< Ezekieli 15 >

1 Yehova anayankhulanso nane kuti,
And the word of Jehovah came to me, saying,
2 “Iwe mwana wa munthu, kodi mtengo wamphesa umapambana bwanji mtengo wina uliwonse? Nthambi zake zimapambana bwanji nthambi ina iliyonse.
Son of man, what is the vine tree more than any tree, the vine branch which is among the trees of the forest?
3 Mtengo umene uja nʼkupangira chiyani? Kodi anthu angathe kupangira chikhomo chokolekapo zinthu zawo?
Shall wood be taken of it to make any work? Or will men take a pin of it to hang any vessel thereon?
4 Taonani, ndi nkhuni chabe zosonkhera moto. Ukaponyedwa pa moto monga nkhuni ndi kuyaka mbali zonse ndi kusanduka makala, kodi ungagwiritsidwe ntchito ina iliyonse?
Behold, it is cast into the fire for fuel. The fire has devoured both the ends of it, and the midst of it is burned. Is it profitable for any work?
5 Ngati pamene unali wosapsa sukanatheka kuwugwiritsa ntchito, nanga bwanji utapserera ndi moto, adzawugwiritsa ntchito bwanji?
Behold, when it was whole, it was fit for no work. How much less, when the fire has devoured it, and it is burned, shall it yet be fit for any work!
6 “Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akuti, ‘Mtengo wamphesa ndidzawuponya mʼmoto monga ndimachitira ndi mitengo ina ya ku nkhalango. Momwemonso ndidzachita ndi anthu a ku Yerusalemu.
Therefore thus says the lord Jehovah: As the vine tree among the trees of the forest, which I have given to the fire for fuel, so I will give the inhabitants of Jerusalem.
7 Ndidzawalanga pamenepo ngakhale iwo atuluka pa moto, motowo udzawatenthabe. Ndipo pamene ndidzatsutsana nawo, mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
And I will set my face against them. They shall go forth from the fire, but the fire shall devour them. And ye shall know that I am Jehovah when I set my face against them.
8 Ine ndidzasandutsa dziko kukhala chipululu chifukwa anthu akhala osakhulupirika, akutero Ambuye Yehova.’”
And I will make the land desolate because they have committed a trespass, says the lord Jehovah.

< Ezekieli 15 >