< Yesaya 19 >

1 Uthenga onena za Igupto: Taonani, Yehova wakwera pa mtambo waliwiro, ndipo akupita ku Igupto. Mafano a ku Igupto akunjenjemera pamaso pake, ndipo mitima ya Aigupto yachokamo ndi mantha.
The burden of Egypt. Behold, Jehovah rides upon a swift cloud, and comes to Egypt. And the idols of Egypt shall tremble at his presence, and the heart of Egypt shall melt in the midst of it.
2 “Ine ndidzadzutsa Aigupto kuti amenyane okhaokha; mʼbale adzamenyana ndi mʼbale wake, mnansi ndi mnansi wake, mzinda ndi mzinda unzake, ndiponso ufumu ndi ufumu unzake.
And I will stir up the Egyptians against the Egyptians, and they shall fight each one against his brother, and each one against his neighbor, city against city, kingdom against kingdom.
3 Aigupto adzataya mtima popeza ndidzalepheretsa zolinga zawo; adzapempha nzeru kwa mafano awo ndiponso kwa woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa, kwa amawula ndi kwa oyankhula ndi mizimu.
And the spirit of Egypt shall fail in the midst of it, and I will destroy the counsel of it. And they shall seek for the idols, and for the charmers, and for those who have familiar spirits, and for the wizards.
4 Ndidzawapereka Aigupto kwa olamulira ankhanza, ndipo mfumu yoopsa idzawalamulira,” akutero Ambuye Yehova Wamphamvuzonse.
And I will give over the Egyptians into the hand of a cruel lord. And a fierce king shall rule over them, says the Lord, Jehovah of hosts.
5 Madzi a mu mtsinje wa Nailo adzaphwa, ndipo mʼmbali mwa mtsinje mudzangʼaluka ndi kuwuma.
And the waters shall fail from the sea, and the river shall be wasted and become dry.
6 Ngalande zake zidzanunkha; ndipo mitsinje ya Igupto idzayamba kuchepa ndi kuwuma. Bango ndi dulu zidzafota,
And the rivers shall become foul. The streams of Egypt shall be diminished and dried up. The reeds and flags shall wither away.
7 ndiponso zomera za mʼmphepete mwa Nailo ndi ku mathiriro a mtsinjewo. Zonse zodzalidwa mʼmbali mwa Nailo zidzawuma, zidzawuluzika ndipo sizidzaonekanso.
The meadows by the Nile, by the brink of the Nile, and all the sown fields of the Nile, shall become dry, be driven away, and be no more.
8 Asodzi adzabuwula ndi kudandaula, onse amene amaponya mbedza mu Nailo; onse amene amaponya makoka mʼmadzi adzalira.
And the fishermen shall lament, and all those who cast a hook into the Nile shall mourn, and those who spread nets upon the waters shall languish.
9 Amene amagwira ntchito yopota thonje adzataya mtima, anthu oluka nsalu zofewa zabafuta adzataya chiyembekezo.
Moreover those who work in combed flax, and those who weave white cloth, shall be confounded.
10 Akatswiri opanga nsalu adzangoti kakasi, ndipo anthu onse ogwira ntchito yolipidwa adzatheratu mphamvu.
And the pillars of Egypt shall be broken in pieces. All those who work for hire shall be grieved in soul.
11 Akuluakulu a ku Zowani ndi zitsiru; aphungu a nzeru a Farao amalangiza zopusa. Kodi mungathe kunena bwanji kwa Farao kuti, “Ine ndine mmodzi mwa anthu anzeru, wophunzira wa mafumu akale?”
The rulers of Zoan are utterly foolish. The counsel of the wisest counselors of Pharaoh has become brutish. How will ye say to Pharaoh, I am the son of wise men, the son of ancient kings?
12 Iwe Farao, anthu ako anzeru ali kuti? Abweretu kuti akuwuze ndi kukudziwitsa zimene Yehova Wamphamvuzonse wakonza kuchitira dziko la Igupto.
Where then are thy wise men? And let them tell thee now, and let them know what Jehovah of hosts has purposed concerning Egypt.
13 Akuluakulu a ku Zowani asanduka zitsiru, atsogoleri a ku Mefisi anamizidwa; atsogoleri a dziko la Igupto asocheretsa anthu a dzikolo.
The rulers of Zoan have become fools. The rulers of Memphis are deceived. They have caused Egypt to go astray, the chief of her tribes.
14 Yehova wasocheretsa anthu a ku Igupto. Iwo akuchita kudzandira pa zonse zimene akuchita, ngati chidakwa choterereka pa masanzi ake.
