< Yobu 16 >

1 Pamenepo Yobu anayankha kuti,
Alors Job prit la parole et dit:
2 “Ndinamvapo zambiri monga zimenezi; nonsenu ndinu anthu osatha kutonthoza mtima mnzanu.
J'ai souvent entendu de semblables harangues; vous êtes tous d'insupportables consolateurs.
3 Kodi mawu anu ochulukawo adzatha? Kodi chikukuvutani nʼchiyani kuti muzingoyankhula mawu otsutsawa?
Quand finiront ces vains discours? Quel aiguillon t'excite à répliquer?
4 Inenso ndikanatha kuyankhula monga inu, inuyo mukanakhala monga ndilili inemu; Ine ndikanatha kuyankhula mawu omveka bwino kutsutsana nanu ndi kukupukusirani mutu wanga.
Moi aussi, je saurais parler comme vous, si vous étiez à ma place; j'arrangerais de beaux discours à votre adresse, je secouerais la tête sur vous;
5 Ndipo mawu a pakamwa panga akanakulimbikitsani; chitonthozo chochokera pa milomo yanga chikanachepetsa ululu wanu.
je vous encouragerais de la bouche, et vous auriez pour soulagement l'agitation de mes lèvres.
6 “Koma ine ndikati ndiyankhule ululu wanga sukuchepa; ndipo ndikati ndikhale chete, ululu wanga sukuchokabe.
Si je parle, ma douleur n'est pas adoucie; si je me tais, en est-elle soulagée?
7 Ndithudi, Inu Mulungu mwanditha mphamvu; mwawononga banja langa lonse.
Aujourd'hui, hélas! Dieu a épuisé mes forces... ô Dieu, tu as moissonné tous mes proches.
8 Inu mwandimanga ndipo kundimangako kwakhala umboni; kuwonda kwanga kwandiwukira ndipo kukuchita umboni wonditsutsa.
Tu me garrottes... c'est un témoignage contre moi!... ma maigreur se lève contre moi, en face elle m'accuse.
9 Mulungu amabwera kwa ine mwankhanza ndipo amadana nane, amachita kulumira mano; mdani wanga amandituzulira maso.
Sa colère me déchire et me poursuit, il grince des dents contre moi; mon ennemi darde sur moi ses regards.
10 Anthu amatsekula pakamwa pawo kundikuwiza; amandimenya pa tsaya mwachipongwe ndipo amagwirizana polimbana nane.
Ils ouvrent leur bouche pour me dévorer, ils me frappent la joue avec outrage, ils se liguent tous ensemble pour me perdre.
11 Mulungu wandipereka kwa anthu ochita zoyipa ndipo wandiponyera mʼmanja mwa anthu oyipa mtima.
Dieu m'a livré au pervers, il m'a jeté entre les mains des méchants.
12 Ine ndinali pamtendere, koma Mulungu ananditswanya; anandigwira pa khosi ndi kundiphwanya. Iye anandisandutsa choponyera chandamale chake;
J'étais en paix, et il m'a secoué, il m'a saisi par la nuque, et il m'a brisé. Il m'a posé en but à ses traits,
13 anthu ake oponya mauta andizungulira. Mopanda kundimvera chisoni, Iye akulasa impsyo zanga ndipo akutayira pansi ndulu yanga.
ses flèches volent autour de moi; il perce mes flancs sans pitié, il répand mes entrailles sur la terre;
14 Akundivulaza kawirikawiri, akuthamangira pa ine monga munthu wankhondo.
il me fait brèche sur brèche, il fond sur moi comme un géant.
15 “Ndasokerera chiguduli pa thupi langa ndipo ndayika mphamvu zanga pa fumbi.
J'ai cousu un sac sur ma peau, et j'ai roulé mon front dans la poussière.
16 Maso anga afiira ndi kulira, ndipo zikope zanga zatupa;
Mon visage est tout rouge de larmes, et l'ombre de la mort s'étend sur mes paupières,
17 komatu manja anga sanachite zachiwawa ndipo pemphero langa ndi lolungama.
quoiqu'il n'y ait pas d'iniquités dans mes mains, et que ma prière soit pure.
18 “Iwe dziko lapansi, usakwirire magazi anga; kulira kwanga kofuna thandizo kusalekeke!
O terre, ne couvre point mon sang, et que mes cris s'élèvent librement!
19 Ngakhale tsopano mboni yanga ili kumwamba; wonditchinjiriza pa mlandu wanga ali komweko.
A cette heure même, voici que j'ai mon témoin dans le ciel, mon défenseur dans les hauts lieux.
20 Wondipembedzera ndi bwenzi langa, pamene maso anga akukhuthula misozi kwa Mulungu;
Mes amis se moquent de moi, c'est vers Dieu que pleurent mes yeux.
21 iye, mʼmalo mwanga, amamudandaulira Mulungu monga munthu amadandaulira bwenzi lake.
Qu'il juge lui-même entre Dieu et l'homme, entre le fils de l'homme et son semblable!
22 “Pakuti sipapita zaka zambiri ndisanayende mʼnjira imene sindidzabwerera.”
Car les années qui me sont comptés s'écoulent, et j'entre dans un sentier d'où je ne reviendrai pas.

< Yobu 16 >