< Yesaya 33 >

1 Tsoka kwa iwe, iwe wowonongawe, amene sunawonongedwepo! Tsoka kwa iwe, iwe mthirakuwiri, iwe amene sunanyengedwepo! Iwe ukadzaleka kuwononga, udzawonongedwa, ukadzasiya umʼthirakuwiri, adzakuwononga, ndipo ukadzaleka kuchita zachinyengo adzakunyenga.
Woe to thee who destroys, and thou were not destroyed, and deal treacherously, and they did not deal treacherously with thee! When thou have ceased to destroy, thou shall be destroyed, and when thou have made an end of dealing treacherously, they shall deal treacherously with thee.
2 Inu Yehova, mutikomere mtima ife; tikulakalaka Inu. Tsiku ndi tsiku mutitchinjirize ndi mkono wanu, ndipo mutipulumutse pa nthawi ya masautso.
O Jehovah, be gracious to us, we have waited for thee. Be thou our arm every morning, also our salvation in the time of trouble.
3 Mukatulutsa liwu lanu longa bingu mitundu ya anthu imathawa; pamene Inu mwadzambatuka mitundu ya anthu imabalalika.
At the noise of the tumult the peoples have fled. At the lifting up of thyself the nations are scattered.
4 Zofunkha za ku nkhondo za mitundu ina Aisraeli adzazisonkhanitsa ngati mmene limachitira dzombe. Iwo adzalumphira zofunkhazo monga mmene limachitira dzombe.
And your spoil shall be gathered as the caterpillar gathers. As locusts leap, men shall leap upon it.
5 Yehova wakwezeka kwambiri pakuti amakhala pamwamba pa zonse adzadzaza Ziyoni ndi chilungamo ndi chipulumutso.
Jehovah is exalted, for he dwells on high. He has filled Zion with justice and righteousness.
6 Iye adzakupatsani mtendere pa nthawi yanu, adzakupatsani chipulumutso chochuluka, nzeru zambiri ndi chidziwitso chochuluka; kuopa Yehova ngati madalitso.
And there shall be stability in thy times, abundance of salvation, wisdom, and knowledge. The fear of Jehovah is thy treasure.
7 Taonani, anthu awo amphamvu akulira mofuwula mʼmisewu; akazembe okhazikitsa mtendere akulira kwambiri.
Behold, their valiant ones cry outside. The ambassadors of peace weep bitterly.
8 Mʼmisewu yayikulu mulibe anthu, mʼmisewu mulibe anthu a paulendo. Mdaniyo ndi wosasunga pangano. Iye amanyoza mboni. Palibe kulemekezana.
The highways lie waste. The wayfaring man ceases. The enemy has broken the covenant. He has despised the cities. He does not regard man.
9 Dziko likulira ndipo likunka likutha. Nkhalango ya Lebanoni ikuchita manyazi, yafota. Chigwa cha chonde cha Saroni chasanduka chachidalala. Masamba a mitengo ya ku Basani ndi Karimeli akuyoyoka.
The land mourns and languishes. Lebanon is confounded and withers away. Sharon is like a desert, and Bashan and Carmel shake off their leaves.
10 Yehova akunena kuti, “Tsopano ndidzadzambatuka ndipo ndidzaonetsa mphamvu zanga, ndipo ndidzakwezedwa.
Now I will arise, says Jehovah. Now I will lift up myself. Now I will be exalted.
11 Zolingalira zanu nʼzachabechabe ngati udzu wamanyowa. Mpweya wamoto udzakupserezani.
Ye shall conceive chaff. Ye shall bring forth stubble. Your breath is a fire that shall devour you.
12 Anthu a mitundu ina adzatenthedwa ngati miyala ya njereza; ndi ngati minga yodulidwa.”
And the peoples shall be as the burnings of lime, as thorns cut down that are burned in the fire.
13 Inu amene muli kutali, imvani zimene ndachita; inu amene muli pafupi, dziwani mphamvu zanga
Hear, ye who are far off, what I have done, and ye who are near, acknowledge my might.
