< Yesaya 34 >

1 Inu anthu a mitundu yonse, bwerani pafupi kuti mumve: tcherani khutu, inu anthu a mitundu ina yonse: Limvetsere dziko lapansi pamodzi ndi zonse zili mʼmenemo, dziko lonse pamodzi ndi zonse zochokera mʼmenemo!
Come near, ye nations, to hear. And hearken, ye peoples. Let the earth hear, and the fullness thereof, the world, and all things that come forth from it.
2 Yehova wayipidwa ndi anthu a mitundu yonse; wapsera mtima magulu awo onse ankhondo. Iye adzawawononga kotheratu, nawapereka kuti aphedwe.
For Jehovah has indignation against all the nations, and wrath against all their host. He has utterly destroyed them. He has delivered them to the slaughter.
3 Anthu awo ophedwa adzatayidwa kunja, mitembo yawo idzawola ndi kununkha; mapiri adzafiira ndi magazi awo.
Their slain also shall be cast out. And the stench of their dead bodies shall come up, and the mountains shall be melted with their blood.
4 Dzuwa, mwezi ndi nyenyezi zidzasungunuka ndipo mlengalenga mudzakulungidwa ngati chipepala; nyenyezi zonse zidzayoyoka ngati masamba ofota a mphesa, ngati masamba onyala a mtengo wa mkuyu.
And all the host of heaven shall be dissolved, and the heavens shall be rolled together as a scroll. And all their host shall fade away as the leaf fades from off the vine, and as a fading leaf from the fig tree.
5 Yehova akuti, “Lupanga langa lakhutiratu magazi kumwamba; taonani, likutsika kudzalanga anthu a ku Edomu, anthu amene ndawawononga kotheratu.”
For my sword has drunk its fill in heaven. Behold, it shall come down upon Edom, and upon the people of my curse, to judgment.
6 Lupanga la Yehova lakhuta magazi, lakutidwa ndi mafuta; magazi a ana ankhosa onenepa ndi ambuzi, mafuta a ku impsyo za nkhosa zazimuna. Pakuti Yehova ali ndi nsembe mu Bozira ndiko kuphedwa kwa anthu ambiri mʼdziko la Edomu.
The sword of Jehovah is filled with blood. It is made fat with fatness, with the blood of lambs and goats, with the fat of the kidneys of rams, for Jehovah has a sacrifice in Bozrah, and a great slaughter in the land of Edom.
7 Pamodzi ndi anthuwo zidzaphedwanso njati, ngʼombe zazimuna zazingʼono ndi zazikulu zomwe. Dziko lawo lidzakhala magazi okhaokha, ndipo nthaka idzakutidwa ndi mafuta.
And the wild oxen shall come down with them, and the bullocks with the bulls. And their land shall be drunken with blood, and their dust made fat with fatness.
8 Iyi ndi nthawi imene Yehova adzalipsira ndi kulanga adani a Ziyoni.
For Jehovah has a day of vengeance, a year of recompense for the cause of Zion.
9 Madzi a mʼmitsinje ya Edomu adzasanduka phula, ndipo fumbi lake lidzasanduka sulufule; dziko lake lidzasanduka phula lamoto!
And the streams of Edom shall be turned into pitch, and the dust of it into brimstone. And the land thereof shall become burning pitch.
10 Motowo sudzazimitsidwa usiku ndi usana; utsi wake udzafuka kosalekeza. Dzikolo lidzakhala chipululu pa mibado ndi mibado; palibe ndi mmodzi yemwe amene adzadutsemo.
It shall not be quenched night nor day. The smoke of it shall go up forever. From generation to generation it shall lie waste. None shall pass through it forever and ever.
11 Mʼdzikomo mudzakhala akabawi ndi anungu; amantchichi ndi akhwangwala adzapanga zisa zawo mʼmenemo. Mulungu adzatambalitsa pa Edomu chingwe choyezera cha chisokonezo ndi chingwe chowongolera cha chiwonongeko.
But the pelican and the porcupine shall possess it. And the owl and the raven shall dwell in it. And he will stretch over it the line of confusion, and the plummet of emptiness.
12 Anthu olemekezeka ake sadzatchedwanso mfumu kumeneko; akalonga ake onse adzachotsedwa.
They shall call the nobles of it to the kingdom, but none shall be there. And all its rulers shall be nothing.
13 Minga idzamera mʼnyumba zake zankhondo zotetezedwa, khwisa ndi mitungwi zidzamera mʼmalinga ake. Ankhandwe azidzadya mʼmenemo; malo okhalamo akadzidzi.
And thorns shall come up in its palaces, nettles and thistles in the fortresses of it. And it shall be a habitation of jackals, a court for ostriches.
14 Avumbwe adzakumana ndi afisi, ndipo zirombo za mʼchipululu zizidzayitanizana. Kumeneko kudzafikanso mizimu yoyipa ndi kupeza malo opumulirako.
And the wild beasts of the desert shall meet with the wolves. And the wild goat shall cry to his fellow. Yea, the screech owl shall settle there, and shall find her a place of rest.
15 Kadzidzi adzamangako chisa chake nʼkuyikirako mazira, adzaswa ana ake ndi kusamalira ana ake mu mthunzi wa mapiko ake; akamtema adzasonkhananso kumeneko, awiriawiri.
There the dart-snake shall make her nest, and lay, and hatch, and gather under her shade. Yea, there the vultures shall be gathered, each one with her mate.
16 Funafunani mʼbuku la Yehova ndi kuwerenga: mwa zolengedwazi palibe chimene chidzasowa; sipadzakhala nʼchimodzi chomwe chopanda chinzake. Pakuti Yehova walamula kuti zitero, ndipo Mzimu wake udzawasonkhanitsa pamodzi.
Seek ye out of the book of Jehovah, and read. No one of these shall be missing. None shall want her mate. For my mouth, it has commanded, and his Spirit, it has gathered them.
17 Yehova wagawa dziko lawo; wapatsa chilichonse chigawo chake. Dziko lidzakhala lawo mpaka muyaya ndipo zidzakhala mʼmenemo pa mibado yonse.
And he has cast the lot for them, and his hand has divided it to them by line. They shall possess it forever. From generation to generation they shall dwell therein.

< Yesaya 34 >