< Yeremiya 24 >

1 Nebukadinezara, mfumu ya ku Babuloni anatenga ukapolo Yekoniya mwana wa Yehoyakimu mfumu ya ku Yuda pamodzi ndi nduna zake, anthu aluso ndi akatswiri a ku Yuda ndi kupita nawo ku Babuloni. Pambuyo pake Yehova anandionetsa madengu awiri a nkhuyu atayikidwa pa khomo pa Nyumba ya Yehova.
Jehovah showed me, and, behold, two baskets of figs set before the temple of Jehovah, after Nebuchadrezzar king of Babylon had carried away captive Jeconiah the son of Jehoiakim, king of Judah, and the rulers of Judah, with the craftsmen and smiths, from Jerusalem, and had brought them to Babylon.
2 Mʼdengu limodzi munali nkhuyu zabwino kwambiri, ngati nkhuyu zoyambirira kucha. Mʼdengu linalo munali nkhuyu zoyipa kwambiri zosati nʼkudya.
One basket had very good figs, like the figs that are first ripe, and the other basket had very bad figs, which could not be eaten they were so bad.
3 Yehova anandifunsa kuti, “Yeremiya, kodi ukuona chiyani?” Ndinayankha kuti, “Ndikuona nkhuyu zabwino kwambiri ndi nkhuyu zoyipa zosati nʼkudya.”
Then Jehovah said to me, What do thou see, Jeremiah? And I said, Figs. The good figs, very good, and the bad, very bad, that cannot be eaten they are so bad.
4 Tsono Yehova anandiwuza kuti,
And the word of Jehovah came to me, saying,
5 “Ine Yehova, Mulungu wa Israeli ndikuti, ‘Anthu a ku Yuda amene ndinawachotsa ku malo ano nʼkupita nawo ku ukapolo ku dziko la Ababuloni ndikuwafanizira ndi nkhuyu zabwinozi.
Thus says Jehovah, the God of Israel: Like these good figs, so I will regard the captives of Judah, whom I have sent out of this place into the land of the Chaldeans, for good.
6 Ndidzaonetsesa kuti ndiwachitire zabwino ndipo ndidzabwera nawonso ku dziko lino. Ndidzawamanga osati kuwapasula; ndidzawadzala osati kuwazula.
For I will set my eyes upon them for good, and I will bring them again to this land. And I will build them, and not pull them down, and I will plant them, and not pluck them up.
7 Ndidzawapatsa mtima woti andidziwe kuti ndine Yehova. Adzakhala anthu anga ndipo Ine ndidzakhala Mulungu wawo, chifukwa adzabwerera kwa Ine ndi mtima wawo wonse.
And I will give them a heart to know me, that I am Jehovah. And they shall be my people, and I will be their God, for they shall return to me with their whole heart.
8 “‘Koma monga nkhuyu zoyipa zija, zomwe ndi zoyipa kwambiri zosati nʼkudya,’ Yehova akuti, ‘ndi mmene ndidzalangire Zedekiya mfumu ya ku Yuda, nduna zake pamodzi ndi otsala a mu Yerusalemu, kaya adzakhala ali mʼdziko muno kapena mʼdziko la Igupto.
And as the bad figs, which cannot be eaten they are so bad, surely thus says Jehovah: So will I give up Zedekiah the king of Judah, and his rulers, and the residue of Jerusalem, who remain in this land, and those who dwell in the land of Egypt.
9 Ndidzawasandutsa chinthu chonyansa kwa maufumu onse a dziko lapansi, chinthu chonyozeka ndi chopandapake, chinthu chochitidwa chipongwe ndi chotembereredwa kulikonse kumene ndidzawabalalitsira.
I will even give them up to be tossed to and fro among all the kingdoms of the earth for evil, to be a reproach and a proverb, a taunt and a curse, in all places where I shall drive them.
10 Ndidzawatumizira nkhondo, njala ndi mliri mpaka atawonongedwa mʼdziko limene ndinawapatsa iwo ndi makolo awo.’”
And I will send the sword, the famine, and the pestilence, among them, till they be consumed from off the land that I gave to them and to their fathers.

< Yeremiya 24 >