< Yeremiya 22 >

1 Yehova anandiwuza kuti, “Pita ku nyumba ya mfumu ya ku Yuda ndipo ukayiwuze kuti,
Thus said Jehovah: Go down to the house of the king of Judah, and speak there this word,
2 ‘Imva mawu a Yehova, iwe mfumu ya ku Yuda, amene umakhala pa mpando waufumu wa Davide; iwe, nduna zako pamodzi ndi anthu ako amene amalowera pa zipata izi.
and say, Hear the word of Jehovah, O king of Judah, who sits upon the throne of David, thou, and thy servants, and thy people who enter in by these gates.
3 Yehova akuti, uziweruza molungama ndi mosakondera. Uzipulumutsa munthu amene walandidwa katundu mʼdzanja la womuzunza. Usazunze kapena kupondereza mlendo, ana amasiye kapena akazi amasiye. Usaphe munthu wosalakwa pa malo pano.
Thus says Jehovah: Execute ye justice and righteousness. And deliver him who is robbed out of the hand of the oppressor. And do no wrong. Do no violence to the sojourner, the fatherless, nor the widow, neither shed innocent blood in this place.
4 Pakuti ngati udzamvera malamulo awa, ndiye kuti mafumu onse okhala pa mpando waufumu wa Davide azidzalowabe pa zipata za nyumba yaufumu ino, atakwera magaleta ndi akavalo, iwowo pamodzi ndi nduna zawo ndi anthu awo.
For if ye do this thing indeed, then there shall enter in by the gates of this house kings sitting upon the throne of David, riding in chariots and on horses, he, and his servants, and his people.
5 Koma ngati sumvera malamulo awa, akutero Yehova, ndikulumbira pali Ine ndemwe kuti nyumba ino yaufumu idzasanduka bwinja.’”
But if ye will not hear these words, I swear by myself, says Jehovah, that this house shall become a desolation.
6 Pakuti zimene Yehova akunena za nyumba yaufumu ya mfumu ya ku Yuda ndi izi: “Ngakhale iwe uli ngati Giliyadi kwa Ine, ngati msonga ya phiri la Lebanoni, komabe ndidzakusandutsa chipululu, ngati mizinda yopanda anthu.
For thus says Jehovah concerning the house of the king of Judah: Thou are Gilead to me, and the head of Lebanon, yet surely I will make thee a wilderness, cities which are not inhabited.
7 Ndidzatuma anthu oti adzakuwononge, munthu aliyense ali ndi zida zake, ndipo adzadula mikungudza yako yokongola nadzayiponya pa moto.
And I will prepare destroyers against thee, each one with his weapons, and they shall cut down thy choice cedars, and cast them into the fire.
8 “Pamene anthu a mitundu ina adzadutsa pa mzinda umenewu adzafunsana kuti, ‘Chifukwa chiyani Yehova wachita chinthu chotere pa mzinda waukuluwu?’
And many nations shall pass by this city, and they shall say each man to his neighbor, Why has Jehovah done thus to this great city?
9 Ndipo yankho lake lidzakhala lakuti, ‘Chifukwa anasiya pangano limene anapangana ndi Yehova Mulungu wawo ndipo anapembedza ndi kutumikira milungu ina.’”
Then they shall answer, Because they forsook the covenant of Jehovah their God, and worshiped other gods, and served them.
10 Musayilire mfumu Yosiya, musamuyimbire nyimbo womwalirayo; mʼmalo mwake, mulire kwambiri chifukwa cha Yehowahazi amene wapita ku ukapolo, chifukwa sadzabwereranso kapena kuonanso dziko lake lobadwira.
Weep ye not for him who is dead, nor bemoan him. But weep greatly for him who goes away, for he shall return no more, nor see his native country.
11 Pakuti zimene Yehova akunena za Yehowahazi mwana wa Yosiya, amene anatenga mpando waufumu wa Yuda mʼmalo mwa abambo ake koma nʼkuwusiya ndi izi: “Iye sadzabwereranso.
For thus says Jehovah concerning Shallum the son of Josiah, king of Judah, who reigned instead of Josiah his father, and who went forth out of this place: He shall not return there any more.
12 Iyeyo adzafera ku ukapoloko. Sadzalionanso dziko lino.”
But in the place where they have led him captive, there he shall die, and he shall see this land no more.
13 “Tsoka kwa munthu womanga nyumba yake mopanda chilungamo, womanga zipinda zake zosanja monyenga, pogwiritsa ntchito abale ake mwathangata, osawapatsa malipiro a ntchito yawo.
Woe to him who builds his house by unrighteousness, and his chambers by injustice, who uses his neighbor's service without wages, and gives him not his hire,
14 Munthuyo amati, ‘Ndidzadzimangira nyumba yayikulu ya zipinda zikuluzikulu zamʼmwamba.’ Kotero ndidzapanga mazenera akuluakulu, ndi kukhomamo matabwa a mkungudza ndi kukongoletsa ndi makaka ofiira.
who says, I will build me a wide house and spacious chambers, and cuts out windows for himself, and it is overlaid with cedar, and painted with vermilion.
15 “Kodi kukhala ndi nyumba ya mkungudza wambiri zingachititse iwe kukhala mfumu? Ganiza za abambo ako. Suja anali ndi zonse zakudya ndi zakumwa. Abambo ako ankaweruza molungama ndi mosakondera, ndipo zonse zinkawayendera bwino.
Shall thou reign, because thou strive to excel in cedar? Did not thy father eat and drink, and do justice and righteousness? Then it was well with him.
