< Ezekieli 10 >

1 Ine nditayangʼana ku thambo limene lili pamwamba pa mitu ya akerubi ndinangoona chinthu chooneka ngati mpando waufumu wa mwala wa safiro.
Then I looked, and, behold, in the firmament that was over the head of the cherubim there appeared above them as it were a sapphire stone, as the appearance of the likeness of a throne.
2 Tsono Yehova anawuza munthu wovala chovala chabafuta uja kuti, “Pita pakati pa mikombero kunsi kwa akerubi. Udzaze manja ako ndi makala oyaka amene ali pakati pa akerubiwo ndipo uwawaze mu mzinda.” Iye anachita zimenezi ine ndikuona.
And he spoke to the man clothed in linen, and said, Go in between the whirling wheels, even under the cherub, and fill both thy hands with coals of fire from between the cherubim, and scatter them over the city. And he went in in my sight.
3 Apa akerubiwo anali atayima mbali ya kummwera kwa Nyumba ya Mulungu pamene munthuyo ankalowa. Tsono mtambo unadzaza bwalo lamʼkati.
Now the cherubim stood on the right side of the house when the man went in, and the cloud filled the inner court.
4 Ndipo ulemerero wa Yehova unachoka pamwamba pa akerubi ndipo unafika ku chiwundo cha Nyumba ya Mulungu. Mtambo unadzaza Nyumba ya Mulungu, ndipo kuwala kwa ulemerero wa Yehova kunadzaza bwalolo.
And the glory of Jehovah mounted up from the cherub, over the threshold of the house. And the house was filled with the cloud, and the court was full of the brightness of Jehovah's glory.
5 Phokoso la mapiko a akerubi limamveka mpaka ku bwalo lakunja, monga momwe linamvekera liwu la Mulungu Wamphamvuzonse akamayankhula.
And the sound of the wings of the cherubim was heard even to the outer court, as the voice of God Almighty when he speaks.
6 Kenaka Yehova analamula munthu wovala chovala chabafuta uja kuti, “Pala moto pakati pa mikombero, pakati pa akerubi.” Munthu uja anapitadi nakayima pa mbali pa mkombero umodzi.
And it came to pass, when he commanded the man clothed in linen, saying, Take fire from between the whirling wheels, from between the cherubim, that he went in, and stood beside a wheel.
7 Ndipo mmodzi wa akerubi anatambalitsa dzanja lake mpaka pa moto umene unali pakati pawo. Iye anapalako motowo ndipo anapatsa munthu wovala chovala chabafuta uja. Tsono iye anawulandira natuluka.
And the cherub stretched forth his hand from between the cherubim to the fire that was between the cherubim, and took, and put it into the hands of him who was clothed in linen, who took it and went out.
8 Ndiye kuti kunsi kwa mapiko akerubi kumaoneka zinthu zooneka ngati manja a munthu.
And there appeared in the cherubim the form of a man's hand under their wings.
9 Ine nditayangʼanitsitsa ndinaona mikombero inayi pambali pa akerubi. Pambali pa kerubi aliyense panali mkombero umodzi; mikomberoyo inkanyezimira ngati miyala yokongola ya krizoliti.
And I looked, and, behold, four wheels beside the cherubim, one wheel beside one cherub, and another wheel beside another cherub. And the appearance of the wheels was like a beryl stone.
10 Maonekedwe a mikombero inayi ija anali ofanana. Mkombero uliwonse umaoneka ngati mkombero wolowana ndi unzake.
And as for their appearance, those four had one likeness, as if a wheel have been within a wheel.
11 Poyenda akerubiwo, amapita mbali iliyonse ya mbali zinayizo kumene akerubiwo amayangʼana. Mikomberoyo simatembenuka pamene akerubiwo ankayenda. Kulikonse kumene mutu walunjika nʼkumene ankapita popanda kutembenuka.
When they went, they went in their four directions. They did not turn as they went, but to the place where the head looked they followed it. They did not turn as they went.
12 Matupi awo onse, misana yawo, manja awo ndi mapiko awo zinali ndi maso okhaokha, monganso mʼmene inalili mikombero yawo inayi ija.
And their whole body, and their backs, and their hands, and their wings, and the wheels, were full of eyes round about, even the wheels that those four had.
13 Ine ndinamva mikombero ikutchedwa kuti, “mikombero yakamvuluvulu.”
As for the wheels, they were called in my hearing, O wheel.
14 Kerubi aliyense anali ndi nkhope zinayi. Nkhope yoyamba inali ya Kerubi, nkhope yachiwiri inali ya munthu, nkhope yachitatu inali ya mkango ndipo nkhope yachinayi inali ya chiwombankhanga.
And each one had four faces. The first face was the face of the cherub, and the second face was the face of a man, and the third face the face of a lion, and the fourth the face of an eagle.
15 Tsono akerubi aja anawuluka. Izi zinali zamoyo zija zimene ndinaziona ku mtsinje wa Kebara.
And the cherubim mounted up. This is the living creature that I saw by the river Chebar.
16 Pamene akerubi ankayenda, nayonso mikombero ya mʼmbali mwawo inkayenda. Akerubiwo ankati akatambasula mapiko awo kuti auluke mikombero sinkachoka mʼmbali mwawo.
And when the cherubim went, the wheels went beside them. And when the cherubim lifted up their wings to mount up from the earth, the wheels also did not turn from beside them.
17 Akerubiwo ankati akayima, mikombero inkayimanso. Ngati akerubiwo auluka, mikomberoyo inkapita nawo chifukwa mzimu wa zamoyozo ndiwo unkayendetsa mikomberoyo.
When they stood, these stood, and when they mounted up, these mounted up with them, for the spirit of the living creature was in them.
18 Pamenepo ulemerero wa Yehova unachoka pa chiwundo cha Nyumba ya Mulungu ndi kukakhala pamwamba pa akerubi.
And the glory of Jehovah went forth from over the threshold of the house, and stood over the cherubim.
19 Ine ndikuona akerubi, anatambasula mapiko awo ndi kuwuluka. Pamene ankapita, mikombero inapita nawo pamodzi. Akerubi anakayima pa khomo la chipata cha kummawa cha Nyumba ya Yehova. Tsono ulemerero wowala wa Mulungu wa Israeli unali pamwamba pawo.
And the cherubim lifted up their wings, and mounted up from the earth in my sight when they went forth, and the wheels beside them. And they stood at the door of the east gate of Jehovah's house, and the glory of the God of Israel was over them above.
20 Izi ndizo zamoyo ndinaziona pansi pa Mulungu wa Israeli ku mtsinje wa Kebara, ndipo ndinazindikira kuti anali akerubi.
This is the living creature that I saw under the God of Israel by the river Chebar, and I knew that they were cherubim.
21 Kerubi aliyense anali ndi nkhope zinayi ndi mapiko anayi, ndipo kunsi kwa mapiko awo kunali chinthu chimene chimaoneka ngati manja a munthu.
Each one had four faces, and each one four wings. And the likeness of the hands of a man was under their wings.
22 Nkhope zawo zinali zofanana ndi zomwe ndinaziona ku mtsinje wa Kebara. Kerubi aliyense amayenda molunjika.
And as for the likeness of their faces, they were the faces which I saw by the river Chebar, their appearances and themselves. They went each one straight forward.

< Ezekieli 10 >