< Yobu 18 >

1 Pamenepo Bilidadi wa ku Suki anayankha kuti,
Alors Baldad de Suhé prit la parole et dit:
2 “Kodi iwe Yobu utsiriza liti zoyankhula zakozi? Khala munthu wozindikira zinthu ndipo ukatero ife tidzayankhula.
Quand donc mettrez-vous un terme à ces discours? Ayez de l'intelligence, puis nous parlerons.
3 Chifukwa chiyani ukutiyesa ngati ngʼombe ndi kuoneka ngati opusa mʼmaso mwako?
Pourquoi nous regardez-vous comme des brutes, et sommes-nous stupides à vos yeux?
4 Iwe amene ukudzipweteka wekha ndi mkwiyo wako, kodi dziko lapansi lisanduke bwinja chifukwa cha iweyo? Kodi kapena thanthwe lisunthidwe kuchoka pa malo ake?
Toi qui te déchires dans ta fureur, veux-tu qu'à cause de toi la terre devienne déserte, que le rocher soit transporté hors de sa place?
5 “Nyale ya munthu woyipa yazimitsidwa; malawi a moto wake sakuwalanso.
Oui, la lumière du méchant s'éteindra, et la flamme de son foyer cessera de briller.
6 Kuwala kwa mʼnyumba mwake kwasanduka mdima; nyale ya pambali pake yazima.
Le jour s'obscurcira sous sa tente, sa lampe s'éteindra au-dessus de lui.
7 Mayendedwe ake amgugu azilala; fundo zake zomwe zamugwetsa.
Ses pas si fermes seront à l'étroit, son propre conseil précipite sa chute.
8 Mapazi ake amulowetsa mu ukonde ndipo akungoyendayenda mu ukondewo.
Ses pieds le jettent dans les rets, il marche sur le piège.
9 Msampha wamkola mwendo; khwekhwe lamugwiritsitsa.
Le filet saisit ses talons; il est serré dans ses nœuds.
10 Amutchera msampha pansi mobisika; atchera diwa pa njira yake.
Pour lui les lacs sont cachés sous terre, et la trappe est sur son sentier.
11 Zoopsa zikumuchititsa mantha kumbali zonse, zikutsatira mayendedwe ake onse.
De tous côtés des terreurs l'assiègent, et le poursuivent pas à pas.
12 Mphamvu zake zatha chifukwa cha njala, tsoka likumudikira.
La disette est son châtiment, et la ruine est prête pour sa chute.
13 Wagwidwa nthenda yoopsa thupi lonse; miyendo yake, manja ake, zonse zawola.
La peau de ses membres est dévorée; ses membres sont dévorés par le premier-né de la mort.
14 Wachotsedwa mʼnyumba imene ankadalira, ndipo amukokera ku imfa, mfumu ya zoopsa zonse.
Il est arraché de sa tente, où il se croyait en sûreté; on le traîne vers le Roi des frayeurs.
15 Mʼnyumba mwake zonse zachotsedwamo; awazamo sulufule kuti aphe tizirombo ta matenda.
Nul des siens n'habite dans sa tente, le soufre est semé sur sa demeure.
16 Mizu yake ikuwuma pansi ndipo nthambi zake zikufota
En bas, ses racines se dessèchent, en haut, ses rameaux sont coupés.
17 Sadzakumbukiridwanso pa dziko lapansi; sadzakhalanso ndi chinthu chomutchukitsa mʼdziko.
Sa mémoire a disparu de la terre, il n'a plus de nom dans la contrée.
18 Amuchotsa pa malo owala ndi kumuponya ku mdima, ndipo amupirikitsa pa dziko lonse.
On le chasse de la lumière dans les ténèbres, on le bannit de l'univers.
19 Iye alibe ana kapena zidzukulu pakati pa anthu ake, kulibe wotsala kumene iye ankakhala.
Il ne laisse ni descendance ni postérité dans sa tribu; aucun survivant dans son séjour.
20 Anthu akumadzulo adabwa kwambiri ndi tsoka lake; anthu akummawa agwidwa ndi mantha aakulu.
Les peuples de l'Occident sont stupéfaits de sa ruine, et ceux de l'Orient en sont saisis d'horreur.
21 Ndithudi, izi ndiye zimagwera munthu woyipa; amenewa ndiye mathero a munthu amene sadziwa Mulungu.”
Telle est la demeure de l'impie, telle est la place de l'homme qui ne connaît pas Dieu.

< Yobu 18 >