< Yesaya 29 >

1 Tsoka kwa iwe, Arieli, Arieli, mzinda umene Davide anakhazikitsamo zithando za nkhondo! Papite chaka chimodzi kapena ziwiri ndipo masiku a zikondwerero zanu azipitirirabe ndithu.
Ho Ariel, Ariel, the city where David encamped! Add ye year to year. Let the feasts come round.
2 Komatu Ine ndidzathira nkhondo Arieli ndipo kudzakhala kulira ndi kudandaula, mzindawo udzasanduka ngati ngʼanjo ya guwa lansembe.
Then I will distress Ariel, and there shall be mourning and lamentation, and she shall be to me as Ariel.
3 Ine ndidzamanga misasa ya nkhondo kulimbana ndi mzindawo; ndidzakuzungulira ndi nsanja za nkhondo ndi kumanga mitumbira yanga ya nkhondo kulimbana nawe.
And I will encamp against thee round about, and will lay siege against thee with posted troops. And I will raise siege works against thee.
4 Utagwetsedwa pansi, iwe udzayankhula kuchokera mʼnthaka, mawu ako adzatuluka uli mʼfumbi, adzamveka ngati a mzukwa. Mawu ako adzamveka ngati onongʼona kuchokera mʼfumbi.
And thou shall be brought down, and shall speak out of the ground. And thy speech shall be low out of the dust, and thy voice shall be as of he who has a familiar spirit, out of the ground. And thy speech shall whisper out of the dust.
5 Koma chigulu cha adani ako chidzasanduka chifwirimbwiti. Chigulu cha ankhondo achilendo chidzabalalika ngati mungu wowuluzika ndi mphepo. Mwadzidzidzi ndi mosayembekezereka,
But the multitude of thy foes shall be like small dust, and the multitude of the terrible ones as chaff that passes away. Yea, it shall be in an instant suddenly.
6 Yehova Wamphamvuzonse adzabwera ndi mabingu ndi chivomerezi ndi phokoso lalikulu, kamvuluvulu ndi namondwe ndi malawi a moto wonyeketsa.
She shall be visited by Jehovah of hosts with thunder, and with earthquake, and great noise, with whirlwind and tempest, and the flame of a devouring fire.
7 Tsono chigulu chankhondo cha mitundu ina yonse chimene chikulimbana ndi mzinda wa Arieli nʼkumathira nkhondo mzindawo, malinga ake ndi kuwuzinga, chigulu chonsecho chidzazimirira ngati maloto, gati zinthu zoziona mʼmasomphenya usiku.
And the multitude of all the nations that fight against Ariel, even all that fight against her and her stronghold, and that distress her, shall be as a dream, a vision of the night.
8 Chidzakhala ngati munthu wanjala wolota akudya, koma podzuka ali nayobe njala; kapena ngati munthu waludzu wolota akumwa, koma podzuka, ali nalobe ludzu, kummero kwake kuli gwaa. Izi zidzachitika pamene chigulu cha nkhondo cha mitundu ina yonse chikunthira nkhondo Phiri la Ziyoni.
And it shall be as when a hungry man dreams, and, behold, he eats. But he awakes, and his soul is empty. Or as when a thirsty man dreams, and, behold, he drinks. But he awakes, and, behold, he is faint, and his soul has appetite. So shall the multitude of all the nations be that fight against mount Zion.
9 Pitirizani kuledzera ndipo mudzakhala opusa. Dzitsekeni mʼmaso ndipo mukhale osapenya, ledzerani, koma osati ndi vinyo, dzandirani, koma osati ndi mowa.
Tarry ye and wonder, take your pleasure and be blind. They are drunken, but not with wine. They stagger, but not with strong drink.
10 Yehova wakugonetsani tulo tofa nato. Watseka maso anu, inu aneneri; waphimba mitu yanu, inu alosi.
For Jehovah has poured out upon you the spirit of deep sleep, and has closed your eyes. The prophets, and your heads, the seers, he has covered.
11 Kwa inu mawu onsewa ali ngati buku lotsekedwa, ndipo ngati lipatsidwa kwa wina wodziwa kuwerenga ndi kunena kuti, “Chonde tawerengani bukuli,” iye adzati, “Sindingathe popeza ndi lomatidwa.”
And all vision has become to you as the words of a book that is sealed, which men deliver to a man who is learned, saying, Read this, I pray thee. And he says, I cannot, for it is sealed.
