< Ezekieli 16 >

1 Yehova anayankhula nane kuti,
Again the word of Jehovah came to me, saying,
2 “Iwe mwana wa munthu, udzudzule Yerusalemu za ntchito zake zonyansa.
Son of man, cause Jerusalem to know her abominations,
3 Umuwuze kuti, ‘Ambuye Yehova akukuwuza, iwe Yerusalemu kuti: Kwawo kwa makolo ako ndi ku Kanaani ndipo iwe unabadwira komweko. Abambo ako anali Mwamori, amayi ako anali Mhiti.
and say, Thus says the lord Jehovah to Jerusalem: Thy birth and thy nativity is from the land of the Canaanite. The Amorite was thy father, and thy mother was a Hittite.
4 Pa tsiku lomwe unabadwa sanadule mchombo wako. Sanakusambitse mʼmadzi kuti uyere. Sanakuthire mchere kapena kukukulunga mʼnsalu.
And as for thy nativity, in the day thou were born thy navel was not cut, nor were thou washed in water to cleanse thee. Thou were not salted at all, nor swaddled at all.
5 Palibe ndi mmodzi yemwe anakusamala kapena kukumvera chisoni kuti akuchitire zimenezi. Mʼmalo mwake anakutaya panja poyera, chifukwa ananyansidwa nawe pa tsiku lako lobadwa.
No eye pitied thee, to do any of these things to thee, to have compassion upon thee, but thou were cast out in the open field. For thy person was abhorred, in the day that thou were born.
6 “‘Tsono pamene ndinkadutsa, ndinakuona ukuvimvinizika mʼmagazi ako. Ndinakuyankhula uli mʼmagazi ako omwewo kuti, ‘Khala ndi moyo,’
And when I passed by thee, and saw thee weltering in thy blood, I said to thee, in thy blood, Live! Yea, I said to thee, in thy blood, Live!
7 ndi kuti ukule ngati mbewu ya mʼmunda. Iwe unakula ndipo unatalika ndi kutha msinkhu. Mawere ako anayamba kumera ndi tsitsi lakonso linayamba kutalika. Komabe unali wamaliseche ndi wausiwa.
I caused thee to multiply as that which grows in the field, and thou increased and grew great. And thou attained to excellent ornament, thy breasts were fashioned, and thy hair was grown. Yet thou were naked and bare.
8 “‘Tsono pamene ndinkadutsanso ndinaona kuti nthawi yako yomanga banja inakwana. Tsono ndinakufunditsa chovala changa ndi kubisa umaliseche wako. Ndinachita nawe pangano la ukwati ndipo unakhala wanga, akutero Ambuye Wamphamvuzonse.
Now when I passed by thee, and looked upon thee, behold, thy time was the time of love. And I spread my skirt over thee, and covered thy nakedness. Yea, I swore to thee, and entered into a covenant with thee, says the lord Jehovah, and thou became mine.
9 “‘Ine ndinakusambitsa mʼmadzi kutsuka magazi ako ndikukudzoza mafuta.
Then I washed thee with water. Yea, I thoroughly washed away thy blood from thee, and I anointed thee with oil.
10 Ndinakuveka zovala zopetapeta ndi nsapato za chikopa. Ndinakuveka zovala zabafuta ndi kukuveka zovala za bafuta.
I also clothed thee with embroidered work, and shod thee with a certain skin. And I girded thee around with fine linen, and covered thee with silk.
11 Ndinakukongoletsa ndi zokometsera zamtengowapatali: ndinakuveka zibangiri mʼmanja mwako ndi mkanda mʼkhosi mwako,
And I decked thee with ornaments, and I put bracelets upon thy hands, and a chain on thy neck.
12 ndipo ndinakuveka chipini pa mphuno yako, ndolo ku makutu ako ndiponso chipewa chaufumu pa mutu wako.
And I put a ring upon thy nose, and earrings in thine ears, and a beautiful crown upon thy head.
13 Choncho unavala zokongoletsa zagolide ndi siliva. Zovala zako zinali zabafuta, zasilika ndi za nsalu zopetapeta. Chakudya chako chinali ufa wosalala uchi ndi mafuta a olivi. Motero unakhala wokongola kwambiri ndipo unasanduka mfumukazi.
