< Yeremiya 25 >

1 Yehova anayankhula ndi Yeremiya za anthu onse a ku Yuda mʼchaka chachinayi cha ufumu wa Yehoyakimu mwana wa Yosiya mfumu ya ku Yuda, chimene chinali chaka choyamba cha ufumu wa Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni.
The word that came to Jeremiah concerning all the people of Judah, in the fourth year of Jehoiakim the son of Josiah, king of Judah (the same was the first year of Nebuchadrezzar king of Babylon),
2 Choncho mneneri Yeremiya anawuza anthu onse a ku Yuda pamodzi ndi onse amene amakhala mu Yerusalemu kuti:
which Jeremiah the prophet spoke to all the people of Judah, and to all the inhabitants of Jerusalem, saying,
3 Kwa zaka 23, kuyambira chaka cha 13 cha ufumu wa Yosiya mwana wa Amoni mfumu ya ku Yuda mpaka lero lino, Yehova wakhala akundipatsa mauthenga ake ndipo ine ndakhala ndikuyankhula ndi inu kawirikawiri, koma inu simunamvere.
From the thirteenth year of Josiah the son of Amon, king of Judah, even to this day, these twenty-three years, the word of Jehovah has come to me, and I have spoken to you, rising up early and speaking. But ye have not hearkened.
4 Ndipo ngakhale Yehova kawirikawiri wakhala akukutumizirani atumiki ake onse, aneneri, inuyo simunamvere kapena kutchera khutu.
And Jehovah has sent to you all his servants the prophets, rising up early and sending them, (but ye have not hearkened, nor inclined your ear to hear),
5 Aneneriwo ankanena kuti, “Ngati aliyense wa inu abwerere, kusiya njira zake zoyipa ndi machitidwe ake oyipa, ndiye kuti mudzakhala mʼdziko limene Yehova anapereka kwa makolo anu kwamuyaya.
saying, Return ye now each one from his evil way, and from the evil of your doings, and dwell in the land that Jehovah has given to you and to your fathers, from of old and even for evermore.
6 Musatsatire milungu ina nʼkuyitumikira ndi kuyipembedza. Musapute mkwiyo wanga ndi mafano amene mwapanga ndi manja anu. Mukatero Ine sindidzakuwonongani.
And go not after other gods to serve them, and to worship them, and provoke me not to anger with the work of your hands. And I will do you no hurt.
7 “Koma inu simunandimvere,” akutero Yehova, “ndipo munaputa mkwiyo wanga ndi mafano amene munapanga ndi manja anu. Choncho munadziwononga nokha.”
Yet ye have not hearkened to me, says Jehovah, that ye may provoke me to anger with the work of your hands to your own hurt.
8 Nʼchifukwa chake Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Chifukwa simunamvere mawu anga,
Therefore thus says Jehovah of hosts: Because ye have not heard my words,
9 ndidzayitana mafuko onse akumpoto, pamodzi ndi mtumiki wanga Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni,” akutero Yehova, “ndipo adzathira nkhondo dziko lino ndi anthu ake pamodzi ndi mitundu yonse ya anthu ozungulira dzikoli. Ndidzawawononga kwathunthu ndi kuwasandutsa chinthu chochititsa mantha ndi chonyozeka, mpaka muyaya.
behold, I will send and take all the families of the north, says Jehovah, and Nebuchadrezzar the king of Babylon, my servant, and will bring them against this land, and against the inhabitants of it, and against all these nations round about. And I will utterly destroy them, and make them an astonishment, and a hissing, and perpetual desolations.
10 Ndidzathetsa mfuwu wachimwemwe ndi wachisangalalo, mawu a mkwati ndi mkwatibwi, phokoso la mphero ndi kuwala kwa nyale.
Moreover I will take from them the voice of mirth and the voice of gladness, the voice of the bridegroom and the voice of the bride, the sound of the millstones, and the light of the lamp.
11 Dziko lonse lidzakhala bwinja ndi chipululu, ndipo mitundu ina idzatumikira mfumu ya ku Babuloni kwa 70.
And this whole land shall be a desolation, and an astonishment. And these nations shall serve the king of Babylon seventy years.
12 “Koma zaka 70 zikadzatha, ndidzalanga mfumu ya ku Babuloni pamodzi ndi anthu ake, chifukwa cha zolakwa zawo,” akutero Yehova, “ndipo dziko lawo lidzakhala chipululu mpaka muyaya.
