< Ezekieli 37 >

1 Dzanja la Yehova linali pa ine, ndipo Mzimu wa Yehova unandinyamula nʼkukandikhazika pakati pa chigwa. Chigwacho chinali chodzaza ndi mafupa.
The hand of Jehovah was upon me, and he brought me out in the Spirit of Jehovah, and set me down in the midst of the valley, and it was full of bones.
2 Yehova anandiyendetsa uku ndi uku pakati pa mafupawo. Mafupawo anali ochuluka kwambiri mʼchigwa monsemo ndipo anali owuma kwambiri.
And he caused me to pass by them round about. And, behold, there were very many in the open valley, and, lo, they were very dry.
3 Tsono Yehova anandifunsa kuti, “Iwe mwana wa munthu, kodi mafupa amenewa angakhalenso ndi moyo?” Ndinayankha kuti, “Inu Ambuye Yehova, Inuyo nokha ndiye mukudziwa.”
And he said to me, Son of man, can these bones live? And I answered, O lord Jehovah, thou know.
4 Pamenepo anandiwuza kuti, “Lengeza kwa mafupa amenewa ndi kuwawuza kuti amve mawu a Ine Yehova!
Again he said to me, Prophesy over these bones, and say to them, O ye dry bones, hear the word of Jehovah.
5 Uwawuze kuti zimene Ine Ambuye Yehova ndikunena kwa mafupa ndi izi: Ndidzawuzira mpweya mwa inu, ndipo mudzakhalanso ndi moyo.
Thus says the lord Jehovah to these bones: Behold, I will cause breath to enter into you, and ye shall live.
6 Ndidzakupatsani mitsempha ndi mnofu. Ndiponso ndidzakukutani ndi khungu. Pambuyo pake ndidzawuzira mpweya mwa inu ndipo mudzakhalanso ndi moyo. Pamenepo mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”
And I will lay sinews upon you, and will bring up flesh upon you, and cover you with skin, and put breath in you, and ye shall live. And ye shall know that I am Jehovah.
7 Ndipo ndinanenera monga anandilamulira. Ndipo pamene ndinkanenera, ndinamva gobedegobede, ndipo mafupa aja anayamba kulumikizana, fupa ku fupa linzake.
So I prophesied as I was commanded. And as I prophesied, there was a noise, and, behold, an earthquake, and the bones came together, bone to its bone.
8 Ine ndinayangʼana, ndipo mitsempha ndi mnofu zinabwera pa mafupawo ndipo khungu linaphimba pamwamba pake, koma munalibe mpweya mwa iwo.
And I beheld, and, lo, there were sinews upon them, and flesh came up, and skin covered them above, but there was no breath in them.
9 Tsono Yehova anandiwuza kuti, “Nenera kwa mpweya, nenera iwe mwana wa munthu ndi kuwuza mpweya mawu a Ine Ambuye Yehova kuti, ‘Bwera kuno iwe mpweya. Bwera kuchokera ku mbali zonse zinayi ndi kudzawuzira anthu ophedwawa kuti akhalenso ndi moyo.’
Then he said to me, Prophesy to the wind. Prophesy, son of man, and say to the wind, Thus says the lord Jehovah: Come from the four winds, O breath, and breathe upon these slain, that they may live.
10 Choncho ndinanenera monga anandilamulira ndipo mpweya unalowa mwa iwo; apo anthu akufawo anakhala ndi moyo, nayimirira ndipo linali gulu lalikulu lankhondo.”
So I prophesied as he commanded me, and the breath came into them, and they lived, and stood up upon their feet, an exceedingly great army.
11 Kenaka Yehova anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, mafupa awa ndi nyumba yonse ya Israeli. Iwo amanena kuti, ‘Mafupa athu awuma ndipo chiyembekezo chathu chatayika, ife tawonongeka!’
Then he said to me, Son of man, these bones are the whole house of Israel. Behold, they say, Our bones are dried up, and our hope is lost. We are clean cut off.
12 Nʼchifukwa chake nenera ndi kuwawuza kuti, ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Inu anthu anga, ndidzafukula manda anu, ndipo ndidzakutulutsanimo ndi kukubwezerani ku dziko la Israeli.
Therefore prophesy, and say to them, Thus says the lord Jehovah: Behold, I will open your graves, and cause you to come up out of your graves, O my people, and I will bring you into the land of Israel.
13 Ndipo inu, anthu anga, mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova, pamene ndidzafukula manda anu ndikukutulutsanimo.
And ye shall know that I am Jehovah when I have opened your graves, and caused you to come up out of your graves, O my people.
14 Ine ndidzayika Mzimu wanga mwa inu ndipo mudzakhalanso ndi moyo. Pambuyo pake ndidzakulowetsani mʼdziko lanulanu. Choncho mudzadziwa kuti Ambuye Yehova ndayankhula zimenezi, ndipo ndidzazichitadi. Ndikutero Ine Yehova!’”
And I will put my Spirit in you, and ye shall live. And I will place you in your own land. And ye shall know that I, Jehovah, have spoken it and performed it, says Jehovah.