Thus thou were decked with gold and silver, and thy raiment was of fine linen, and silk, and embroidered work. Thou ate fine flour, and honey, and oil. And thou were very beautiful, and thou prospered to royalty.
14 Ndipo mbiri ya kukongola kwako inawanda pakati pa anthu a mitundu ina, chifukwa ulemerero umene ndinakupatsa unapititsa patsogolo kukongola kwako, akutero Ambuye Yehova.
And thy renown went forth among the nations for thy beauty. For it was perfect, through my majesty which I had put upon thee, says the lord Jehovah.
15 “‘Koma iwe unatama kukongola kwako ndipo unayamba kuchita zadama chifukwa cha kutchuka kwako. Unkachita chigololo ndi kumangodzipereka kwa aliyense wodutsa ndipo kukongola kwako kunakhala kwake.
But thou trusted in thy beauty, and played the harlot because of thy renown, and poured out thy whoredoms on everyone who passed by; his it was.
16 Unatenga zovala zako zina nukakongoletsera malo opembedzerako mafano, ndipo kumeneko umachitirako zigololo. Zinthu izi sizinachitikepo nʼkale lomwe ndipo sizidzachitikanso.
And thou took of thy garments, and made high places for thee, decked with various colors, and played the harlot upon them, things which should not come, nor should it be.
17 Unatenga zokongoletsera zopangidwa ndi golide ndi siliva zimene ndinakupatsa ndipo unadzipangira wekha mafano aamuna amene unkachita nawo za dama.
Thou also took thy fair jewels of my gold and of my silver, which I had given thee, and made for thee images of men, and played the harlot with them.
18 Ndipo iwe unatenga zovala zako zopetapeta ndi kuveka mafano. Mafuta anga ndi lubani wanga unapereka kwa mafanowo.
And thou took thy embroidered garments, and covered them, and set my oil and my incense before them.
19 Chakudya chimene ndinakupatsa, ufa, mafuta ndi uchi, zimene ndinkakudyetsa nazo unazitenga nʼkuzipereka kwa mafanowo ngati nsembe ya fungo lokoma. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
My bread also which I gave thee, fine flour and oil and honey, with which I fed thee, thou even set it before them for a sweet savor, and thus it was, says the lord Jehovah.
20 “‘Ndipo unatenga ana ako aamuna ndi ana aakazi amene unandibalira ine, ndipo unakawapereka ngati nsembe kwa mafanowo. Kodi zigololo zakozo sizinakukwanire
Moreover thou have taken thy sons and thy daughters, whom thou have borne to me, and thou have sacrificed these to them to be devoured. Were thy whoredoms a small matter,
21 kuti uziphanso ana anga ndi kuwapereka ngati nsembe kwa mafano akowo?
that thou have slain my children, and delivered them up, in causing them to pass through the fire to them?
22 Chifukwa cha zadama zako zonyansazi unayiwala masiku a ubwana wako pamene unali wamaliseche, wausiwa ndiponso womangovivinizika mʼmagazi.
And in all thine abominations and thy whoredoms thou have not remembered the days of thy youth when thou were naked and bare, and were weltering in thy blood.
23 “‘Tsoka! Tsoka kwa iwe, akutero Ambuye Yehova chifukwa powonjezera pa zoyipa zako zonse,
And it has come to pass according to all thy wickedness, (woe, woe to thee! says the lord Jehovah),
24 wadzimangira wekha nsanja ndi guwa pa mabwalo onse.
that thou have built thyself a vaulted place, and have made thee a lofty place in every street.
25 Pa msewu uliwonse wamanga nsanjazo. Motero wanyazitsa kukongola kwako podzipereka kwa aliyense amene adutsapo.
Thou have built thy lofty place at the head of every way, and have made thy beauty an abomination. And have opened thy feet to everyone who passed by, and multiplied thy whoredom.
26 Umachita chigololo ndi Aigupto, anthu adama oyandikana nawe. Choncho unandikwiyitsa chifukwa unachulukitsa za dama zako.
Thou have also committed fornication with the Egyptians, thy neighbors, great of flesh, and have multiplied thy whoredom, to provoke me to anger.
27 Nʼchifukwa chake ndinatambasula dzanja langa kukukantha ndi kuchepetsa dziko lako. Ndinakupereka kwa adani ako, Afilisti amene amayipidwa ndi makhalidwe ako onyansa.