12 Kapena ngati lipatsidwa kwa amene sadziwa kuwerenga ndi kunena kuti, “Chonde werenga bukuli,” iye adzayankha kuti, “Ine sindidziwa kuwerenga.”
And the book is delivered to him who is not learned, saying, Read this, I pray thee. And he says, I am not learned.
13 Ambuye akuti, “Anthu awa amandipembedza Ine ndi pakamwa pawo, ndi kundilemekeza Ine ndi milomo yawo, koma mitima yawo ili kutali ndi Ine. Kundipembedza kwawo ndi kwa chiphamaso. Amandipembedza motsata malamulo a anthu amene anaphunzitsidwa.
And the Lord said, Inasmuch as this people draw near me with their mouth, and honor me with their lips, but have removed their heart far from me, but in vain they worship me, teaching the commandments and doctrines of men.
14 Nʼchifukwa chakenso Ine ndidzapitirira kuwachitira ntchito zodabwitsa; nzeru za anthu anzeru zidzatha, luntha la anthu aluntha Ine ndidzalinyoza.”
Therefore, behold, I will proceed to do a marvelous work among this people, even a marvelous work and a wonder. I will destroy the wisdom of the wise, and the understanding of their prudent men shall be hidden.
15 Tsoka kwa amene amayesetsa kubisira Yehova maganizo awo, amene amachita ntchito zawo mu mdima nʼkumanena kuti, “Ndani amene akundiona kapena ndani akudziwa zimene ndikuchita?”
Woe to those who hide deep their counsel from Jehovah, and whose works are in the dark, and who say, Who sees us? and, Who knows us?
16 Inu mumazondotsa zinthu ngati kuti dothi lasanduka wowumba mbiya. Kodi chinthu chopangidwa chingawuze wochipanga kuti “Sunandipange ndi iwe?” Kapena mʼphika kunena kwa amene anawuwumba kuti, “Iwe sudziwa chilichonse?”
Ye turn things upside down! Shall the potter be esteemed as clay, that the thing made should say of him who made it, He did not make me, or the thing formed say of him who formed it, He has no understanding?
17 Kodi Lebanoni posachedwapa sadzasanduka munda wachonde, ndipo kodi munda wachondewo ngati nkhalango?
Is it not yet a very little while, and Lebanon shall be turned into a fruitful field, and the fruitful field shall be esteemed as a forest?
18 Tsiku limenelo anthu osamva adzamva mawu a mʼbuku, ndipo anthu osaona amene ankakhala mu mdima adzapenya.
And in that day the deaf shall hear the words of the book, and the eyes of the blind shall see out of obscurity and out of darkness.
19 Anthu odzichepetsa adzakhalanso ndi chimwemwe mwa Yehova; ndipo anthu osowa adzakondwa chifukwa cha Woyerayo wa Israeli.
The meek also shall increase their joy in Jehovah, and the poor among men shall rejoice in the Holy One of Israel.
20 Koma anthu ankhanza adzazimirira, oseka anzawo sadzaonekanso, ndipo onse okopeka ndi zoyipa adzawonongedwa.
For the terrible one is brought to nothing, and the scoffer ceases. And all those who watch for iniquity are cut off,
21 Yehova adzalanga amene amasinjirira munthu kuti apezeke wolakwa, kapena kuphophonyetsa anthu ozenga mlandu ndi umboni wonama kuti osalakwa asaweruzidwe mwachilungamo.
who make a man an offender in his cause, and lay a snare for him who reproves in the gate, and turn aside the just with a thing of nothing.
22 Choncho Yehova amene anawombola Abrahamu, akunena kwa zidzukulu za Yakobo kuti, “Anthu anga sadzachitanso manyazi; nkhope zawo sizidzagwanso ndi manyazi.
Therefore thus says Jehovah, who redeemed Abraham, concerning the house of Jacob: Jacob shall not now be ashamed, nor shall his face now grow pale.
23 Akadzaona ana awo ndi ntchito ya manja anga pakati pawo, adzatamanda dzina langa loyera; adzazindikira kuyera kwa Woyerayo wa Yakobo, ndipo adzachita naye mantha Mulungu wa Israeli.
But when he sees his children, the work of my hands, in the midst of him, they shall sanctify my name. Yea, they shall sanctify the Holy One of Jacob, and shall stand in awe of the God of Israel.
24 Anthu opusa adzapeza nzeru; onyinyirika adzalandira malangizo.”
They also who err in spirit shall come to understanding, and those who murmur shall receive instruction.

< Yesaya 29 >