< Ezekieli 35 >

1 Yehova anandiyankhula kuti:
Moreover the word of Jehovah came to me, saying,
2 “Iwe mwana wa munthu, yangʼana phiri la Seiri; yankhula moliyimba mlandu ndipo
Son of man, set thy face against mount Seir, and prophesy against it.
3 awawuze anthu a kumeneko kuti zimene ndikuyankhula Ine Ambuye Yehova ndi izi: Inu anthu a ku mapiri a Seiri ndikudana nanu. Ndidzatambasula dzanja langa kulimbana nanu, ndipo ndidzasandutsa dziko lanu kukhala chipululu.
And say to it, Thus says the lord Jehovah: Behold, I am against thee, O mount Seir, and I will stretch out my hand against thee, and I will make thee a desolation and an astonishment.
4 Mizinda yanu ndidzayisandutsa mabwinja, ndipo dziko lanu lidzasanduka chipululu. Zikadzachitika izi mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
I will lay thy cities waste, and thou shall be desolate. And thou shall know that I am Jehovah.
5 “Munali adani a Israeli nthawi zonse, ndipo munkalola kuti Aisraeli aphedwe pa nkhondo pa nthawi ya mavuto awo, pa nthawi imene chilango chawo chinafika pachimake.
Because thou have had a perpetual enmity, and have given over the sons of Israel to the power of the sword in the time of their calamity, in the time of the iniquity of the end,
6 Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pali Ine wamoyo, ndithu ndidzakukanthani. Imfa idzakulondolani. Popeza sunadane nako kukhetsa magazi, imfa idzakulondola.
therefore, as I live, says the lord Jehovah, I will prepare thee to blood, and blood shall pursue thee. Since thou have not hated blood, therefore blood shall pursue thee.
7 Phiri la Seiri ndidzalisandutsa chipululu ndipo ndidzapha onse amene amapita nabwerera kumeneko.
Thus I will make mount Seir an astonishment and a desolation, and I will cut off from it him who passes through and him who returns.
8 Ndidzaza mapiri ake ndi mitembo. Ophedwa pa nkhondo adzagwera pa zitunda zanu, zigwa zanu ndi mʼmitsinje yanu yonse.
And I will fill its mountains with its slain. In thy hills and in thy valleys and in all thy watercourses they shall fall who are slain with the sword.
9 Ndidzasandutsa dziko lanu kukhala chipululu mpaka muyaya, ndipo mʼmizinda yanu simudzakhalanso anthu. Zikadzachitika izi mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
I will make thee a perpetual desolation, and thy cities shall not be inhabited. And ye shall know that I am Jehovah.
10 “Inu munanena kuti, ‘Mitundu iwiri iyi ya anthu, Yuda ndi Israeli, pamodzi ndi mayiko awo omwe idzakhala yathu.’ Munanena chomwechi ngakhale kuti Ine Yehova ndinali momwemo.
Because thou have said, These two nations and these two countries shall be mine, and we will possess it, whereas Jehovah was there,
11 Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pali Ine wamoyo, ndithu ndidzachita nanu monga munachita ndi anthu a ku Yuda ndi Israeli poonetsa mkwiyo wanu, nsanje yanu ndi chidani chanu pa iwo. Ndikadzakulangani mudzandidziwadi pakati panupo.
therefore, as I live, says the lord Jehovah, I will do according to thine anger, and according to thine envy which thou have shown out of thy hatred against them. And I will make myself known among them when I shall judge thee.
12 Ndipo mudzadziwa kuti Ine Yehova ndinamva mawu anu onse onyoza amene munanena molimbana ndi mapiri a Israeli. Inu munati, ‘Mapiri a Israeli asanduka bwinja, ndipo aperekedwa kwa ife kuti tiwawononge.’
And thou shall know that I, Jehovah, have heard all thy revilings which thou have spoken against the mountains of Israel, saying, They are laid desolate. They are given us to devour.
13 Mawu anu amene munayankhula monyada kundinyoza Ine ndinawamva.
And ye have magnified yourselves against me with your mouth, and have multiplied your words against me. I have heard it.
14 Ine Ambuye Yehova ndikuti: Dziko lonse lapansi lidzasangalala pamene ndidzakusandutsani bwinja.
Thus says the lord Jehovah: When the whole earth rejoices, I will make thee desolate.
15 Monga momwe inu munasangalala pamene anthu anga Aisraeli anagwa, Inenso ndidzakuchitani chimodzimodzi. Udzasanduka bwinja, iwe Phiri la Seiri, iwe ndi dziko lonse la Edomu. Zikadzatero anthu onse adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”
As thou rejoiced over the inheritance of the house of Israel, because it was desolate, so I will do to thee. Thou shall be desolate, O mount Seir, and all Edom, even all of it, and they shall know that I am Jehovah.

< Ezekieli 35 >