< Ezekieli 36 >

1 “Iwe mwana wa munthu, yankhula kwa mapiri a Israeli ndipo unene kuti, ‘Inu mapiri a Israeli, imvani mawu a Yehova.’
And thou, son of man, prophesy to the mountains of Israel, and say, Ye mountains of Israel, hear the word of Jehovah.
2 Ine Ambuye Yehova ndikuti: Mdani wanu ankanena kuti, ‘Aa! Dziko lamapiri lakalekale lija lasanduka lathu.’
Thus says the lord Jehovah: Because the enemy has said against you, Aha! and, The ancient high places are ours in possession,
3 Choncho nenera ndipo uwawuze kuti, ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Popeza anakusakazani ndi kukuponderezani ku mbali zonse motero kuti munakhala mʼmanja mwa anthu a mitundu ina yonse ndipo anthu ankakunenani ndi kukunyozani,
therefore prophesy, and say, Thus says the lord Jehovah: Because, even because they have made you desolate, and swallowed you up on every side, that ye might be a possession to the residue of the nations, and ye are taken up in the lips of talkers, and the evil report of the people,
4 choncho, inu mapiri a Israeli, imvani zimene Ine Ambuye Yehova ndikuwuza mapiri ndi magomo, zigwembe ndi zigwa, mabwinja ndi mizinda yosiyidwa imene yakhala ikufunkhidwa komanso kunyozedwa ndi anthu a mitundu ina okuzungulirani.
therefore, ye mountains of Israel, hear the word of the lord Jehovah. Thus says the lord Jehovah to the mountains and to the hills, to the watercourses and to the valleys, to the desolate wastes and to the cities that are forsaken, which have become a prey and derision to the residue of the nations that are round about,
5 Tsono Ine Ambuye Yehova ndikuti: Mu mkwiyo wanga woopsa ndinayankhula kuyimba mlandu mitundu ina yonse ya anthu makamaka a ku Edomu. Iwowa mwa chimwemwe chodzaza tsaya ndi mwa nkhwidzi analanda dziko langa ndi kulisandutsa lawo ndi kutengeratu dziko la msipu kukhala lawo.’
therefore thus says the lord Jehovah: Surely in the fire of my jealousy I have spoken against the residue of the nations, and against all Edom, who have appointed my land to themselves for a possession with the joy of all their heart, with spite of soul, to cast it out for a prey.
6 Nʼchifukwa chake, lengeza ku dziko la Israeli, ndipo uwuze mapiri ndi magomo, zigwembe ndi zigwa kuti, ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ine ndikuyankhula ndi mtima wokwiya kwambiri chifukwa inu munalandira chitonzo cha anthu a mitundu ina.’
Therefore prophesy concerning the land of Israel, and say to the mountains and to the hills, to the watercourses and to the valleys, Thus says the lord Jehovah: Behold, I have spoken in my jealousy and in my wrath, because ye have borne the shame of the nations.
7 Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndikulumbira nditakweza dzanja langa kuti mitundu ya anthu idzatozedwanso.
Therefore thus says the lord Jehovah: I have sworn, saying, Surely the nations that are round about you, they shall bear their shame.
8 “Koma Inu mapiri a Israeli mudzaphukanso nthambi ndipo mudzawabalira zipatso anthu anga a Israeli, pakuti ali pafupi kubwerera kwawo.
But ye, O mountains of Israel, ye shall shoot forth your branches, and yield your fruit to my people Israel, for they are at hand to come.
9 Taonani, Ine ndili mbali yanu ndipo ndidzakukomerani mtima. Mudzalimidwa ndi kudzalidwa.
For, behold, I am for you, and I will turn into you, and ye shall be tilled and sown.
10 Ndidzachulukitsa chiwerengero cha anthu anu, nyumba yonse ya Israeli. Mʼmizinda mudzakhalanso anthu ndipo mabwinja adzamangidwanso.
And I will multiply men upon you, all the house of Israel, even all of it, and the cities shall be inhabited, and the waste places shall be built.
11 Ndidzachulukitsa chiwerengero cha amuna pamodzi ndi ziweto zomwe, ndipo adzachuluka kwambiri ndi kubereka ana ambiri. Ndidzakhazika anthu mʼdzikomo monga analili kale, ndi kukulemeretsani kuposa kale. Pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
And I will multiply upon you man and beast, and they shall increase and be fruitful. And I will cause you to be inhabited according to your former estate, and will do better to you than at your beginnings. And ye shall know that I am Jehovah.
