< Ezekieli 8 >

1 Tsiku lachisanu la mwezi wachisanu ndi chimodzi, mʼchaka chachisanu ndi chimodzi, ndinakhala mʼnyumba mwanga pamodzi ndi akuluakulu a ku Yuda. Tsono mphamvu za Ambuye Yehova zinandifikira.
And it came to pass in the sixth year, in the sixth month, in the fifth day of the month, as I sat in my house, and the elders of Judah sat before me, that the hand of the lord Jehovah fell there upon me.
2 Nditayangʼana ndinangoona chinthu chooneka ngati munthu. Kuchokera pamene pamaoneka ngati chiwuno chake kumatsika mʼmunsi anali ngati moto, ndipo kuchokera mʼchiwuno kukwera mmwamba amaoneka mowala ngati mkuwa wonyezimira.
Then I beheld, and, lo, a likeness as the appearance of fire, from the appearance of his loins and downward, fire, and from his loins and upward, as the appearance of brightness, as it were glowing metal.
3 Iye anatambasula chinthu chooneka ngati dzanja ndipo anagwira tsitsi la pamutu panga. Nthawi yomweyo Mzimu unandikweza mlengalenga. Tsono ndikumachita ngati ndikuona Mulungu kutulo, Mzimu uja unapita nane ku Yerusalemu nundiyika pa khomo la chipata chamʼkati choyangʼana kumpoto. Kumeneko kunali fano limene limaputa mkwiyo wa Mulungu.
And he put forth the form of a hand, and took me by a lock of my head. And the Spirit lifted me up between earth and heaven, and brought me in the visions of God to Jerusalem, to the door of the gate of the inner court that looks toward the north, where the seat of the image of jealousy was, which provokes to jealousy.
4 Kumeneko ndinaona ulemerero wa Mulungu wa Israeli ngati momwe ndinaonera mʼmasomphenya mʼchigwa muja.
And, behold, the glory of the God of Israel was there, according to the appearance that I saw in the plain.
5 Tsono Yehova anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, tayangʼana kumpoto.” Choncho ndinayangʼana kumpoto ndipo ndinaona pa khomo la chipata pafupi ndi guwa lansembe ndinaona fano loputa mkwiyo wa Mulungu lija.
Then he said to me, Son of man, lift up thine eyes now the way toward the north. So I lifted up my eyes the way toward the north, and, behold, northward of the gate of the altar was this image of jealousy in the entry.
6 Ndipo Yehova anandifunsa kuti, “Iwe mwana wa munthu, kodi ukuona zimene akuchitazi, zonyansa zazikulu zimene Aisraeli akuchita kuno, zinthu zondichotsa Ine kumalo anga opatulika? Koma iwe udzaona zinthu zimene zili zonyansa kwambiri.”
And he said to me, Son of man, see thou what they do, even the great abominations that the house of Israel commit here, that I should go far off from my sanctuary? But thou shall again see yet other great abominations.
7 Kenaka Iye anandipititsa ku khomo lolowera ku bwalo la Nyumba ya Mulungu. Nditayangʼanitsitsa ndinangoona dzenje pa khomapo.
And he brought me to the door of the court. And when I looked, behold, a hole in the wall.
8 Yehova anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, tsopano bowola pa khomapo.” Ndinabowoladi pa khomapo ndipo ndinapezapo khomo.
Then he said to me, Son of man, dig now in the wall. And when I had dug in the wall, behold, a door.
9 Ndipo Yehova anandiwuza kuti, “Lowa, ndipo ona zinthu zonyansa zimene akuchita pamenepa.”
And he said to me, Go in, and see the wicked abominations that they do here.
10 Motero Ine ndinalowa ndi kuyangʼana, ndipo ndinaona pa makoma onse zithunzi za zinthu zosiyanasiyana zokwawa pansi, za nyama zonyansa ndiponso za mafano onse amene Aisraeli ankapembedza.
So I went in and saw, and, behold, every form of creeping things, and abominable beasts, and all the idols of the house of Israel, portrayed upon the wall round about.
11 Patsogolo pa zimenezi panayima akuluakulu makumi asanu ndi awiri a Aisraeli, ndipo Yaazaniya mwana wa Safani anali atayima pakati pawo. Aliyense wa iwo anali ndi chofukizira lubani mʼdzanja lake ndipo utsi wa fungo lokoma la lubani unkafuka.
And there stood before them seventy men of the elders of the house of Israel. And in the midst of them stood Jaazaniah the son of Shaphan, each man with his censer in his hand, and the odor of the cloud of incense went up.
12 Tsono Yehova anandifunsa kuti, “Iwe mwana wa munthu, kodi waona zimene akuluakulu a Aisraeli akuchita mu mdima, aliyense akupembedza fano lakelake mʼnyumbamo? Iwo akuti, ‘Yehova sakutiona; Yehova walisiya dziko!’
Then he said to me, Son of man, have thou seen what the elders of the house of Israel do in the dark, each man in his chambers of imagery? For they say, Jehovah does not see us. Jehovah has forsaken the land.
13 Iye anandiwuzanso kuti, ‘Iwe udzawaonanso akuchita zinthu zonyansa kwambiri.’”
He also said to me, Thou shall again see yet other great abominations which they do.
14 Kenaka anapita nane pa khomo la ku khomo la chipata cha Nyumba ya Mulungu choyangʼana kumpoto, ndipo kumeneko ndinaona akazi ena atakhala pansi, akulira mulungu wawo wotchedwa Tamuzi.
Then he brought me to the door of the gate of Jehovah's house which was toward the north. And, behold, there sat the women weeping for Tammuz.
15 Yehova anandifunsa kuti, “Iwe mwana wa munthu, kodi ukuziona zimenezi? Iwe udzaona zinthu zimene zili zonyansa kwambiri kuposa izi.”
Then he said to me, Have thou seen this, O son of man? Thou shall again see yet greater abominations than these.
16 Kenaka Iye anapita nane mʼkati mwa bwalo la Nyumba ya Yehova. Kumeneko ku khomo lolowera ku Nyumba ya Yehova pakati pa khonde ndi guwa lansembe, panali amuna 25. Anafulatira Nyumba ya Mulungu wa Yehova ndipo nkhope zawo zinaloza kummawa, ndipo ankapembedza dzuwa choyangʼana kummawa.
And he brought me into the inner court of Jehovah's house. And, behold, at the door of the temple of Jehovah, between the porch and the altar, were about twenty-five men with their backs toward the temple of Jehovah, and their faces toward the east, and they were worshiping the sun toward the east.
17 Yehova anandifunsa kuti, “Iwe mwana wa munthu, kodi waziona zimenezi? Kodi nʼchinthu chopepuka kuti anthu a ku Yuda azichita zonyansa zimene akuchitazi pano? Kodi afike mpaka pomafalitsa za ndewu mʼdziko lonse? Iwotu akuwutsa ukali wanga. Akundipsetsa mtima ndi zochita zawo!
Then he said to me, Have thou seen this, O son of man? Is it a light thing to the house of Judah that they commit the abominations which they commit here? For they have filled the land with violence, and have turned again to provoke me to anger. And, lo, they put the branch to their nose.
18 Choncho Ine ndidzawalanga ndili wokwiya. Sindidzawamvera chisoni kapena kuwaleka. Ngakhale atandifuwulira mʼmakutu mwanga sindidzawamvera.”
Therefore I will also deal in wrath. My eye shall not spare, nor will I have pity. And though they cry in my ears with a loud voice, yet I will not hear them.

< Ezekieli 8 >