And it shall come to pass, when seventy years are accomplished, that I will punish the king of Babylon, and that nation, says Jehovah, for their iniquity, and the land of the Chaldeans, and I will make it desolate forever.
13 Ndidzachita zinthu zonse zimene ndinayankhula zotsutsa dzikolo, zonse zimene zalembedwa mʼbuku lino, ndiponso zonse zimene Yeremiya analosera zotsutsa anthu amenewa.
And I will bring upon that land all my words which I have pronounced against it, even all that is written in this book, which Jeremiah has prophesied against all the nations.
14 Iwo eni adzakhala akapolo a anthu a mitundu yochuluka ndi mafumu amphamvu. Ndidzawabwezera molingana ndi zochita zawo ndi ntchito za manja awo.”
For many nations and great kings shall make bondmen of them, even of them, and I will recompense them according to their deeds, and according to the work of their hands.
15 Yehova, Mulungu wa Israeli, anandiwuza kuti, “Tenga chikho ichi chodzaza ndi vinyo wa ukali wanga, ndipo ukamwetse anthu a mitundu yonse kumene ndikukutuma.
For thus says Jehovah, the God of Israel, to me: Take this cup of the wine of wrath at my hand, and cause all the nations, to whom I send thee, to drink it.
16 Akadzamwa adzayamba kudzandira ndi kuchita misala chifukwa cha nkhondo imene ndikuyitumiza pakati pawo.”
And they shall drink, and reel to and fro, and be mad, because of the sword that I will send among them.
17 Choncho ine ndinatenga chikhocho mʼdzanja la Yehova ndipo ndinamwetsa mitundu yonse ya anthu kumene Iye ananditumako:
Then I took the cup at Jehovah's hand, and made all the nations to drink, to whom Jehovah had sent me:
18 Anandituma ku Yerusalemu ndi ku mizinda ya Yuda, kwa mafumu ake ndi nduna zake kuti ndikawasandutse ngati bwinja ndi chinthu chochititsa mantha ndi chonyozeka ndiponso chotembereredwa, monga mmene alili lero lino.
Jerusalem, and the cities of Judah, and the kings of it, and the rulers of it, to make them a desolation, an astonishment, a hissing, and a curse, as it is this day,
19 Ananditumanso kwa Farao, mfumu ya ku Igupto, kwa atumiki ake, nduna zake ndi kwa anthu ake onse,
Pharaoh king of Egypt, and his servants, and his rulers, and all his people,
20 ndi kwa anthu ena onse a mitundu yachilendo; mafumu onse a ku Uzi; mafumu onse a Afilisti, a ku Asikeloni, ku Gaza, ku Ekroni ndiponso kwa anthu a ku chigwa chotsala cha Asidodi;
and all the mixed people, and all the kings of the land of the Uz, and all the kings of the Philistines, and Ashkelon, and Gaza, and Ekron, and the remnant of Ashdod,
21 Edomu, Mowabu ndi Amoni.
Edom, and Moab, and the sons of Ammon,
22 Ananditumanso kwa mafumu onse a ku Turo ndi ku Sidoni; kwa mafumu a kutsidya la nyanja;
and all the kings of Tyre, and all the kings of Sidon, and the kings of the isle which is beyond the sea,
23 ku Dedani, ku Tema, ku Buzi ndi kwa onse ometa chamʼmbali.
Dedan, and Tema, and Buz, and all who have the corners of their hair cut off,
24 Ananditumanso kwa mafumu onse a ku Arabiya ndi mafumu onse a anthu achilendo amene amakhala mʼchipululu.
and all the kings of Arabia, and all the kings of the mixed people who dwell in the wilderness,
25 Anandituma kwa mafumu onse a ku Zimuri, Elamu ndi Mediya;
and all the kings of Zimri, and all the kings of Elam, and all the kings of the Medes,
26 ndiponso kwa mafumu onse a kumpoto, akufupi ndi kutali omwe, mafumu onse a dziko lapansi. Ndipo potsiriza pake, idzamwenso ndi mfumu Sesaki.
and all the kings of the north, far and near, one with another, and all the kingdoms of the world, which are upon the face of the earth. And the king of Sheshach shall drink after them.
27 “Ndipo uwawuze kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Imwani, ledzerani ndipo musanze, mugwe osadzukanso chifukwa cha nkhondo imene ndikutumiza pakati panu.’