12 Ndidzachititsa anthu kuyenda pa inu, ndiye kuti inu anthu anga Aisraeli. Iwowo adzakhazikika pa inu, ndipo inu mudzakhala cholowa chawo. Simudzalandanso ana awo.
Yea, I will cause men to walk upon you, even my people Israel, and they shall possess thee, and thou shall be their inheritance, and thou shall no more henceforth bereave them of sons.
13 “Ine Ambuye Yehova ndikuti: Popeza anthu amanena kuti, ndiwe dziko limene limadya anthu ake ‘kulanda ana a mtundu wake,’
Thus says the lord Jehovah: Because they say to you, Thou O land are a devourer of men, and have been a bereaver of thy nation,
14 nʼchifukwa chake, simudzadyanso anthu kapena kulanda ana a mtundu wako. Ine Ambuye Yehova ndikutero.
therefore thou shall no more devour men, nor bereave thy nation any more, says the lord Jehovah.
15 Sindidzakulolaninso kumva mnyozo wa anthu a mitundu ina, kapena kupirira kunyogodola kwawo kapenanso kupunthwitsanso anthu a mʼdziko lako. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.”
Neither will I let thee hear any more the shame of the nations, nor shall thou bear the reproach of the peoples any more, nor shall thou cause thy nation to stumble any more, says the lord Jehovah.
16 Yehova anandiyankhulanso kuti:
Moreover the word of Jehovah came to me, saying,
17 “Iwe mwana wa munthu, pamene anthu a Israeli ankakhala mʼdziko lawolawo, analiyipitsa ndi makhalidwe awo ndiponso zochita zawo. Machitidwe awo pamaso panga anali onyansa pa zachipembedzo ngati msambo wa mkazi amene ali pa nthawi yake.
Son of man, when the house of Israel dwelt in their own land, they defiled it by their way and by their doings. Their way before me was as the uncleanness of a woman in her impurity.
18 Tsono ndinawalanga chifukwa cha magazi amene anakhetsa mʼdzikomo, ndiponso chifukwa anayipitsa dziko ndi mafano awo.
Therefore I poured out my wrath upon them for the blood which they had poured out upon the land, and because they had defiled it with their idols.
19 Ndinawamwaza pakati pa anthu a mitundu ina ndipo anabalalikira mʼmayiko onse. Ndinawalanga molingana ndi makhalidwe awo ndi zochita zawo.
And I scattered them among the nations, and they were dispersed through the countries. I judged them according to their way and according to their doings.
20 Atafika kwa anthu a mitundu ina, kulikonse kumene anapitako, anayipitsa dzina langa loyera. Zinatero popeza anthu ponena za iwo ankanena kuti, ‘Awa ndi anthu a Yehova, komatu anachotsedwa ku dziko lake.’
And when they came to the nations where they went, they profaned my holy name, in that men said of them, These are the people of Jehovah, and have gone forth out of his land.
21 Koma Ine ndinkadera nkhawa dzina langa loyera, limene Aisraeli analiyipitsa pakati pa anthu a mitundu ina kumene anapitako.
But I had regard for my holy name, which the house of Israel had profaned among the nations where they went.
22 “Nʼchifukwa chake awuze Aisraeliwo kuti Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ine ndidzachita zimene ndidzachitezo osati chifukwa cha inuyo Aisraelinu ayi, koma chifukwa cha dzina langa, limene mwaliyipitsa pakati pa anthu a mitundu ina kumene munapitako.
Therefore say to the house of Israel, Thus says the lord Jehovah: I do this not for your sake, O house of Israel, but for my holy name, which ye have profaned among the nations where ye went.
23 Ndidzaonetsa chiyero cha dzina langa lotchuka, limene layipitsidwa pakati pawo. Anthu a mitundu inayo atadzazindikira kuti ndaonetsa kudzera mwa inu kuti dzina langa ndi loyera, iwo adzadziwanso kuti Ine ndine Yehova. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
And I will sanctify my great name, which has been profaned among the nations, which ye have profaned in the midst of them. And the nations shall know that I am Jehovah, says the lord Jehovah, when I shall be sanctified in you before their eyes.
24 “Pakuti Ine ndidzakuchotsani pakati pa anthu a mitundu ina. Ndidzakusonkhanitsani kuchoka ku mayiko onse ndi kukubwezerani ku dziko lanulanu.
For I will take you from among the nations, and gather you out of all the countries, and will bring you into your own land.
25 Ndidzakuwazani madzi oyera, ndipo mudzakhala oyera mtima. Zonse zimene zimakuyipitsani zidzachoka. Ndidzakuyeretsani pochotsa mafano anu onse.
And I will sprinkle clean water upon you, and ye shall be clean. I will cleanse you from all your filthiness, and from all your idols.
