< Genesis 9 >

1 Ndipo Mulungu anadalitsa Nowa ndi ana ake aamuna nati kwa iwo, “Berekanani ndipo muchulukane ndi kudzaza dziko lapansi.
And God blessed Noah and his sons, and said to them, Be fruitful, and multiply, and fill the earth.
2 Nyama zonse za dziko lapansi, ndi mbalame zonse za mlengalenga, ndi chamoyo chilichonse chokwawa, ndiponso nsomba zonse za ku nyanja; zidzakuopani ndipo ndazipereka kuti muzilamulire.
And the fear of you and the dread of you shall be upon every beast of the earth, and upon every bird of the heavens, with all with which the ground teems, and all the fishes of the sea. They are delivered into your hand.
3 Tsopano chamoyo chilichonse chidzakhala chakudya chanu. Monga momwe ndinakupatsirani ndiwo zamasamba, tsopano ndikupatsaninso nyama iliyonse.
Every moving thing that lives shall be food for you. As the green herb, I have given you all.
4 “Koma musamadye nyama imene ikanali ndi magazi oyenda.
But flesh with the life of it, which is the blood of it, ye shall not eat.
5 Aliyense wopha munthu adzaphedwa, nyama iliyonse yopha munthu idzaphedwa, munthu aliyense wopha munthu mnzake, adzaphedwa.
And surely your blood, the blood of your lives, I will require. At the hand of every beast I will require it. And at the hand of man, even at the hand of every man's brother, I will require the life of man.
6 “Aliyense wopha munthu, adzaphedwanso ndi munthu; pakuti Mulungu analenga munthu mʼchifanizo chake.
Whoever sheds man's blood, by man shall his blood be shed. For in the image of God he made man.
7 Inu muberekane ndi kuchulukana kuti mudzaze dziko lonse lapansi ndi kuligonjetsa.”
And you, be ye fruitful, and multiply. Bring forth abundantly on the earth, and multiply on it.
8 Mulungu anawuza Nowa ndi ana ake kuti,
And God spoke to Noah, and to his sons with him, saying,
9 “Tsopano Ine ndapangana ndi iwe ndi zidzukulu zako zamʼtsogolomo,
And I, behold, I establish my covenant with you, and with your seed after you,
10 pamodzi ndi zamoyo zonse, mbalame, ziweto ndi nyama zonse za kuthengo, ndi zonse zimene zinatuluka mʼchombo pamodzi ndi iwe.
and with every living creature that is with you, the birds, the cattle, and every beast of the earth with you, of all that go out of the ark, even every beast of the earth.
11 Pangano langa ndi ili: Ine ndilonjeza kuti sindidzawononganso zamoyo ndi madzi a chigumula. Chigumula sichidzawononganso dziko lapansi.”
And I will establish my covenant with you. Neither shall all flesh be cut off any more by the waters of the flood, nor shall there be a flood any more to destroy the earth.
12 Ndipo Mulungu anati, “Ine ndikupereka chizindikiro ichi cha pangano langa la pakati pa Ine ndi iwe, ana ako, zamoyo zonse, pamodzi ndi mibado ya mʼtsogolo.
And God said, This is the sign of the covenant which I make between me and you and every living creature that is with you, for perpetual generations:
13 Ndayika utawaleza wanga mʼmitambo, ndipo chidzakhala chizindikiro cha pangano langa ndi dziko lapansi.
I set my bow in the cloud, and it shall be for a sign of a covenant between me and the earth.
14 Nthawi zonse pakakhala mitambo mu mlengalenga ndipo utawaleza uwoneka,
And it shall come to pass, when I bring a cloud over the earth, that the bow shall be seen in the cloud.
15 ndizikumbukira pangano langa pakati pa Ine ndi inu ndi zolengedwa zonse. Madzi sadzakhalanso chigumula chowononga dziko lapansi.
And I will remember my covenant, which is between me and you and every living creature of all flesh. And the waters shall no more become a flood to destroy all flesh.
16 Utawaleza ukamadzaoneka mʼmitambo, ndidzawuona ndi kukumbukira pangano losatha pakati pa Mulungu ndi zamoyo zonse pa dziko lapansi.”
And the bow shall be in the cloud, and I will look upon it, that I may remember the everlasting covenant between God and every living creature of all flesh that is upon the earth.
17 Choncho Mulungu anati kwa Nowa, “Ichi ndiye chizindikiro cha pangano limene ndalichita pakati pa Ine ndi zamoyo zonse pa dziko lapansi.”
And God said to Noah, This is the sign of the covenant which I have established between me and all flesh that is upon the earth.
18 Ana aamuna a Nowa amene anatuluka mʼchombo muja anali Semu, Hamu ndi Yafeti. Hamu anali abambo ake a Kanaani.
And the sons of Noah, who went forth from the ark, were Shem, and Ham, and Japheth. And Ham is the father of Canaan.
19 Ana aamuna a Nowa amenewa ndiwo anali makolo a anthu onse pa dziko lapansi.
These three were the sons of Noah, and from these the whole earth was spread over.
20 Nowa anali munthu woyamba kulima munda wamphesa.
And Noah began to be a farmer, and planted a vineyard.
21 Tsiku lina pamene Nowa anamwako vinyo wa zipatso za mʼmundawo analedzera ndipo anavula zovala zake zonse ndi kugona mu tenti yake ali maliseche.
And he drank of the wine, and was drunken. And he was uncovered within his tent.
22 Hamu, abambo ake a Kanaani ataona kuti abambo ake ali maliseche anakawuza abale ake awiri aja omwe anali panja.
And Ham, the father of Canaan, saw the nakedness of his father, and told his two brothers outside.
23 Koma Semu ndi Yafeti anatenga chofunda nachiyika pa mapewa awo; ndipo anayenda chamʼmbuyo naphimba umaliseche wa abambo awo. Anafulatira kuti asaone umaliseche wa abambo awo.
And Shem and Japheth took a garment, and laid it upon both their shoulders, and went backward, and covered the nakedness of their father. And their faces were backward, and they did not see their father's nakedness.
24 Nowa atadzuka, kuledzera kutatha, ndikudziwa zimene mwana wake wamngʼono wamwamuna uja anamuchitira,
And Noah awoke from his wine, and knew what his youngest son had done to him.
25 anati, “Atembereredwe Kanaani! Adzakhala kapolo wa pansi kwenikweni kwa abale ake.”
And he said, Cursed be Canaan. He shall be a servant of servants to his brothers.
26 Anatinso, “Atamandike Yehova, Mulungu wa Semu! Kanaani akhale kapolo wa Semu.
And he said, Blessed be Jehovah, the God of Shem. And let Canaan be his servant.
27 Mulungu akulitse dziko la Yafeti; Yafeti alandire madalitso pamodzi ndi Semu, ndipo Kanaani akhale kapolo wawo.”
God enlarge Japheth, and let him dwell in the tents of Shem. And let Canaan be his servant.
28 Chitatha chigumula, Nowa anakhala ndi moyo zaka 350.
And Noah lived three hundred and fifty years after the flood.
29 Anamwalira ali ndi zaka 950.
And all the days of Noah were nine hundred and fifty years, and he died.

< Genesis 9 >