< Yesaya 49 >

1 Mverani Ine, inu anthu a pa zilumba tcherani khutu, inu anthu a mayiko akutali: Yehova anandiyitana ine ndisanabadwe, ananditchula dzina ndili mʼmimba ya amayi anga.
Listen, O isles, to me, and hearken, ye peoples from far. Jehovah has called me from the womb. From the bowels of my mother he has made mention of my name.
2 Iye anasandutsa pakamwa panga kukhala ngati lupanga lakuthwa, anandibisa mu mthunzi wa dzanja lake; Iye anandisandutsa ngati muvi wakuthwa ndipo anandibisa mʼchimake.
And he has made my mouth like a sharp sword. He has hid me in the shadow of his hand, and he has made me a polished shaft. He has kept me close in his quiver.
3 Iye anati kwa ine, “Ndiwe mtumiki wanga, Israeli. Anthu adzanditamanda chifukwa cha iwe.”
And he said to me, Thou are my servant, Israel, in whom I will be glorified.
4 Koma Ine ndinati, “Ine ndinkaganiza kuti ndinagwira ntchito ndi kuwononga mphamvu zanga pachabe, koma ayi, zondiyenera zili mʼmanja a Yehova, ndipo mphotho yanga ili mʼmanja mwa Mulungu wanga.”
But I said, I have labored in vain. I have spent my strength for nothing and vanity. Yet surely the justice due to me is with Jehovah, and my recompense with my God.
5 Yehova anandiwumba ine mʼmimba mwa amayi anga kuti ndikhale mtumiki wake kuti ndibweze fuko la Yakobo kwa Iye ndi kusonkhanitsa Israeli kwa Iye, choncho ndimalemekezeka mʼmaso mwa Yehova, ndipo ndimapeza mphamvu mwa Mulungu wanga.
And now says Jehovah who formed me from the womb to be his servant, to bring Jacob again to him, and that Israel be gathered to him (for I am honorable in the eyes of Jehovah, and my God has become my strength),
6 Yehovayo tsono akuti, “Nʼchinthu chochepa kwambiri kwa iwe kuti ukhale mtumiki wanga, kuti udzutse mafuko a Yakobo ndi kuwabweretsa kwawo Aisraeli amene anapulumuka. Choncho iwe udzakhala ngati chowunikira, udzafikitsa uthenga wa chipulumutso changa ku mathero a dziko lapansi.”
yea, he says, It is too light a thing that thou should be my servant to raise up the tribes of Jacob, and to restore the preserved of Israel. I will also give thee for a light to the Gentiles, that thou may be my salvation to the end of the earth.
7 Yehova Mpulumutsi ndi Woyerayo wa Israeli akuyankhula, Woyerayo wa Israeli akunena, amene mitundu ya anthu inamuda, amenenso anali kapolo wa mafumu ankhanza uja kuti, “Mafumu adzaona ntchito ya chipulumutso changa ndipo adzayimirira. Akalonga nawonso adzagwada pansi. Zimenezi zidzachitika chifukwa cha Yehova amene ndi wokhulupirika ndi Woyerayo wa Israeli amene wakusankha iwe.”
Thus says Jehovah, the Redeemer of Israel, and his Holy One, to him whom man despises, to him whom the nation abhors, to a servant of rulers. Kings shall see and arise, rulers, and they shall worship, because of Jehovah who is faithful, even the Holy One of Israel, who has chosen thee.
8 Yehova akuti, “Pa nthawi imene ndinakukomera mtima ndinakuyankha, ndipo pa tsiku lachipulumutso ndinakuthandiza; ndinakusunga ndi kukusandutsa kuti ukhale pangano kwa anthu, kuti dziko libwerere mwakale ndi kuti cholowa changa chowonongeka chija ndichigawegawenso.
Thus says Jehovah, In an acceptable time I have heard thee, and in a day of salvation I have helped thee. And I will preserve thee, and give thee for a covenant of the people, to raise up the land, to make them inherit the desolate heritages,
9 Ndidzawuza a mʼndende kuti atuluke ndi a mu mdima kuti aonekere poyera. “Adzapeza chakudya mʼmphepete mwa njira ndi msipu pa mʼmalo owuma.
saying to those who are bound, Go forth; to those who are in darkness, Show yourselves. They shall feed in the ways, and their pasture shall be on all bare heights.
10 Iwo sadzamva njala kapena ludzu, kutentha kwa mʼchipululu kapena dzuwa silidzawapsereza; chifukwa Iye amene amawachitira chifundo adzawatsogolera ndi kuwaperekeza ku akasupe a madzi.
They shall not hunger nor thirst, neither shall the heat nor sun smite them. For he who has mercy on them will lead them. He will guide them even by springs of water.
11 Mapiri anga onse ndidzawasandutsa njira yoyendamo, ndipo misewu yanga yayikulu ndidzayikweza.
And I will make all my mountains a way, and my highways shall be exalted.
12 Taonani, anthu anga adzachokera kutali, ena kumpoto, ena kumadzulo, enanso adzachokera ku chigawo cha Asuwani.”
Lo, these shall come from far, and, lo, these from the north and from the west, and these from the land of Sinim.
13 Imbani mwachimwemwe, inu zolengedwa zamlengalenga; kondwera, iwe dziko lapansi; imbani nyimbo inu mapiri! Pakuti Yehova watonthoza mtima anthu ake, ndipo wachitira chifundo anthu ake ovutika.