15 Yehova anandiyankhula kuti:
The word of Jehovah came again to me, saying,
16 “Iwe mwana wa munthu, tenga ndodo ndipo ulembepo kuti, ‘Ndodo ya Yuda ndi Aisraeli oyanjana nawo.’ Utengenso ndodo ina ndipo ulembepo kuti, ‘Ndodo ya Efereimu, ndiye kuti fuko la Yosefe ndi Aisraeli onse oyanjana nawo.’
And thou, son of man, take thee one stick, and write upon it, For Judah, and for the sons of Israel his companions. Then take another stick, and write upon it, For Joseph, the stick of Ephraim, and for all the house of Israel his companions.
17 Ulumikize ndodo ziwirizi kuti zikhale ndodo imodzi mʼdzanja lako.
And join them one to another into one stick for thyself, that they may become one in thy hand.
18 “Anthu a mtundu wako akadzakufunsa tanthauzo la zimenezi
And when the sons of thy people shall speak to thee, saying, Will thou not show us what thou mean by these?
19 iwe udzawawuze mawu awa a Ine Ambuye Yehova akuti, ‘Ine ndidzatenga ndodo ya Yosefe imene ili mʼdzanja la Efereimu, ndi ya mafuko a Aisraeli oyanjana naye, ndi kuyilumikiza ku ndodo ya Yuda, kuti zikhale ndodo imodzi, ndipo zidzakhaladi ndodo imodzi mʼdzanja langa!’
say to them, Thus says the lord Jehovah: Behold, I will take the stick of Joseph, which is in the hand of Ephraim, and the tribes of Israel his companions, and I will put them with it, even with the stick of Judah, and make them one stick, and they shall be one in my hand.
20 Ndodo ziwiri zimene udzalembepozo zikadzakhala mʼmanja mwako pamaso pa anthu onse,
And the sticks on which thou write shall be in thy hand before their eyes.
21 udzawawuze kuti Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndidzawachotsa Aisraeli pakati pa anthu a mitundu ina kumene anapita ku ukapolo. Ndidzawasonkhanitsa kuchokera ku mbali zonse ndi kubwera nawo ku dziko lawolawo.
And say to them, Thus says the lord Jehovah: Behold, I will take the sons of Israel from among the nations where they have gone, and will gather them on every side, and bring them into their own land.
22 Ndidzawasandutsa mtundu umodzi mʼdzikomo, pa mapiri a Israeli. Padzakhala mfumu imodzi yowalamulira, ndipo sadzakhalanso mitundu iwiri kapena kugawikana maufumu awiri.
And I will make them one nation in the land, upon the mountains of Israel, and one king shall be king to them all. And they shall no more be two nations, nor shall they be divided into two kingdoms any more at all.
23 Sadzadziyipitsanso ndi mafano awo, kapena ndi zinthu zawo zonyansa, kapenanso ndi ntchito zawo zoyipa zilizonse. Ndidzawapulumutsa ku machimo awo onse ndi kuwayeretsa. Choncho adzakhala anthu anga, ndipo Ine ndidzakhala Mulungu wawo.
Neither shall they defile themselves any more with their idols, nor with their detestable things, nor with any of their transgressions, but I will save them out of all their dwelling-places in which they have sinned, and will cleanse them. So they shall be my people, and I will be their God.
24 “‘Mtumiki wanga Davide adzakhala mfumu yawo, motero onsewa adzakhala ndi mʼbusa mmodzi. Iwo adzatsatira malamulo anga ndipo adzasamalira kusunga malangizo anga.
And my servant David shall be king over them, and they all shall have one shepherd. They shall also walk in my ordinances, and observe my statutes, and do them.
25 Iwo adzakhala mʼdziko limene ndinalipereka kwa mtumiki wanga Yakobo, dziko limene makolo anu ankakhalamo. Iwo ndi ana awo pamodzi ndi zidzukulu zawo adzakhala kumeneko ndipo Davide adzakhala mfumu yawo kwa muyaya.
And they shall dwell in the land that I have given to Jacob my servant, in which your fathers dwelt. And they shall dwell therein, they, and their sons, and their son's sons, forever. And David my servant shall be their ruler forever.
26 Ndidzachita nawo pangano lamtendere; lidzakhala pangano lamuyaya. Ndidzawakhazikitsa ndi kuwachulukitsa, ndipo ndidzayika malo anga opatulika pakati pawo kwamuyaya.
Moreover I will make a covenant of peace with them. It shall be an everlasting covenant with them, and I will place them, and multiply them, and will set my sanctuary in the midst of them for evermore.
27 Nyumba yanga yokhalamo idzakhala pakati pawo; Ine ndidzakhala Mulungu wawo, ndipo iwo adzakhala anthu anga.
My tabernacle shall also be with them, and I will be their God, and they shall be my people.
28 Pamenepo anthu a mitundu ina adzadziwa kuti Ine Yehova ndiye amene ndimasandutsa Israeli kukhala woyera, pamene malo anga opatulika adzakhala pakati pawo kwamuyaya!’”
And the nations shall know that I am Jehovah, who sanctifies Israel, when my sanctuary shall be in the midst of them for evermore.

< Ezekieli 37 >