< Ezekieli 34 >

1 Yehova anandiyankhula kuti:
And the word of Jehovah came to me, saying,
2 “Iwe mwana wa munthu, yankhula mawu oyimba mlandu abusa a Israeli. Lengeza ndipo uwawuze kuti Ine Ambuye Yehova ndikuti, ‘Tsoka kwa abusa a Israeli amene mumangodzisamala nokha! Kodi abusa sayenera kusamalira nkhosa?
Son of man, prophesy against the shepherds of Israel. Prophesy, and say to them, even to the shepherds, Thus says the Lord Jehovah: Woe to the shepherds of Israel who feed themselves! Should not the shepherds feed the sheep?
3 Mumadya chambiko, mumadziveka zovala zaubweya, ndi kupha nyama zonenepa, koma simusamalira nkhosazo.
Ye eat the fat, and ye clothe yourselves with the wool. Ye kill the fatlings, but ye do not feed the sheep.
4 Simunalimbitse nkhosa zofowoka, kapena kuchiritsa zodwala, kapena kumanga mabala a nkhosa zopweteka. Simunabweze zosochera kapena kufunafuna zotayika. Munaziweta mozunza ndi mwankhanza.
Ye have not strengthened the diseased, nor have ye healed that which was sick, nor have ye bound up that which was broken, nor have ye brought back that which was driven away, nor have ye sought that which was lost, but ye have ruled over them with force and with rigor.
5 Kotero zinabalalika chifukwa zinalibe mʼbusa, ndipo pamene zinabalalika zinakhala chakudya cha zirombo zonse zakuthengo.
And they were scattered because there was no shepherd. And they became food to all the beasts of the field, and were scattered.
6 Nkhosa zanga zinayendayenda mʼmapiri onse ndi mʼzitunda zonse zazitali. Zinabalalika pa dziko lonse lapansi, ndipo palibe amene anazilondola kapena kuzifunafuna.
My sheep wandered through all the mountains, and upon every high hill. Yea, my sheep were scattered upon all the face of the earth, and there was none who searched or sought.
7 “‘Choncho Inu abusa, tamvani zimene Ine Yehova ndikukuwuzani.
Therefore, ye shepherds, hear the word of Jehovah:
8 Pali Ine wamoyo, akutero Ambuye Wamphamvuzonse, ndithu, nkhosa zanga zinajiwa ndi zirombo zakuthengo, zinasanduka chakudya cha zirombo chifukwa panalibe abusa. Abusa anga sanafunefune nkhosa zanga. Iwo ankangosamala za iwo okha mʼmalo mosamala nkhosa zanga.
As I live, says the lord Jehovah, surely inasmuch as my sheep became a prey, and my sheep became food to all the beasts of the field, because there was no shepherd, nor did my shepherds search for my sheep, but the shepherds fed themselves, and did not feed my sheep,
9 Chifukwa chake, inu abusa, tamvani zimene Ine Yehova ndikukuwuzani.
therefore, ye shepherds, hear the word of Jehovah.
10 Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ine ndayipidwa nanu, inu abusa. Ndidzakulandani nkhosa zanga ndipo simudzazidyetsanso. Ndidzakuchotsani pa ntchito ya ubusa kuti musamangodzidyetsa nokha. Ndidzalanditsa nkhosa zanga kukamwa kwanu ndipo simudzazidyanso.
Thus says the lord Jehovah: Behold, I am against the shepherds, and I will require my sheep at their hand, and cause them to cease from feeding the sheep. Neither shall the shepherds feed themselves any more, and I will deliver my sheep from their mouth, that they may not be food for them.
11 “‘Tsono Ine Ambuye Yehova ndikuti, mwini wakene ndidzazifunafuna nkhosa zanga ndi kuzisamalira.
For thus says the lord Jehovah: Behold, I myself, even I, will search for my sheep, and will seek them out.
12 Monga mʼbusa amanka nafunafuna nkhosa zake pamene zina zabalalikira kutali, moteronso Ine ndidzafunafuna nkhosa zanga. Ndidzazipulumutsa kuchoka kumalo onse kumene zinabalalikira pa nthawi yankhungu ndi mdima.
As a shepherd seeks out his flock, in the day that he is among his sheep that are scattered abroad, so I will seek out my sheep, and I will deliver them out of all places where they have been scattered in the cloudy and dark day.
13 Ndidzazitulutsa pakati pa mitundu ya anthu ndi kuzisonkhanitsa kuchokera ku mayiko ena, ndipo ndidzazibwezera ku dziko lawo. Ndidzaziwetera ku mapiri a Israeli, mʼmbali mwa mitsinje ndi kumalo kumene kumakhala anthu.
And I will bring them out from the peoples, and gather them from the countries, and will bring them into their own land. And I will feed them upon the mountains of Israel, by the watercourses, and in all the inhabited places of the country.
14 Ndidzaziwetera kumalo a msipu wabwino. Mapiri okwera a Israeli adzakhala malo azidyetserako. Kumeneko zidzapumula ku abusa abwino a msipu ndipo zizidzadyadi msipu wonenepetsa pa mapiri a Israeli.
I will feed them with good pasture, and their fold shall be upon the mountains of the height of Israel. There they shall lie down in a good fold, and on fat pasture they shall feed upon the mountains of Israel.
15 Ine mwini wake ndidzaziweta nkhosa zanga ndi kuzilola kuti zipumule. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
I myself will be the shepherd of my sheep, and I will cause them to lie down, says the lord Jehovah.