Sing, O heavens, and be joyful, O earth, and break forth into singing, O mountains. For Jehovah has comforted his people, and will have compassion upon his afflicted.
14 Koma Ziyoni anati, “Yehova wandisiya, Ambuye wandiyiwala.”
But Zion said, Jehovah has forsaken me, and the Lord has forgotten me.
15 “Kodi amayi angathe kuyiwala mwana wawo wakubere ndi kusachitira chifundo mwana amene anabereka iwo eni? Ngakhale iye angathe kuyiwala, Ine sindidzakuyiwala iwe!
Can a woman forget her sucking child, that she should not have compassion on the son of her womb? Yea, these may forget, yet I will not forget thee.
16 Taona, ndakulemba iwe mʼzikhantho zanga; makoma ako ndimawaona nthawi zonse.
Behold, I have engraved thee upon the palms of my hands. Thy walls are continually before me.
17 Amisiri odzakumanganso akubwerera mofulumira, ndipo amene anakupasula akuchokapo.
Thy sons make haste. Thy destroyers and those who made thee waste shall go forth from thee.
18 Kweza maso ako ndipo uyangʼaneyangʼane ana ako onse akusonkhana ndipo akubwera kwa iwe. Yehova akuti, ‘Ine Yehova wamoyo, anthu ako adzakhala ngati chinthu chodzikongoletsa chimene mkwatibwi wavala pa mkono pake.’
Lift up thine eyes round about, and behold. All these gather themselves together, and come to thee. As I live, says Jehovah, thou shall surely clothe thee with them all, as with an ornament, and gird thyself with them, like a bride.
19 “Ngakhale unasanduka bwinja ndi kuwonongedwa ndipo dziko lako ndi kusakazidwa, chifukwa cha kuchuluka kwa anthu malo okhalamo adzakhala operewera ndipo amene anakuwononga iwe aja adzakhala kutali.
For, as for thy waste and thy desolate places, and thy land that has been destroyed, surely now thou shall be too narrow for the inhabitants, and those who swallowed thee up shall be far away.
20 Ana obadwa nthawi yako yachisoni adzanena kuti, ‘Malo ano atichepera, tipatse malo ena woti tikhalemo.’
The sons of thy bereavement shall yet say in thine ears, The place is too narrow for me. Give a place to me that I may dwell.
21 Tsono iwe udzadzifunsa kuti, ‘Kodi ndani anandiberekera ana amenewa? Ana anga onse anamwalira ndipo sindinathenso kukhala ndi ana ena; ndinapita ku ukapolo ndipo ndinachotsedwa. Ndani anawalera ana amenewa? Ndinatsala ndekha, nanga awa, achokera kuti?’”
Then thou shall say in thy heart, Who has begotten these for me, seeing I have been bereaved of my sons, and am solitary, an exile, and wandering to and fro? And who has brought up these? Behold, I was left alone, these, where were they?
22 Zimene Ambuye Yehova akunena ndi izi, “Taonani, Ine ndidzakodola Anthu a mitundu ina kuti abwere. Ndidzawakwezera anthu a mitundu ina mbendera yanga kuti abwere. Tsono adzabwera ndi ana ako aamuna atawanyamula mʼmanja mwawo ndipo adzanyamula ana ako aakazi pa mapewa awo.
Thus says the lord Jehovah: Behold, I will lift up my hand to the nations, and set up my ensign to the peoples. And they shall bring thy sons in their bosom, and thy daughters shall be carried upon their shoulders.
23 Mafumu adzakhala abambo wongokulera ndipo akazi a mafumu adzakhala amayi wongokulera. Iwo adzagwetsa nkhope zawo pansi. Ndiye inu mudzazindikira kuti Ine ndine Yehova; iwo amene amadalira Ine sadzakhumudwa.”
And kings shall be thy nursing fathers, and their queens thy nursing mothers. They shall bow down to thee with their faces to the earth, and lick the dust of thy feet. And thou shall know that I am Jehovah, and those who wait for me shall not be put to shame.
24 Kodi mungathe kulanda anthu ankhondo zofunkha zawo, kapena kupulumutsa anthu ogwidwa mʼdzanja la munthu wankhanza?
Shall the prey be taken from the mighty, or the lawful captives be delivered?
25 Koma zimene Yehova akunena ndi izi, “Ankhondo adzawalanda amʼndende awo, ndipo munthu woopsa adzamulanda zofunkha zawo; ndidzalimbana ndi amene amalimbana nanu, ndipo ndidzapulumutsa ana anu.
But thus says Jehovah, Even the captives of the mighty shall be taken away, and the prey of the terrible shall be delivered. For I will contend with him who contends with thee, and I will save thy sons.
26 Anthu amene anakuponderezani adzadya mnofu wawo omwe; adzamwa magazi awo omwe ngati aledzera ndi vinyo. Zikadzatero anthu onse adzadziwa kuti Ine Yehova, ndine Mpulumutsi wanu, Momboli wanu, Wamphamvu wa Yakobo.”
And I will feed those who oppress thee with their own flesh. And they shall be drunken with their own blood, as with sweet wine. And all flesh shall know that I, Jehovah, am thy Savior and thy Redeemer, the Mighty One of Jacob.

< Yesaya 49 >