14 Mu mzinda wa Ziyoni anthu ochimwa agwidwa ndi mantha; anthu osapembedza Mulungu akunjenjemera: Iwo akunena kuti, “Ndani wa ife angathe kukhala mʼmoto wonyeketsa? Ndani wa ife angathe kukhala moto wosatha?”
The sinners in Zion are afraid. Trembling has seized the profane. Who among us can dwell with the devouring fire? Who among us can dwell with everlasting burnings?
15 Angathe kuti ndi amene amachita zolungama ndi kuyankhula zoona, amene amakana phindu lolipeza monyenga ndipo salola manja ake kulandira ziphuphu, amene amatseka makutu ake kuti angamve mawu opangana kupha anzawo ndipo amatsinzina kuti angaone zoyipa.
He who walks righteously, and speaks uprightly. He who despises the gain of oppressions, who shakes away his hands from taking a bribe, who stops his ears from hearing of blood, and shuts his eyes from looking upon evil.
16 Munthu wotere ndiye adzakhale pa nsanja, kothawira kwake kudzakhala mʼmalinga a mʼmapiri. Azidzalandira chakudya chake ndipo madzi sadzamusowa.
He shall dwell on high. His place of defense shall be the munitions of rocks. His bread shall be given. His waters shall be sure.
17 Nthawi imeneyo maso a ana adzaona mfumu ya maonekedwe wokongola ndi kuona dziko lotambasukira kutali.
Thine eyes shall see the king in his beauty. They shall behold a land that reaches afar.
18 Mu mtima mwanu muzidzalingalira zoopsa zinachitika kale zija: “Ali kuti mkulu wa Asilikali uja? Ali kuti wokhometsa misonkho uja? Ali kuti mkulu woyangʼanira nsanja?”
Thy heart shall muse on the terror. Where is he who counted? Where is he who weighed the tribute? Where is he who counted the towers?
19 Simudzawaonanso anthu odzikuza aja, anthu aja achiyankhulo chosadziwika, chachilendo ndi chosamveka.
Thou shall not see the fierce people, a people of a deep speech that thou cannot comprehend, of a strange tongue that thou cannot understand.
20 Taonani Ziyoni, mzinda wa zikondwerero zachipembedzo chathu; maso anu adzaona Yerusalemu, mzinda wamtendere, tenti imene sidzachotsedwa, zikhomo zake sizidzazulidwa, kapena zingwe zake kuduka.
Look upon Zion, the city of our solemnities. Thine eyes shall see Jerusalem a quiet habitation, a tent that shall not be removed. The stakes of which shall never be plucked up, nor shall any of the cords of it be broken.
21 Kumeneko Yehova adzaonetsa ulemerero wake ndipo mzindawo udzakhala kasupe wa mitsinje yayikulu. Ngalawa za zopalasa sizidzapitamo, sitima zapamadzi zikuluzikulu sizidzayendamo.
But Jehovah will be with us there in majesty. A place of broad rivers and streams, in which shall go no galley with oars, nor shall a gallant ship pass thereby.
22 Pakuti Yehova ndi woweruza wathu, Yehova ndiye wotilamulira, Yehova ndiye mfumu yathu; ndipo ndiye amene adzatipulumutse.
For Jehovah is our judge. Jehovah is our lawgiver. Jehovah is our king, he will save us.
23 Zingwe za sitima zapamadzi za adani athu zamasuka, sizikutha kulimbitsa mlongoti wake, matanga ake sakutheka kutambasuka. Ngakhale tidzagawana zofunkha zochuluka kwambiri ndipo ngakhale olumala adzatenga zofunkhazo.
Thy tacklings are loosed. They could not strengthen the foot of their mast. They could not spread the sail. Then the prey of a great spoil was divided. The lame took the prey.
24 Palibe ndi mmodzi yemwe wokhala mʼZiyoni adzanene kuti, “Ndikudwala” ndipo anthu onse okhala mʼmenemo machimo awo adzakhululukidwa.
And the inhabitant shall not say, I am sick. The people who dwell in it shall be forgiven their iniquity.

< Yesaya 33 >