Behold therefore, I have stretched out my hand over thee, and have diminished thy portion, and delivered thee to the will of those who hate thee, the daughters of the Philistines, who are ashamed of thy lewd way.
28 Chifukwa cha chilakolako chako unachitanso zadama ndi Aasiriya. Ngakhale unachita nawo chigololo koma sunakhutitsidwebe.
Thou have played the harlot also with the Assyrians, because thou were insatiable. Yea, thou have played the harlot with them, and yet thou were not satisfied.
29 Choncho unapitirirabe kuchita chigololo ndi Ababuloni, anthu a mʼdziko lokonda zamalonda. Ngakhale unachita izi, komabe sunakhutitsidwe.
Thou have moreover multiplied thy whoredom to the land of traffic, to Chaldea, and yet thou were not satisfied with this.
30 “‘Ambuye Yehova akuti: Mtima wako ndi wofowoka kwambiri chifukwa unachita zonsezo monga ngati mkazi wopanga manyazi.
How weak is thy heart, says the lord Jehovah, seeing thou do all these things, the work of an impudent harlot,
31 Unamanga nsanja pa msewu uliwonse. Unamanganso kachisi pabwalo lililonse. Komabe sunachite ngati mkazi wadama chifukwa unakana malipiro.
in that thou build thy vaulted place at the head of every way, and make thy lofty place in every street. And have not even been as a harlot, in that thou scorn hire.
32 “‘Iwe mkazi wachigololo! Umakonda amuna achilendo kupambana mwamuna wakowako!
A wife who commits adultery, who takes strangers instead of her husband!
33 Amuna ndiwo amapereka malipiro kwa mkazi wadama. Koma iwe ndi amene ukupereka mphatso kwa zibwenzi zako zonse. Choncho umazinyengerera kuti zizibwera kwa iwe kuchokera mbali zonse kudzagona nawe.
They give gifts to all harlots, but thou give thy gifts to all thy lovers, and bribe them, that they may come to thee on every side for thy whoredoms.
34 Chotero iwe ukusiyana ndi akazi ena achigololo, pakuti palibe amene ankakunyengerera kuti uchite naye chigololo. Iweyo ndiye unkapereka ndalama osati ena kukupatsa ndalama ayi. Motero unalidi wosiyana kwambiri ndi akazi ena.
And thou are different from other women in thy whoredoms, in that none follows thee to play the harlot. And whereas thou give a wage, and no wage is given to thee, therefore thou are different.
35 “‘Tsono mkazi wachigololo iwe, imva mawu a Yehova!
Therefore, O harlot, hear the word of Jehovah.
36 Ambuye Yehova akuti, popeza unavula ndi kuonetsa umaliseche wako mopanda manyazi, unachita chigololo ndi zibwenzi zako pamodzi ndi mafano ako onyansa, komanso popeza unapereka ana ako kuti aphedwe ngati nsembe zoperekedwa kwa mafano,
Thus says the lord Jehovah: Because thy filthiness was poured out, and thy nakedness uncovered through thy whoredoms with thy lovers, and because of all the idols of thy abominations, and for the blood of thy sons, that thou gave to them,
37 nʼchifukwa chake Ine ndidzasonkhanitsa zibwenzi zako zonse, zimene unkasangalala nazo, amene unkawakonda ndi amene unkawada. Ndidzawasonkhanitsa motsutsana nawe kuchokera ku madera onse okuzungulira ndipo Ine ndidzakuvula pamaso pawo, ndipo iwo adzaona umaliseche wako wonse.
therefore, behold, I will gather all thy lovers, with whom thou have taken pleasure, and all those whom thou have loved, with all those whom thou have hated, I will even gather them against thee on every side. And I will uncover thy nakedness to them, that they may see all thy nakedness.
38 Ine ndidzakulanga monga mmene amalangira akazi amene amachita chigololo ndiponso opha anthu. Chifukwa cha ukali wanga ndi nsanje yanga, ndidzakhetsa magazi ako mokwiya kwambiri.
And I will judge thee, as women who break wedlock and shed blood are judged. And I will bring upon thee the blood of wrath and jealousy.
39 Ndidzakupereka mʼmanja mwa zibwenzi zako ndi kuwononga nyumba zopembedzera mafano ako. Iwo adzakuvula zovala zako ndi kutenga zodzikometsera zako zabwino. Choncho adzakusiya wa maliseche ndi wausiwa.
