< Yesaya 27 >

1 Tsiku limenelo, Yehova ndi lupanga lake lakuthwa, lalikulu ndi lamphamvu, adzalanga Leviyatani chinjoka chothawa chija, Leviyatani chinjoka chodzikulunga; adzapha chirombo choopsa cha mʼnyanja.
In that day Jehovah with his hard and great and strong sword will punish leviathan the swift serpent, and leviathan the crooked serpent, and he will kill the monster that is in the sea.
2 Tsiku limenelo Yehova adzati, “Tidzayimba nyimbo ya munda wamphesa wobereka bwino:
In that day is a vineyard of wine. Sing ye to it.
3 Ine, Yehova, ndimawuyangʼanira; ndimawuthirira nthawi zonse. Ndimawulondera usana ndi usiku kuti wina angawononge.
I Jehovah am its keeper, I will water it every moment. Lest any hurt it, I will guard it night and day.
4 Ine sindinakwiye. Ngati mkandankhuku ndi minga zikanaoneka ndikanalimbana nazo! Ndikachita nazo nkhondo; ndikanazitentha zonse ndi moto.
Wrath is not in me. Would that the briers and thorns were against me in battle! I would march upon them. I would burn them together.
5 Koma ngati apo ayi, abweretu kwa Ine adani angawo kuti ndidzawateteze; apangane nane za mtendere, ndithu, apangane nane za mtendere.”
Or else let him take hold of my strength, that he may make peace with me. Yea, let him make peace with me.
6 Masiku akubwerawo Yakobo adzazika mizu, Israeli adzaphukira ndi kuchita maluwa, ndipo adzadzaza dziko lonse lapansi ndi zipatso.
In days to come Jacob shall take root; Israel shall blossom and bud. And they shall fill the face of the world with fruit.
7 Kodi Yehova anakantha Israeli ngati momwe anakanthira anthu amene anazunza Israeli? Kapena kodi Yehova anapha Israeli ngati mmene anthu ena anaphera Israeli?
Has he smitten them as he smote those who smote them? Or are they slain according to the slaughter of those who were slain by them?
8 Yehova mwawalanga powapirikitsa ndi kuwatumiza ku ukapolo, mwawachotsa ndi mpweya wanu woopsa, monga zimachitikira pa tsiku la mkuntho wochokera kummawa.
In measure, in sending it forth, thou contend with it. He has removed with his rough blast in the day of the east wind.
9 Yehova adzakhululuka kulakwa kwa Yakobo. Iwo adzaonetsa kuti alapadi pamene adzaphwanya miyala yonse ya guwa lachikunja, ngati mmene anthu amaphwanyira miyala yanjereza mpaka kukhala ngati fumbi lokhalokha. Sipadzapezekanso mafano a Asera kapena maguwa ofukiza lubani.
Therefore by this the iniquity of Jacob shall be forgiven. And this is all the fruit of taking away his sin: that he makes all the stones of the altar as chalkstones that are beaten apart, so that the Asherim and the sun-images shall rise no more.
10 Mzinda wamalinga uja wasanduka bwinja, wasanduka malo osiyidwa, ndi kutayidwa ngati chipululu; kumeneko amadyetselako ana angʼombe kumeneko zimapumulako ziweto ndi kumwetula nthambi za mitengo kotheratu.
For the fortified city is solitary, a habitation deserted and forsaken like the wilderness. There the calf shall feed, and there he shall lie down, and consume the branches of it.
11 Pamene nthambi za mitengoyo zauma, zimathyoka ndipo amayi amabwera nazitola ndi kuzisandutsa nkhuni. Pakuti awa ndi anthu opanda nzeru; kotero Mulungu amene anawapanga sadzachitira chisoni, ndipo Mlengi wawo sawakomera mtima.
When the boughs of it are withered, they shall be broken off. The women shall come, and set them on fire, for it is a people of no understanding. Therefore he who made them will not have compassion upon them, and he who formed them will show them no favor.
12 Tsiku limenelo Yehova adzasonkhanitsa pamodzi anthu ake mmodzimmodzi kumalo opunthira tirigu, kuchokera ku mtsinje wa Yufurate mpaka ku mtsinje wa ku Igupto.
And it shall come to pass in that day, that Jehovah will beat off his fruit, from the flood of the River to the brook of Egypt. And ye shall be gathered one by one, O ye sons of Israel.
13 Ndipo tsiku limenelo lipenga lalikulu lidzalira. Amene akuzunzika ku Asiriya iwo amene ali ku ukapolo ku Igupto adzabwera ndi kudzalambira Yehova pa phiri lopatulika mu Yerusalemu.
And it shall come to pass in that day, that a great trumpet shall be blown. And they shall come who were ready to perish in the land of Assyria, and those who were outcasts in the land of Egypt. And they shall worship Jehovah in the holy mountain at Jerusalem.

< Yesaya 27 >