< Yobu 30 >

1 “Koma tsopano akundinyoza, ana angʼonoangʼono kwa ine, anthu amene makolo awo sindikanawalola kuti azithandizana ndi agalu anga kuweta nkhosa zanga.
But now those who are younger than I have me in derision, whose fathers I disdained to set with the dogs of my flock.
2 Kodi mphamvu zawo ndi za phindu lanji kwa ine, pakuti mphamvu zawo zinatha kale?
Yea, the strength of their hands, to what should it profit me? Men in whom ripe age is perished.
3 Anali atatheratu kuwonda ndi njala, ankayendayenda mʼdziko lopanda madzi, mʼchipululu usiku.
They are gaunt with want and famine. They gnaw the dry ground in the gloom of waste and desolation.
4 Ankathyola therere ndi masamba owawa, ndipo chakudya chawo chinali mizu ya mitengo ya masache.
They pluck mallows by the bushes, and the roots of the juniper are their food.
5 Anapirikitsidwa pakati pa anthu anzawo, akuwakuwiza ngati kuti anali akuba.
They are driven forth from the midst of men. They cry out after them as after a thief,
6 Anawumirizidwa kukhala ku zigwembe za mitsinje yowuma, pakati pa matanthwe ndi mʼmaenje a mʼnthaka.
so that they dwell in frightful valleys, in holes of the earth and of the rocks.
7 Ankalira ngati nyama kuthengo ndipo ankawunjikana pamodzi pa ziyangoyango.
Among the bushes they bray, under the nettles they are gathered together.
8 Anali anthu achabechabe ndi wopanda dzina, anathamangitsidwa mʼdziko.
They are sons of fools, yea, sons of base men. They were scourged out of the land.
9 “Ndipo tsopano ana awo akundiyimba nyimbo zachipongwe; ineyo ndasanduka chisudzo chawo.
And now I have become their song, Yea, I am a byword to them.
10 Iwo amanyansidwa nane ndipo amandithawa; akandiona salephera kundilavulira mʼmaso mwangamu.
They abhor me. They stand aloof from me, and do not spare to spit in my face.
11 Tsopano pakuti Mulungu wakhwefula uta wanga ndipo wandisautsa, iwowo analekeratu kundiopa.
For he has loosed his cord, and afflicted me. And they have cast off the bridle before me.
12 Ku dzanja langa lamanja anthu akulimbana nane; andikumbira dzenje loti ndigweremo ndikamayenda, andipangira mitumbira ya nkhondo kuti alimbane nane.
Upon my right hand rise the rabble. They thrust aside my feet, and they cast up against me their ways of destruction.
13 Iwo anditsekera njira; akufuna kundichititsa ngozi, popanda wina aliyense wowaletsa.
They mar my path. They set forward my calamity, even men who have no helper.
14 Akundithamangitsa ngati madzi olowera pa mpanda wobowoka, iwo akubwererabwerera pakati pa chipasupasu.
As through a wide breach they come. In the midst of the ruin they roll themselves upon me.
15 Zoopsa zandithetsa mphamvu; ulemu wanga wachita ngati wauluzika ndi mphepo, chuma changa chija chazimirira ngati mtambo.
Terrors are turned upon me. They chase my honor as the wind, and my welfare is passed away as a cloud.
16 “Ndipo tsopano mtima wanga wachokamo; ndili mʼmasiku amasautso.
And now my soul is poured out within me. Days of affliction have taken hold upon me.
17 Mafupa anga akuphwanya usiku pakuti zowawa zanga sizikuleka.
In the night season my bones are pierced in me, and the pains that gnaw me take no rest.
18 Mʼmphamvu zake Mulungu wakhala ngati chovala changa; Iye wandigwira ngati chovala chondithina pa khosi.
By the great force my garment is disfigured. It binds me about as the collar of my coat.
19 Wandiponya mʼmatope, ndipo ndasanduka ngati fumbi ndi phulusa.
He has cast me into the mire, and I have become like dust and ashes.
20 “Inu Mulungu, ine ndikulirira kwa Inu, koma simukundiyankha; ndikayimirira, Inu simundiyangʼana nʼkomwe.
I cry to thee, and thou do not answer me. I stand up, and thou gaze at me.
21 Inuyo mumandichitira zankhanza; mumandizunza ndi dzanja lanu lamphamvu.
Thou have turned to be cruel to me. With the might of thy hand thou persecute me.
22 Mwandinyamulira ku mphepo ndipo mwandiwulutsa ndi mphepoyo; mwandiponya mʼmphepo ya mkuntho.
Thou lift me up to the wind. Thou cause me to ride upon it, and thou disintegrate me in the storm.
23 Ndikudziwa kuti Inu mudzandifikitsa ku imfa, kumalo kumene amoyo onse adzapitako.
For I know that thou will bring me to death, and to the house appointed for all living.
24 “Ndithudi palibe munthu amene amalanga munthu wosweka mtima, amene akupempha thandizo mʼmasautso ake.
However does not a man stretch out the hand in his fall? Or in his calamity therefore cry for help?
25 Kodi ine sindinalire nawo iwo amene anali pamavuto? Kodi mtima wanga sunamvere chisoni anthu osauka?
Did I not weep for him who was in trouble? Was not my soul grieved for the needy?
26 Koma pamene ndinkayembekezera zabwino, zoyipa ndiye zinandigwera; pamene ndinkafunafuna kuwala, mdima ndiye unandigwera.
When I looked for good, then evil came. And when I waited for light, there came darkness.
27 Kuwawa kwa mʼkati mwanga sikukuleka; ndili mʼmasiku amasautso.
My heart is troubled, and does not rest. Days of affliction have come upon me.
28 Ndikuyenda wothimbirira, komatu osati ndi dzuwa; ndimayimirira pa msonkhano ndi kupempha chithandizo molira.
I go mourning without the sun. I stand up in the assembly, and cry for help.
29 Ndasanduka mʼbale wa nkhandwe, mnzawo wa akadzidzi.
I am a brother to jackals, and a companion to ostriches.
30 Khungu langa layamba kuda ndipo likufunduka; thupi langa likutentha chifukwa cha kuphwanya kwa thupi.
My skin is black, and falls from me. And my bones are burned with heat.
31 Pangwe wanga wasanduka woyimbira maliro, ndipo chitoliro changa chikuyimbira anthu olira.
Therefore my harp has turned to mourning, and my pipe into the voice of those who weep.

< Yobu 30 >