anthu oweta nkhosa ku Tekowa. Zimene iye anaona mʼmasomphenya zokhudza Israeli patatsala zaka ziwiri kuti chivomerezi chichitike, nthawi imene Uziya anali mfumu ya Yuda ndipo Yeroboamu mwana wa Yowasi anali mfumu ya Israeli.
The words of Amos, who was among the herdsmen of Tekoa, which he saw concerning Israel in the days of Uzziah king of Judah, and in the days of Jeroboam the son of Joash king of Israel, two years before the earthquake.
2 Amosi anati: “Yehova akubangula mu Ziyoni ndipo akumveka ngati bingu mu Yerusalemu; msipu wa abusa ukulira, ndipo pamwamba pa Karimeli pakuwuma.”
And he said, Jehovah will roar from Zion, and utter his voice from Jerusalem, and the pastures of the shepherds shall mourn, and the top of Carmel shall wither.
3 Yehova akuti, “Chifukwa anthu a ku Damasiko akunka nachimwirachimwira, Ine sindileka kuwalanga. Popeza anapuntha Giliyadi ndi zopunthira za mano achitsulo,
Thus says Jehovah: For three transgressions of Damascus, yea, for four, I will not turn away the punishment of it, because they have threshed Gilead with threshing instruments of iron.
4 Ine ndidzatumiza moto pa nyumba ya Hazaeli umene udzanyeketsa nyumba zaufumu za Beni-Hadadi.
But I will send a fire into the house of Hazael, and it shall devour the palaces of Ben-hadad.
5 Ndidzathyola chipata cha Damasiko; ndidzawononga mfumu yokhala ku Chigwa cha Aveni, ndiponso iye amene akugwira ndodo yaufumu mu Beti-Edeni. Anthu a ku Aramu adzapita ku ukapolo ku Kiri,” akutero Yehova.
And I will break the bar of Damascus, and cut off the inhabitant from the valley of Aven, and he who holds the scepter from the house of Eden, and the people of Syria shall go into captivity to Kir, says Jehovah.
6 Yehova akuti, “Chifukwa anthu a ku Gaza akunka nachimwirachimwira, Ine sindileka kuwalanga. Popeza anatenga ukapolo mtundu wathunthu ndi kuwugulitsa ku Edomu,
Thus says Jehovah: For three transgressions of Gaza, yea, for four, I will not turn away the punishment of it, because they carried away captive the whole people, to deliver them up to Edom.
7 ndidzatumiza moto pa makoma a Gaza umene udzanyeketsa nyumba zake zaufumu.
But I will send a fire on the wall of Gaza, and it shall devour the palaces of it.
8 Ndidzawononga mfumu ya ku Asidodi komanso amene akugwira ndodo yaufumu ku Asikeloni. Ndidzalanga Ekroni, mpaka wotsala mwa Afilisti atafa,” akutero Ambuye Yehova.
And I will cut off the inhabitant from Ashdod, and him who holds the scepter from Ashkelon. And I will turn my hand against Ekron, and the remnant of the Philistines shall perish, says the lord Jehovah.
9 Yehova akuti, “Chifukwa anthu a ku Turo akunka nachimwirachimwira, Ine sindileka kuwalanga. Popeza iwo anagulitsa mtundu wathunthu ku ukapolo ku Edomu, osasunga pangano laubale lija,
Thus says Jehovah: For three transgressions of Tyre, yea, for four, I will not turn away the punishment of it, because they delivered up the whole people to Edom, and did not remember the brotherly covenant.
10 Ine ndidzatumiza moto pa makoma a Turo umene udzanyeketsa nyumba zake zaufumu.”
But I will send a fire on the wall of Tyre, and it shall devour the palaces of it.
11 Yehova akuti, “Chifukwa anthu a ku Edomu akunka nachimwirachimwira, Ine sindileka kuwalanga. Popeza anathamangitsa mʼbale wake ndi lupanga, popanda nʼchifundo chomwe. Popeza mkwiyo wake unakulabe ndipo ukali wake sunatonthozeke,
Thus says Jehovah: For three transgressions of Edom, yea, for four, I will not turn away the punishment of it, because he pursued his brother with the sword, and cast off all pity. And his anger tore perpetually, and he kept his wrath forever.
12 Ine ndidzatumiza moto pa Temani umene udzanyeketsa nyumba zaufumu za Bozira.”
But I will send a fire upon Teman, and it shall devour the palaces of Bozrah.
13 Yehova akuti, “Chifukwa anthu a ku Amoni akunka nachimwirachimwira, Ine sindileka kuwalanga. Popeza anatumbula akazi oyembekezera a ku Giliyadi nʼcholinga choti akuze malire awo,
Thus says Jehovah: For three transgressions of the sons of Ammon, yea, for four, I will not turn away the punishment of it, because they have ripped up the women with child of Gilead, that they may enlarge their border.
14 Ine ndidzayatsa moto pa makoma a ku Raba umene udzanyeketsa nyumba zake zaufumu. Padzakhala kulira kwakukulu pa tsiku la nkhondoyo, kumenyana kudzakhala kwafumbi ngati mkuntho wa kamvuluvulu.
But I will kindle a fire in the wall of Rabbah, and it shall devour the palaces of it, with shouting in the day of battle, with a tempest in the day of the whirlwind.
15 Mfumu yawo idzatengedwa kupita ku ukapolo, iyo pamodzi ndi akuluakulu ake,” akutero Yehova.
And their king shall go into captivity, he and his rulers together, says Jehovah.

< Amosi 1 >