< Genesis 10 >

1 Nayi mbiri ya ana a Nowa, Semu, Hamu ndi Yafeti. Ana atatuwa anabereka ana awo chitatha chigumula.
Now these are the generations of the sons of Noah, of Shem, Ham, and Japheth. And sons were born to them after the flood.
2 Ana aamuna a Yafeti anali: Gomeri, Magogi, Madai, Yavani, Tubala, Mesaki ndi Tirasi.
The sons of Japheth: Gomer, and Magog, and Madai, and Javan, and Tubal, and Meshech, and Tiras.
3 Ana aamuna a Gomeri anali: Asikenazi, Rifati ndi Togarima.
And the sons of Gomer: Ashkenaz, and Riphath, and Togarmah.
4 Ana aamuna a Yavani anali: Elisa, Tarisisi, Kitimu ndi Rodanimu.
And the sons of Javan: Elishah, and Tarshish, Kittim, and Dodanim.
5 (Amenewa ndiwo makolo a anthu okhala mʼmphepete mwa nyanja. Awa ndi ana a Yafeti monga mwa mafuko a mu mitundu yawo, uliwonse ndi chiyankhulo chake).
From these were the islands of the nations divided in their lands, every man according to his tongue, according to their families, in their nations.
6 Ana aamuna a Hamu anali: Kusi, Miziraimu, Puti ndi Kanaani.
And the sons of Ham: Cush, and Mizraim, and Put, and Canaan.
7 Ana aamuna a Kusi anali: Seba, Havila, Sabita, Raama ndi Sabiteka. Ana aamuna a Raama anali: Seba ndi Dedani.
And the sons of Cush: Seba, and Havilah, and Sabtah, and Raamah, and Sabteca. And the sons of Raamah: Sheba, and Dedan.
8 Kusi anabereka Nimurodi amene anali wankhondo wamphamvu kwambiri pa dziko lapansi.
And Cush begot Nimrod. He began to be a mighty man on the earth.
9 Iye anali mlenje wamphamvu kwambiri pamaso pa Yehova; nʼchifukwa chake anthu ali ndi chisudzo, chakuti, “Ndiwe mlenje wamphamvu kwambiri pamaso pa Yehova monga Nimurodi.”
He was a mighty hunter before Jehovah. Therefore it is said, Like Nimrod a mighty hunter before Jehovah.
10 Malo oyambirira a ufumu wake anali Babeli, Ereki, Akadi ndi Kaline. Malo onsewa anali mʼdziko la Sinara.
And the beginning of his kingdom was Babel, and Erech, and Accad, and Calneh, in the land of Shinar.
11 Atachoka mʼdziko limeneli anapita ku Asiriya kumene anakamanga Ninive, Rehoboti-Iri, Kala,
He went forth out of that land into Assyria, and built Nineveh, and Rehoboth-ir, and Calah,
12 ndi Reseni, mzinda waukulu umene uli pakati pa Ninive ndi Kala.
and Resen between Nineveh and Calah (the same is the great city).
13 Igupto ndiye kholo la Aludi, Aanami, Alehabu, Anafutu,
And Mizraim begot Ludim, and Anamim, and Lehabim, and Naphtuhim,
14 Apaturusi, Akasilu ndi Akafitori (kumene kunachokera Afilisti).
and Pathrusim, and Casluhim (from where the Philistines went forth), and Caphtorim.
15 Kanaani anabereka mwana wake wachisamba, Sidoni, ndipo anaberekanso Ahiti;
And Canaan begot Sidon his firstborn, and Heth,
16 Ayebusi, Aamori, Agirigasi;
and the Jebusite, and the Amorite, and the Girgashite,
17 Ahivi, Aariki, Asini,
and the Hivite, and the Arkite, and the Sinite,
18 Aaravadi, Azemari ndi Ahamati. Pambuyo pake, mafuko a Akanaani anafalikira ponseponse,
and the Arvadite, and the Zemarite, and the Hamathite. And afterward the families of the Canaanite were spread abroad.
19 mpaka ku malire a Kanaani. Malirewo anachokera ku Sidoni kulowa cha ku Gerari mpaka ku Gaza, ndi kulowa ku Sodomu, Gomora, Adima ndi Zeboimu mpaka ku Lasa.
And the border of the Canaanite was from Sidon, as thou go toward Gerar, to Gaza, as thou go toward Sodom and Gomorrah and Admah and Zeboiim, to Lasha.
20 Amenewa ndiwo ana aamuna a Hamu monga mwa mafuko ndi ziyankhulo zawo, mʼmadera omwe amakhala ndi mitundu yawo.
These are the sons of Ham, according to their families, according to their tongues, in their lands, in their nations.
21 Semu amene anali mkulu wake wa Yafeti nayenso anabereka nakhala kholo la Eberi.
And to Shem, the father of all the sons of Eber, the elder brother of Japheth, sons were also born to him.
22 Ana aamuna a Semu anali: Elamu, Asuri, Aripakisadi, Ludi ndi Aramu.
The sons of Shem: Elam, and Asshur, and Arphaxad, and Lud, and Aram.
23 Ana aamuna a Aramu anali: Uzi, Huri, Geteri ndi Mesaki.
And the sons of Aram: Uz, and Hul, and Gether, and Mash.
24 Aripakisadi anabereka Sela, ndipo Selayo anabereka Eberi.
And Arphaxad begot Shelah, and Shelah begot Eber.
25 A Eberi anabereka ana aamuna awiri: Wina anamutcha Pelegi chifukwa pa nthawiyo anthu a pa dziko lapansi anagawikana. Dzina la mʼbale wake linali Yokitani.
And to Eber were born two sons. The name of the one was Peleg. For in his days the earth was divided. And his brother's name was Joktan.
26 Yokitani anabereka Alimodadi, Selefi, Hazari-Maveti, Yera,
And Joktan begot Almodad, and Sheleph, and Hazarmaveth, and Jerah,
27 Hadoramu, Uzali, Dikila,
and Hadoram, and Uzal, and Diklah,
28 Obali, Abimaeli, Seba,
and Obal, and Abimael, and Sheba,
29 Ofiri, Havila ndi Yobabu. Onsewa anali ana aamuna a Yokitani.
and Ophir, and Havilah, and Jobab. All these were the sons of Joktan.
30 Chigawo chimene ankakhala chinayambira ku Mesa mpaka ku Seferi, ku dera la mapiri chakummawa.
And their dwelling was from Mesha, as thou go toward Sephar, the mountain of the east.
31 Amenewa ndiwo ana a Semu monga mwa mafuko ndi ziyankhulo zawo, mʼmadera omwe ankakhala ndi mitundu yawo.
These are the sons of Shem, according to their families, according to their tongues, in their lands, according to their nations.
32 Amenewa ndiwo mafuko a ana aamuna a Nowa monga mwa mibado ya mitundu yawo. Mitundu yonse ya anthu inatuluka mwa iwowa ndi kufalikira pa dziko lonse lapansi chitatha chigumula chija.
These are the families of the sons of Noah, according to their generations, in their nations. And from these the nations were divided on the earth after the flood.

< Genesis 10 >