< Ezekieli 9 >

1 Pambuyo pake Yehova anandiyankhula mofuwula kuti, “Bwerani pafupi, inu odzalanga mzindawu, aliyense ali ndi chida chake mʼmanja.”
Then he cried in my ears with a loud voice, saying, Cause ye those who have charge over the city to draw near, each man with his destroying weapon in his hand.
2 Ndipo ndinaona anthu asanu ndi mmodzi akubwera kuchokera ku chipata chakumtunda chimene chimaloza kumpoto, aliyense ali ndi chida choopsa cha nkhondo mʼdzanja lake. Pagulu pawopa panali munthu wovala chovala chabafuta, atatenga zolembera pambali pake. Iwo analowa ndi kuyima pambali pa guwa lamkuwa.
And, behold, six men came from the way of the upper gate, which lies toward the north, each man with his slaughter weapon in his hand, and one man in the midst of them clothed in linen, with a writer's case by his side. And they went in, and stood beside the brazen altar.
3 Tsono ulemerero wa Mulungu wa Israeli unakwera kuchokera pamwamba pa akerubi, pamene unali, ndipo unafika pa chiwundo cha Nyumba ya Mulungu. Pamenepo Yehova anayitana munthu amene anavala chovala chabafuta uja amene anatenga zolembera pambali pake
And the glory of the God of Israel went up from the cherub, upon which it was, to the threshold of the house, and he called to the man clothed in linen who had the writer's case by his side.
4 ndipo anamuwuza kuti, “Pita mu mzinda wonse wa Yerusalemu ndi kuyika chizindikiro pamphumi pa anthu amene akumva chisoni ndi kulira chifukwa cha zinthu zonse zonyansa zimene zikuchitika mu mzindamo.”
And Jehovah said to him, Go through the midst of the city, through the midst of Jerusalem, and set a mark upon the foreheads of the men who sigh and who cry over all the abominations that are done in the midst of it.
5 Kenaka ndinamva Yehova akuwuza anthu ena aja kuti, “Mutsateni mu mzinda wonse ndipo mukakanthe aliyense mopanda kumvera chisoni kapena chifundo.
And to the others he said in my hearing, Go ye through the city after him, and smite. Let not your eye spare, nor have ye pity.
6 Mukaphe kotheratu anthu okalamba, anyamata ndi atsikana, makanda ndi akazi koma musakakhudze wina aliyense amene ali ndi chizindikiro. Muyambire ku Nyumba yanga yopatulika.” Motero iwo anayamba ndi akuluakulu amene anali kutsogolo kwa Nyumba ya Mulungu.
Kill utterly the old man, the young man, and the virgin, and little sons, and women, but come not near any man upon whom is the mark. And begin at my sanctuary. Then they began at the old men who were before the house.
7 Ndipo Yehova anawawuza kuti, “Ipitsani Nyumba ya Mulungu ndipo mudzaze mabwalo ake ndi anthu akufa. Pitani.” Choncho iwo anapita nayamba kupha anthu mu mzinda monse.
And he said to them, Defile the house, and fill the courts with the slain. Go ye forth. And they went forth, and smote in the city.
8 Pamene iwo ankapha anthu, ine ndinatsala ndekha. Tsono ndinadzigwetsa chafufumimba ndi kufuwula kuti, “Aa, Ambuye Yehova! Kodi mwawakwiyiratu anthu a ku Yerusalemu motero kuti mudzawononga kotheratu anthu onse otsala ku Israeli?”
And it came to pass, while they were smiting, and I was left, that I fell upon my face, and cried, and said, Ah lord Jehovah! Will thou destroy all the residue of Israel in thy pouring out of thy wrath upon Jerusalem?
9 Iye anandiyankha kuti, “Tchimo la Aisraeli ndi Yuda ndi lalikulu kwambiri; dziko ladzaza ndi zophana ndipo mu mzinda mwadzaza ndi zosalungama. Iwo akunena kuti, ‘Yehova walisiya dziko lake; Yehova sakuona.’
Then he said to me, The iniquity of the house of Israel and Judah is exceedingly great, and the land is full of blood, and the city full of perverseness. For they say, Jehovah has forsaken the land, and Jehovah does not see.
10 Choncho sindidzawamvera chisoni kapena kuwaleka, koma Ine ndidzawalanga potsata zochita zawo.”
And as for me also, my eye shall not spare, nor will I have pity, but I will bring their way upon their head.
11 Ndipo munthu wovala chovala chabafuta uja atatenga zolembera pambali pake anadzafotokozera Yehova kuti, “Ndachita monga munandilamulira.”
And, behold, the man clothed in linen, who had the writing case by his side, reported the matter, saying, I have done as thou have commanded me.

< Ezekieli 9 >