I will also give thee into their hand, and they shall throw down thy vaulted place, and break down thy lofty places. And they shall strip thee of thy clothes, and take thy fair jewels, and they shall leave thee naked and bare.
40 Iwo adzabweretsa gulu la anthu limene lidzakuponya miyala ndi kukutematema ndi malupanga awo.
They shall also bring up a company against thee, and they shall stone thee with stones, and thrust thee through with their swords.
41 Adzatentha nyumba zako ndi kukulanga iwe pamaso pa akazi ambiri. Ndidzathetsa chigololo chako, ndipo sudzalipiranso zibwenzi zako.
And they shall burn thy houses with fire, and execute judgments upon thee in the sight of many women. And I will cause thee to cease from playing the harlot, and thou shall also give no wage any more.
42 Ukali wanga udzalekera pamenepo ndipo sindidzakuchitiranso nsanje. Ndidzakhala chete osakwiyanso.
So I will cause my wrath toward thee to rest, and my jealousy shall depart from thee, and I will be quiet, and will no more be angry.
43 “‘Popeza sunakumbukire masiku a ubwana wako koma unandikwiyitsa ndi zinthu zonsezi, Ine ndidzakubwezera ndithu chilango pamutu pako chifukwa cha zimene wachita, akutero Ambuye Yehova. Paja unawonjezera chigololo pa machitidwe ako onyansa.
Because thou have not remembered the days of thy youth, but have raged against me in all these things, therefore, behold, I also will bring thy way upon thy head, says the lord Jehovah. And thou shall not commit this lewdness with all thine abominations.
44 “‘Taona, onse onena miyambi adzakuphera mwambi wakuti, ‘Make mbuu, mwana mbuu.’
Behold, everyone who uses proverbs shall use this proverb against thee, saying, As is the mother, so is her daughter.
45 Ndiwedi mwana weniweni wamkazi wa mayi wako, amene amanyoza mwamuna wake ndi ana ake. Ndiwe mʼbale weniweni wa abale ako, amene amanyoza amuna awo ndi ana awo. Amayi ako anali Mhiti ndipo abambo ako anali Mwamori.
Thou are the daughter of thy mother, who loathes her husband and her sons. And thou are the sister of thy sisters, who loathed their husbands and their sons. Your mother was a Hittite, and your father an Amorite.
46 Mkulu wako anali Samariya, ndipo iye pamodzi ndi ana ake aakazi ankakhala cha kumpoto kwako. Mngʼono wako, Sodomu ankakhala cha kummwera kwako pamodzi ndi ana ake aakazi.
And thine elder sister is Samaria, who dwells at thy left hand, she and her daughters. And thy younger sister, who dwells at thy right hand, is Sodom and her daughters.
47 Iwe sunangotsatira kokha njira zawo zoyipa ndi kuchita zonyansa zawo, koma patangopita nthawi pangʼono machitidwe ako oyipa anaposa awo.
Yet thou have not walked in their ways, nor done according to their abominations, but, like it was a very little thing, thou were more corrupt than they in all thy ways.
48 Ndithu pali Ine wamoyo, akutero Ambuye Yehova, ngakhale mʼbale wako Sodomu ndi ana ake aakazi sanachitepo zimene iwe ndi ana ako aakazi munachita.
As I live, says the lord Jehovah, Sodom thy sister has not done, she nor her daughters, as thou have done, thou and thy daughters.
49 “‘Tsono tchimo la mʼbale wako Sodomu linali ili: Iye ndi ana ake aakazi ankanyadira kuchuluka kwa chakudya ndi chuma chawo. Koma sanalabadireko kuthandiza osauka ndi aumphawi.
Behold, this was the iniquity of thy sister Sodom: pride, fullness of bread, and prosperous ease was in her and in her daughters, and she did not strengthen the hand of a poor and needy man.
50 Anali odzitukumula ndipo ankachita zonyansa pamaso panga. Nʼchifukwa chake ndinawachotsa monga mmene waoneramu.
And they were haughty, and committed abomination before me. Therefore I took them away as I saw fit.
51 Samariya sanachite ngakhale theka la machimo amene unachita. Iwe wachita zinthu zonyansa zambiri kuposa iwo, motero kuti abale ako awiriwo amaoneka ngati olungama kuyerekeza ndi iye.