26 Ndidzakupatsani mtima watsopano ndi kulowetsa mzimu watsopano mwa inu. Ndidzachotsa mwa inu mtima wanu wowuma ngati mwala ndi kukupatsani mtima wofewa ngati mnofu.
I will also give you a new heart, and I will put a new spirit within you. And I will take away the stony heart out of your flesh, and I will give you a heart of flesh.
27 Ndipo ndidzayika Mzimu wanga mwa inu ndipo ndidzakuthandizani kutsatira malangizo anga ndi kukusungitsani mosamala kwambiri malamulo anga.
And I will put my Spirit within you, and cause you to walk in my statutes, and ye shall keep my ordinances, and do them.
28 Mudzakhala mʼdziko limene ndinapatsa makolo anu. Mudzakhala anthu anga, ndipo Ine ndidzakhala Mulungu wanu.
And ye shall dwell in the land that I gave to your fathers, and ye shall be my people, and I will be your God.
29 Ndidzakupulumutsani ku zonse zokuyipitsani. Ndidzakuchulukitsirani tirigu ndipo sindidzakugwetseraninso njala.
And I will save you from all your uncleannesses. And I will call for the grain, and will multiply it, and lay no famine upon you.
30 Ndidzachulukitsa zipatso za mʼmitengo yanu ndi zokolola za mʼmunda mwanu, kotero kuti simudzanyozedwanso pakati pa anthu a mitundu ina chifukwa cha njala.
And I will multiply the fruit of the tree, and the increase of the field, that ye may no more receive the reproach of famine among the nations.
31 Pamenepo mudzakumbukira makhalidwe anu oyipa ndi ntchito zanu zoyipa. Machimo anu ndi ntchito zanu zonyansa zidzakuchititsa nokha manyazi.
Then ye shall remember your evil ways, and your doings that were not good. And ye shall loathe yourselves in your own sight for your iniquities and for your abominations.
32 Tsono dziwani kuti Ine sindidzachita zimenezi chifukwa cha inuyo ayi, ndikutero Ine Ambuye Wamphamvuzonse. Ndiyetu chitani manyazi ndipo mugwetse nkhope zanu, inu Aisraeli chifukwa cha makhalidwe anu!
I do this not for your sake, says the lord Jehovah; be it known to you. Be ashamed and confounded for your ways, O house of Israel.
33 “Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pa tsiku limene ndidzayeretse machimo anu onse, ndidzayikamonso anthu mʼmizinda yanu, ndipo ndidzamanganso nyumba pa mabwinja.
Thus says the lord Jehovah: In the day that I cleanse you from all your iniquities, I will cause the cities to be inhabited, and the waste places shall be built.
34 Dziko limene linasanduka chipululu lizidzalimidwanso. Mʼmalo moti aliyense wopitamo alione dzikolo ngati chipululu tsopano adzaliona lolimidwa.
And the land that was desolate shall be tilled, whereas it was a desolation in the sight of all who passed by.
35 Iwo adzati, ‘Dziko ili, limene linali chipululu, lasanduka munda wa Edeni. Mizinda imene inali mabwinja osiyidwa ndi owonongedwa, tsopano ndi yotetezedwa ndi yokhalamo anthu.
And they shall say, This land that was desolate has become like the garden of Eden. And the waste and desolate and ruined cities are fortified and inhabited.
36 Ndipo anthu a mitundu ina okhala pafupi nanu amene anatsala adzadziwa kuti Ine Yehova ndine amene ndinamanganso mizinda yowonongeka ndi kudzalanso zinthu zatsopano mʼmalo mʼmene munali chipululu. Ine Yehova ndayankhula ndipo ndidzazichitadi.’
Then the nations that are left round about you shall know that I, Jehovah, have built the ruined places, and planted that which was desolate. I, Jehovah, have spoken it, and I will do it.
37 “Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndidzalolanso Aisraeli kuti andipemphe zoti ndiwachitire: Ndidzachulukitsa anthu awo ngati nkhosa.
Thus says the lord Jehovah: For this, moreover, I will be inquired of by the house of Israel, to do it for them. I will increase them with men like a flock.
38 Adzachulukadi ngati nkhosa zomwe ankapereka ngati nsembe ku Yerusalemu pa nthawi za chikondwerero. Choncho mizinda ya mabwinja idzadzaza ndi anthu. Zikadzatero adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”
As the flock for sacrifice, as the flock of Jerusalem in her appointed feasts, so shall the waste cities be filled with flocks of men. And they shall know that I am Jehovah.

< Ezekieli 36 >