16 Iye ankateteza anthu osauka ndi osowa, ndipo zonse zinkamuyendera bwino. Kodi zimenezi sindiye tanthauzo la kudziwa Ine?” akutero Yehova.
He judged the cause of the poor and needy man, then it was well. Was not this to know me? says Jehovah.
17 “Koma maso ako ndi mtima sizili penanso, koma zili pa phindu lachinyengo, pa zopha anthu osalakwa ndi pa kuzunza ndi pakulamulira mwankhanza.”
But thine eyes and thy heart are not but for thy covetousness, and for shedding innocent blood, and for oppression, and for violence, to do it.
18 Nʼchifukwa chake Yehova ponena za Yehoyakimu mwana wa Yosiya mfumu ya ku Yuda akuti, “Anthu sadzamulira maliro kapena kunena kuti, ‘Kalanga ine, mʼbale wanga! Kalanga ine mlongo wanga! Anthu ake sadzamulira maliro kuti, Kalanga ine, mbuye wathu! Taonani ulemerero wake wapita!’
Therefore thus says Jehovah concerning Jehoiakim the son of Josiah, king of Judah. They shall not lament for him, saying, Ah my brother! or, Ah sister! They shall not lament for him, saying Ah lord! or, Ah his glory!
19 Adzayikidwa ngati bulu, kuchita kumuguguza ndi kukamutaya kunja kwa zipata za Yerusalemu.”
He shall be buried with the burial of a donkey, drawn and cast forth beyond the gates of Jerusalem.
20 “Tsono inu anthu a ku Yerusalemu, pitani ku mapiri a Lebanoni kuti mukalire mofuwula kumeneko, mawu anu akamveke mpaka ku Basani. Mulire mofuwula muli ku Abarimu chifukwa abwenzi ako onse awonongeka.
Go up to Lebanon, and cry. And lift up thy voice in Bashan, and cry from Abarim. For all thy lovers are destroyed.
21 Ndinakuchenjezani pamene munali pa mtendere. Koma inu munati, ‘Sindidzamvera.’ Umu ndi mmene mwakhala mukuchitira kuyambira mukali aangʼono. Simunandimvere Ine.
I spoke to thee in thy prosperity, but thou said, I will not hear. This has been thy manner from thy youth, that thou obeyed not my voice.
22 Mphepo idzakuchotserani abusa anu onse, ndipo abwenzi anu adzatengedwa ku ukapolo. Pamenepo mudzachita manyazi ndi kunyozedwa chifukwa cha zoyipa zanu zonse.
The wind shall feed all thy shepherds, and thy loved ones shall go into captivity. Surely then thou shall be ashamed and confounded for all thy wickedness.
23 Inu amene mumakhala mʼnyumba ya ku Lebanoni, amene munamanga nyumba zanu pakati pa mikungudza, mudzabuwula kwambiri pamene zowawa zidzakugwerani, zonga za mkazi pa nthawi yake yochira!
O inhabitant of Lebanon, who makes thy nest in the cedars, how greatly to be pitied thou shall be when pangs come upon thee, the pain as of a woman in travail!
24 “Pali Ine wamoyo, akutero Yehova, ngakhale iwe, Yehoyakini mwana wa Yehoyakimu mfumu ya ku Yuda, ukanakhala ngati mphete ya ku dzanja langa lamanja, ndikanakuvula nʼkukutaya.
As I live, says Jehovah, though Coniah the son of Jehoiakim king of Judah were the signet upon my right hand, yet I would pluck thee from there,
25 Ndidzakupereka kwa amene akufuna kukupha, amene iwe umawaopa. Ndidzakupereka kwa Nebukadinezara, mfumu ya ku Babuloni ndi anthu ake.
and I will give thee into the hand of those who seek thy life, and into the hand of those of whom thou are afraid, even into the hand of Nebuchadrezzar king of Babylon, and into the hand of the Chaldeans.
26 Iwe pamodzi ndi amayi ako amene anakubereka ndidzakupititsani ku dziko lachilendo. Ngakhale inu simunabadwire kumeneko, komabe mudzafera komweko.
And I will cast thee out, and thy mother who bore thee, into another country where ye were not born, and there ye shall die.
27 Simudzabwereranso ku dziko limene mudzafuna kubwerera.”
But to the land to which their soul longs to return, there they shall not return.
28 Kodi Yehoyakini wakhala ngati mbiya yonyozeka, yosweka imene anthu sakuyifunanso? Kodi nʼchifukwa chake iye pamodzi ndi ana ake, achotsedwa nʼkutayidwa ku dziko limene iwo sakulidziwa?
Is this man Coniah a despised broken vessel? Is he a vessel in which none delights? Why are they cast out, he and his seed, and are cast into the land which they know not?
29 Iwe dziko, dziko, dziko, Imva mawu a Yehova!
O earth, earth, earth, hear the word of Jehovah.
30 Yehova akuti, “Munthu ameneyu mumutenge ngati wopanda ana, munthu amene sadzakhala wochita bwino pamoyo wake wonse, pakuti palibe ndi mmodzi yemwe mwa zidzukulu zake zomwe zidzachita bwino. Palibe amene adzathe kukhala pa mpando waufumu wa Davide ndi kulamulira Yuda.”
Thus says Jehovah: Write ye this man childless, a man who shall not prosper in his days. For no more shall a man of his seed prosper, sitting upon the throne of David, and ruling in Judah.

< Yeremiya 22 >