And thou shall say to them, Thus says Jehovah of hosts, the God of Israel: Drink ye, and be drunken, and spew, and fall, and rise no more, because of the sword which I will send among you.
28 Koma ngati akana kutenga chikhocho mʼdzanja lako ndi kumwa, uwawuze kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse akuti: Muyenera kumwa ndithu!’”
And it shall be, if they refuse to take the cup at thy hand to drink, then thou shall say to them, Thus says Jehovah of hosts: Ye shall surely drink.
29 Taonani, tsopano ndiyamba kulanga mzinda uno umene umadziwika ndi dzina langa. Kodi inu muganiza kuti simudzalangidwa? Ayi, simudzapulumuka chifukwa ndikutumiza nkhondo pa onse okhala pa dziko lapansi, akutero Yehova Wamphamvuzonse.
For, lo, I begin to work evil at the city which is called by my name, and should ye be utterly unpunished? Ye shall not be unpunished. For I will call for a sword upon all the inhabitants of the earth, says Jehovah of hosts.
30 “Tsopano iwe nenera mawu owatsutsa ndipo uwawuze kuti, “‘Yehova adzabangula kumwamba; mawu ake adzamveka ngati bingu kuchokera ku malo ake opatulika. Adzabangula mwamphamvu kukalipira dziko lake. Iye adzafuwula ngati anthu oponda mphesa, kukalipira onse amene akukhala pa dziko lapansi.
Therefore prophesy thou against them all these words, and say to them, Jehovah will roar from on high, and utter his voice from his holy habitation. He will mightily roar against his fold. He will give a shout, as those who tread grapes, against all the inhabitants of the earth.
31 Phokoso lalikulu lidzamveka mpaka kumalekezero a dziko lonse lapansi, chifukwa Yehova adzazenga mlandu anthu a mitundu yonse; adzaweruza mtundu wonse wa anthu ndipo oyipa adzawapha ndi lupanga,’” akutero Yehova.
A noise shall come even to the end of the earth, for Jehovah has a controversy with the nations. He will enter into judgment with all flesh. As for the wicked, he will give them to the sword, says Jehovah.
32 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Taonani! Mavuto akuti akachoka pa mtundu wina akukagwa pa mtundu wina; mphepo ya mkuntho ikuyambira ku malekezero a dziko.”
Thus says Jehovah of hosts: Behold, evil shall go forth from nation to nation, and a great tempest shall be raised up from the outermost parts of the earth.
33 Pa tsiku limenelo, onse ophedwa ndi Yehova adzangoti mbwee ponseponse, pa dziko lonse lapansi. Palibe amene adzawalire kapena kusonkhanitsa mitemboyo kuti ikayikidwe mʼmanda, koma idzakhala mbwee ngati ndowe.
And the slain of Jehovah shall be at that day from one end of the earth even to the other end of the earth. They shall not be lamented, nor gathered, nor buried; they shall be dung upon the face of the ground.
34 Khetsani misozi ndi kufuwula mwamphamvu, abusa inu; gubudukani pa fumbi, inu atsogoleri a nkhosa. Pakuti nthawi yanu yophedwa yafika; mudzagwa ndi kuphwanyika ngati mbiya yabwino kwambiri.
Wail, ye shepherds, and cry. And wallow, ye principal men of the flock. For the days of your slaughter and of your dispersions have fully come, and ye shall fall like a goodly vessel.
35 Abusa adzasowa kothawira, atsogoleri a nkhosa adzasowa malo opulumukira.
And the shepherds shall have no way to flee, nor the principal men of the flock to escape.
36 Imvani kulira kwa abusa, atsogoleri a nkhosa akulira, chifukwa Yehova akuwononga msipu wawo.
A voice of the cry of the shepherds, and the wailing of the principal men of the flock! For Jehovah lays waste their pasture.
37 Makola awo a nkhosa amene anali pamtendere adzasanduka bwinja chifukwa cha mkwiyo woopsa wa Yehova.
And the peaceable folds are brought to silence because of the fierce anger of Jehovah.
38 Ngati mkango, Yehova wasiya phanga lake, pakuti dziko lawo lasanduka chipululu chifukwa cha nkhondo ya owazunza ndiponso chifukwa cha mkwiyo woopsa wa Yehova.
He has left his covert as the lion. For their land has become an astonishment because of the fierceness of the oppressing sword, and because of his fierce anger.

< Yeremiya 25 >