Neither has Samaria committed half of thy sins, but thou have multiplied thine abominations more than they, and have justified thy sisters by all thine abominations which thou have done.
52 Tsono iwenso uyenera kuchita manyazi popeza waonetsa abale ako ngati osachimwa. Popeza kuti machimo ako ndi onyansa kwambiri kupambana awo, tsonotu iwowo akuoneka olungama kupambana iweyo. Choncho iwenso uchite manyazi ndi kunyozedwa popeza unaonetsa abale ako ngati olungama.
Thou also, bear thou thine own shame, in that thou have given judgment for thy sisters, through thy sins that thou have committed more abominable than they. They are more righteous than thou. Yea, be thou also confounded, and bear thy shame, in that thou have justified thy sisters.
53 “‘Koma, ndidzadalitsanso Sodomu ndi ana ake aakazi. Ndidzadalitsanso Samariya ndi ana ake aakazi. Pa nthawi yomweyo ndidzakudalitsanso iwe Yerusalemu.
And I will turn back again their captivity, the captivity of Sodom and her daughters, and the captivity of Samaria and her daughters, and the captivity of thy captives in the midst of them,
54 Ndidzatero kuti uchite manyazi ndi kunyozeka chifukwa cha zonse zimene unachita powatonthoza anthuwa.
that thou may bear thine own shame, and may be ashamed because of all that thou have done, in that thou are a comfort to them.
55 Motero mʼbale wako Sodomu ndi ana ake akadzakhala monga mmene analili poyamba paja, ndiponso mʼbale wako Samariya akadzakhalanso monga mmene anali poyamba paja, ndiye kuti iwenso ndi ana ako mudzakhala monga mmene munalili payamba paja.
And thy sisters, Sodom and her daughters, shall return to their former estate, and Samaria and her daughters shall return to their former estate, and thou and thy daughters shall return to your former estate.
56 Kale lija pamene unkanyada, suja unkanyogodola mʼbale wako Sodomu
For thy sister Sodom was not mentioned by thy mouth in the day of thy pride,
57 kuyipa kwako kusanadziwike? Koma tsopano wafanana naye. Wasandukano chinthu chonyozeka kwa anthu a ku Edomu ndi kwa onse owazungulira ndiponso kwa Afilisti. Ndithu onse amene akuzungulira amakunyoza.
before thy wickedness was uncovered, as at the time of the reproach of the daughters of Syria, and of all who are round about her, the daughters of the Philistines, who do despite to thee round about.
58 Choncho udzalangidwa chifukwa cha zigololo zako ndi machitidwe anu onyansa, akutero Yehova.
Thou have borne thy lewdness and thine abominations, says Jehovah.
59 “‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndidzakulanga molingana ndi zimene unachita. Iwe unanyoza lumbiro lako pophwanya pangano langa.
For thus says the lord Jehovah: I will also deal with thee as thou have done, who have despised the oath in breaking the covenant.
60 Komabe, Ine ndidzakumbukira pangano limene ndinachita nawe mʼmasiku a unyamata wako, ndipo ndidzakhazikitsa pangano losatha ndi iwe.
Nevertheless I will remember my covenant with thee in the days of thy youth, and I will establish to thee an everlasting covenant.
61 Tsono udzakumbukira njira zako zakale. Udzachita manyazi polandiranso abale ako, wamkulu ndi wamngʼono yemwe. Ndidzawaperekanso kwa iwe kuti akhale ngati ana ako ngakhale kuti sali a mʼpangano langa ndi iwe.
Then thou shall remember thy ways, and be ashamed, when thou shall receive thy sisters, thine elder sisters and thy younger, and I will give them to thee for daughters, but not by thy covenant.
62 Kotero ndidzakhazikitsa pangano langa ndi iwe, ndipo iwe udzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
And I will establish my covenant with thee, and thou shall know that I am Jehovah,
63 Ndikadzakukhululukira zoyipa zako zonse zimene unachita, udzazikumbukira ndipo udzachita manyazi kwambiri, kotero kuti sudzatha nʼkuyankhula komwe, akutero Ambuye Yehova.’”
that thou may remember, and be confounded, and never open thy mouth any more, because of thy shame, when I have forgiven thee all that thou have done, says the lord Jehovah.

< Ezekieli 16 >