16 Ndidzafunafuna zotayika ndi kubweza zosochera. Ndidzamanga mabala a zopweteka ndi kulimbikitsa zofowoka. Koma zonenepa ndi zamphamvu ndidzaziwononga. Ndidzaweta nkhosazo mwachilungamo.
I will seek that which was lost, and will bring back that which was driven away, and will bind up that which was broken, and will strengthen that which was sick, but I will destroy the fat and the strong. I will feed them in justice.
17 “‘Kunena za inu, nkhosa zanga, Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndidzaweruza pakati pa nkhosa ndi nkhosa, pakati pa nkhosa zazimuna ndi mbuzi zazimuna.
And as for you, O my flock, thus says the lord Jehovah: Behold, I judge between sheep and sheep, the rams and the he-goats.
18 Kodi sikukukwanirani kudya msipu wabwino kuti muzichita kuponderezanso msipu umene simunadyewo? Kodi simukhutira ndi kumwa madzi abwino kuti muzinka mudetsanso madzi otsalawo ndi mapazi anu?
Does it seem a small thing to you to have fed upon the good pasture, but ye must tread down with your feet the residue of your pasture, and to have drunk of the clear waters, but ye must foul the residue with your feet?
19 Kodi nkhosa zanga zidye zimene mwazipondaponda ndi kumwa madzi amene mwawadetsa ndi mapazi anu?
And as for my sheep, they eat that which ye have trodden with your feet, and they drink that which ye have fouled with your feet.
20 “‘Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Taonani, Ine mwini wake ndidzaweruza pakati pa nkhosa zonenepa ndi nkhosa zowonda.
Therefore thus says the lord Jehovah to them: Behold, I, even I, will judge between the fat sheep and the lean sheep.
21 Popeza zofowoka mumaziwomba ndi kuzikankhira kumbali, ndipo mumazigunda ndi nyanga zanu nʼkuzimwazira kutali,
Because ye thrust with side and with shoulder, and push all the diseased with your horns, till ye have scattered them abroad,
22 tsono Ine ndidzapulumutsa nkhosa zanga, ndipo sindidzalolanso kuti zijiwe. Ndidzaweruza pakati pa nkhosa ina ndi nkhosa inanso.
therefore I will save my flock, and they shall no more be a prey. And I will judge between sheep and sheep.
23 Ndidzaziyikira mʼbusa mmodzi, mtumiki wanga Davide. Iyeyo ndiye azidzazisamala. Adzakhala mʼbusa wawo.
And I will set up one shepherd over them, and he shall feed them, even my servant David. He shall feed them, and he shall be their shepherd.
24 Ine Yehova ndidzakhala Mulungu wake ndipo mtumiki wanga Davide adzakhala mfumu pakati pa nkhosazo. Ine Yehova ndayankhula.
And I, Jehovah, will be their God, and my servant David ruler among them. I, Jehovah, have spoken it.
25 “‘Ndidzapangana nazo pangano la mtendere. Ndidzachotsa mʼdzikomo zirombo zolusa. Choncho nkhosa zanga zidzakhala mu mtendere mu chipululu ngakhalenso mʼthengo.
And I will make a covenant of peace with them, and will cause evil beasts to cease out of the land, and they shall dwell securely in the wilderness, and sleep in the woods.
26 Ndidzakhazika anthu anga pafupi ndi phiri langa loyera ndipo ndidzawadalitsa. Ndidzawagwetsera mvula pa nthawi yake ndipo idzakhala mvula ya madalitso.
And I will make them and the places round about my hill a blessing, and I will cause the shower to come down in its season; there shall be showers of blessing.
27 Mitengo ya mʼminda idzabereka zipatso zake, ndipo nthaka idzakhala ndi zokolola zake. Anthu adzakhala mwamtendere mʼdziko lawo. Iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova, pamene ndidzathyola magoli awo ndi kuwapulumutsa kuchoka mʼmanja mwa amene anawagwira ukapolo.
And the tree of the field shall yield its fruit, and the earth shall yield its increase, and they shall be secure in their land. And they shall know that I am Jehovah when I have broken the bars of their yoke, and have delivered them out of the hand of those who made bondmen of them.
28 Anthu amitundu ina sadzawafunkhanso ndipo sadzadyedwa ndi zirombo zakuthengo. Adzakhala mwamtendere ndipo palibe amene adzawaopseze.
And they shall no more be a prey to the nations, nor shall the beasts of the earth devour them, but they shall dwell securely, and none shall make them afraid.
29 Ndidzawapatsa zokolola zochuluka motero kuti sadzavutikanso ndi njala. Anthu a mitundu ina sadzawanyozanso.
And I will raise up to them a plantation for renown, and they shall no more be consumed with famine in the land, nor bear the shame of the nations any more.
30 Pamenepo iwo adzadziwa kuti Ine Yehova Mulungu wawo ndili nawo pamodzi, ndipo kuti iwo, Aisraeli, ndi anthu anga. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
And they shall know that I, Jehovah, their God am with them, and that they, the house of Israel, are my people, says the lord Jehovah.
31 Inu ndinu nkhosa zanga, nkhosa zimene ndimazidyetsa. Ine ndine Mulungu wanu. Ndikutero Ine Ambuye Wamphamvuzonse.’”
And ye my sheep, the sheep of my pasture, are men, and I am your God, says the lord Jehovah.

< Ezekieli 34 >