< Yobu 17 >

1 “Mtima wanga wasweka, masiku anga atha, manda akundidikira.
Mon souffle s'épuise, mes jours s'éteignent, il ne me reste plus que le tombeau.
2 Ndithudi, anthu ondiseka andizungulira; maso anga akupenyetsetsa mdani wanga.
Je suis environné de moqueurs, mon œil veille au milieu de leurs outrages.
3 “Inu Mulungu, patseni chikole chimene mukufuna. Ndani wina amene adzandiperekera ine chikole?
O Dieu, fais-toi auprès de toi-même ma caution: quel autre voudrait me frapper dans la main?
4 Inu mwatseka maganizo awo kuti asamvetse zinthu; choncho simudzawalola kuti apambane.
Car tu as fermé leur cœur à la sagesse; ne permets donc pas qu'ils s'élèvent.
5 Ngati munthu apereka mnzake chifukwa cha chuma, ana ake sadzaona mwayi.
Tel invite ses amis au partage, quand défaillent les yeux de ses enfants.
6 “Mulungu wandisandutsa chisudzo chochiseka aliyense, munthu amene anthu amalavulira malovu nkhope yake.
Il a fait de moi la risée des peuples; je suis l'homme à qui l'on crache au visage.
7 Mʼmaso mwanga mwada ndi chisoni; ndawonda ndi mutu womwe.
Mon œil est voilé par le chagrin, et tous mes membres ne sont plus qu'une ombre.
8 Anthu olungama akudabwa nazo zimenezi; anthu osachimwa akupsera mtima anthu osapembedza Mulungu.
Les hommes droits en sont stupéfaits, et l'innocent s'irrite contre l'impie.
9 Komabe anthu olungama adzasunga njira zawo, ndipo anthu a makhalidwe abwino mphamvu zawo zidzanka zikuchuluka.
Le juste néanmoins demeure ferme dans sa voie, et qui a les mains pures redouble de courage.
10 “Tsono bwerani nonsenu, bwerezaninso mawu anuwo, sindidzapezapo munthu wanzeru pakati panupo.
Mais vous tous, revenez, venez donc; ne trouverai-je pas un sage parmi vous?
11 Masiku anga atha, zimene ndinakonza zalephereka, pamodzinso ndi zokhumba za mtima wanga.
Mes jours sont écoulés, mes projets anéantis, ces projets que caressait mon cœur.
12 Anthu awa amasandutsa usiku kukhala usana, nthawi ya usiku iwo amati ‘kwatsala pangʼono kucha.’
De la nuit ils font le jour; en face des ténèbres, ils disent que la lumière est proche!
13 Ngati nyumba imene ndikuyiyembekezera ndi manda, ngati ndiyala bedi langa mu mdima, (Sheol h7585)
J'ai beau attendre, le schéol est ma demeure; dans les ténèbres j'ai disposé ma couche. (Sheol h7585)
14 ngati ndinena kwa dzenje la manda ‘ndinu abambo anga,’ ndiponso kwa mphutsi kuti, ‘ndinu amayi anga’ kapena ‘mlongo wanga,’
J'ai dit à la fosse: « Tu es mon père; » aux vers: « Vous êtes ma mère et ma sœur! »
15 tsono chiyembekezo changa chili kuti? Ndani angaone populumukira panga?
Où est donc mon espérance? Mon espérance, qui peut la voir?
16 Ndithu sindidzakhalanso ndi chiyembekezo chilichonse, polowa mʼmanda, pamene ndidzatsikira ku fumbi.” (Sheol h7585)
Elle est descendue aux portes du schéol, si du moins dans la poussière on trouve du repos!... (Sheol h7585)

< Yobu 17 >