Jehovah has mingled a spirit of perverseness in the midst of her, and they have caused Egypt to go astray in every work of it, as a drunken man staggers in his vomit.
15 Palibe chimene munthu wa mu Igupto angachite, mtsogoleri kapena wotsatira, nthambi ya kanjedza kapena bango.
Neither shall there be for Egypt any work, which head or tail, palm-branch or rush, may do.
16 Tsiku limenelo Aigupto adzakhala ngati amayi. Adzanjenjemera ndi kuchita mantha akadzaona Yehova Wamphamvuzonse, atakweza dzanja lake kufuna kuwalanga.
In that day the Egyptians shall be like women, and they shall tremble and fear because of the shaking of the hand of Jehovah of hosts, which he shakes over them.
17 Ndipo dziko la Yuda lidzaopsa dziko la Aigupto. Aliyense amene adzamve dzina la Yuda adzaopsedwa chifukwa cha zimene Yehova Wamphamvuzonse wakonzekera kuchitira dziko la Igupto.
And the land of Judah shall become a terror to Egypt. Everyone to whom mention is made of it shall be afraid because of the purpose of Jehovah of hosts, which he purposes against it.
18 Tsiku limenelo ku dziko la Igupto kudzakhala mizinda isanu yoyankhula chiyankhulo cha Akanaani, ndipo anthu ake adzalumbira kwa Yehova Wamphamvuzonse kuti adzamutumikira. Umodzi mwa mizindayo udzatchedwa Mzinda Wachilungamo.
In that day there shall be five cities in the land of Egypt that speak the language of Canaan, and swear to Jehovah of hosts. One shall be called The city of destruction.
19 Tsiku limenelo mʼkati mwa dziko la Igupto mudzakhala guwa lansembe la Yehova, ndipo mʼmalire mwake adzayikira Yehova mwala wachikumbutso.
In that day shall there be an altar to Jehovah in the midst of the land of Egypt, and a pillar to Jehovah at the border of it.
20 Zimenezo zidzakhala umboni wozindikiritsa kuti Yehova Wamphamvuzonse alimo mʼdziko la Igupto. Pamene Aigupto adzalirira Yehova chifukwa cha owapondereza, Iye adzawatumizira mpulumutsi ndi mtetezi ndipo adzawalanditsa.
And it shall be for a sign and for a witness to Jehovah of hosts in the land of Egypt. For they shall cry to Jehovah because of oppressors, and he will send them a savior, and a defender, and he will deliver them.
21 Kotero Yehova adzadziulula yekha kwa Aigupto, ndipo tsiku limenelo adzadziwa Yehova. Adzapembedza Yehova popereka nsembe ndi popereka zopereka zachakudya; Adzalumbira kwa Yehova ndipo adzachita zimene alumbirazo.
And Jehovah shall be known to Egypt, and the Egyptians shall know Jehovah in that day. Yea, they shall worship with sacrifice and oblation, and shall vow a vow to Jehovah, and shall perform it.
22 Yehova adzakantha Aigupto ndi mliri. Iye adzawakanthadi ndipo kenaka adzawachiritsa. Aigupto adzatembenukira kwa Yehova ndipo Iye adzamva madandawulo awo ndi kuwachiritsa.
And Jehovah will smite Egypt, smiting and healing, and they shall return to Jehovah. And he will be entreated by them, and will heal them.
23 Tsiku limenelo kudzakhala msewu waukulu wochoka ku Igupto kupita ku Asiriya. Aasiriya adzapita ku Igupto ndi Aigupto ku Asiriya. Aigupto ndi Aasiriya adzapembedza pamodzi.
In that day there shall be a highway out of Egypt to Assyria. And the Assyrian shall come into Egypt, and the Egyptian into Assyria, and the Egyptians shall worship with the Assyrians.
24 Tsiku limenelo Israeli adzakhala pamodzi ndi Igupto ndi Asiriya, mayiko atatuwa adzakhala dalitso pa dziko lapansi.
In that day Israel shall be the third with Egypt and with Assyria, a blessing in the midst of the earth,
25 Yehova Wamphamvuzonse adzawadalitsa, ndi mawu awa, “Adalitsike anthu anga Aigupto, Aasiriya, ntchito ya manja anga, ndi Aisraeli osankhidwa anga.”
in that Jehovah of hosts has blessed them, saying, Blessed be Egypt my people, and Assyria the work of my hands, and Israel my inheritance.

< Yesaya 19 >