< Ezekieli 1 >

1 Tsiku lachisanu la mwezi wachinayi, chaka cha makumi atatu, ine ndinali pakati pa amʼndende mʼmbali mwa mtsinje wa Kebara. Tsono kumwamba kunatsekuka ndipo ndinaona maonekedwe a Mulungu mʼmasomphenya.
Now it came to pass in the thirtieth year, in the fourth month, in the fifth day of the month, as I was among the captives by the river Chebar, that the heavens were opened, and I saw visions of God.
2 Pa tsiku lachisanu la mwezi, chaka chachisanu Yehoyakini ali mʼndende,
In the fifth day of the month, which was the fifth year of king Jehoiachin's captivity,
3 Yehova anayankhula ndi wansembe Ezekieli, mwana wa Buzi, mʼmbali mwa mtsinje wa Kebara mʼdziko la Ababuloni. Dzanja la Yehova linali pa iye kumeneko.
the word of Jehovah came expressly to Ezekiel the priest, the son of Buzi, in the land of the Chaldeans by the river Chebar, and the hand of Jehovah was there upon him.
4 Ndinayangʼana ndipo ndinangoona mphepo yamkuntho ikubwera kuchokera kumpoto. Panali mtambo waukulu wozunguliridwa ndi kuwala ndipo moto unali lawilawi kuchokera mu mtambowo. Pakati pa motowo pankaoneka ngati mkuwa wonyezimira.
And I looked, and, behold, a stormy wind came out of the north, a great cloud, with a fire enfolding itself, and a brightness round about it, and out of the midst of it, as it were glowing metal, out of the midst of the fire.
5 Mʼkatikati mwa motowo munali zinthu zinayi zamaonekedwe a nyama. Thupi lawo limaoneka ngati la munthu
And out of the midst of it came the likeness of four living creatures. And this was their appearance. They had the likeness of a man.
6 koma chilichonse chinali ndi nkhope zinayi ndiponso mapiko anayi.
And each one had four faces, and each one of them had four wings.
7 Miyendo yake inali yowongoka; mapazi ake anali a ziboda ngati phazi la mwana wangʼombe. Ndipo zibodazo zinkawala ngati mkuwa wonyezimira.
And their feet were straight feet, and the sole of their feet was like the sole of a calf's foot, and they sparkled like burnished brass.
8 Mʼmunsi mwa mapiko awo kumbali zonse zinayi, nyamazo zinali ndi manja a munthu. Zonse zinayi zinali ndi nkhope ndi mapiko,
And they had the hands of a man under their wings on their four sides. And those four had their faces and their wings thus:
9 ndipo mapiko awowo anakhudzana. Chilichonse chimapita molunjika kutsogolo; sizimatembenuka pamene zimayenda.
Their wings were joined one to another. They did not turn when they went; they went each one straight forward.
10 Nkhope zawo zimaoneka motere: Chilichonse chinali ndi nkhope ya munthu, ndipo mbali ya kumanja chilichonse chinali ndi nkhope zinayi zosiyana motere: nkhope ya munthu, nkhope ya mkango ku dzanja lamanja, nkhope ya ngʼombe ku dzanja lamanzere, ndipo kumbuyo kwake nkhope ya chiwombankhanga.
As for the likeness of their faces, they had the face of a man. And those four had the face of a lion on the right side, and those four had the face of an ox on the left side, those four also had the face of an eagle.
11 Ndi mʼmene zinalili nkhope zawo. Mapiko awo anali otambasukira mmwamba. Chamoyo chilichonse chinali ndi mapiko awiri okhudzana ndi mapiko a chinzake. Chinalinso ndi mapiko ena awiri ophimbira thupi lake.
And their faces and their wings were separate above, two wings of each one were joined one to another, and two covered their bodies.
12 Zamoyozo zinkayenda molunjika kutsogolo. Kulikonse kumene mzimu umazitsogolera kupita, nazonso zimapita kumeneko, osatembenuka pamene zikupita.
And they went each one straight forward. Where the spirit was to go, they went. They did not turn when they went.
13 Pakati pa zamayozo panali chinthu chooneka ngati makala oyaka kapena miyuni yoyaka. Moto umayendayenda pakati pa zamayozo; wowala kwambiri, ndipo mphenzi zimatuluka pakati pawo.
As for the likeness of the living creatures, their appearance was like burning coals of fire, like the appearance of torches. It went up and down among the living creatures, and the fire was bright, and out of the fire went forth lightning.
14 Zamoyozo zinkathamanga uku ndi uko ngati kungʼanima kwa mphenzi.
And the living creatures ran and returned as the appearance of a flash of lightning.
15 Pamene ndinali kuyangʼana zamoyozo, ndinangoona mikombero ndipo pansi pambali pa chamoyo chilichonse panali mkombero umodzi.
Now as I beheld the living creatures, behold, one wheel was upon the earth beside the living creatures, for each of the four faces of it.
16 Maonekedwe a mikomberoyo anali ngati mwala wonyezimira. Mikombero yonse inali yofanana ndipo mapangidwe awo anali ngati wongolowanalowana.
The appearance of the wheels and their work was like a beryl. And those four had one likeness, and their appearance and their work was as it were a wheel within a wheel.
17 Mikombero ija poyenda inkatha kupita mbali iliyonse yomwe zamoyozo zinayangʼana popanda kutembenuka.
When they went, they went in their four directions. They did not turn when they went.
18 Marimu a mikomberoyo anali aatali ndi ochititsa mantha ndipo marimu onse anayi anali ndi maso ponseponse.
As for their rims, they were high and fearful. And those four had their rims full of eyes round about.
19 Zamoyozo zinkati zikamayenda, mikomberoyo imayendanso mʼmbali mwake; ndipo zamoyozo zinkati zikamakwera mmwamba, mikomberoyo imakweranso.
And when the living creatures went, the wheels went beside them. And when the living creatures were lifted up from the earth, the wheels were lifted up.
20 Kulikonse kumene mzimu wake unkazitsogolera, zamoyozo zinkapita komweko. Ndipo mikombero ija inkapita nawo pamodzi popeza kuti mzimu wa zamoyozo ndiwo umayendetsa mikombero ija.
Wherever the spirit was to go, they went; there the spirit was to go. And the wheels were lifted up beside them, for the spirit of the living creature was in the wheels.
21 Zamoyo zija zinkati zikamayenda mikombero imayendanso. Zamoyozo zimati zikayima, nayonso mikombero inkayima. Zamoyozo zinkati zikawuluka, mikomberonso imawuluka nazo pamodzi chifukwa mzimu wa zamoyo zija ndiwo umayendetsa mikombero ija.
When those went, these went, and when those stood, these stood, and when those were lifted up from the earth, the wheels were lifted up beside them, for the spirit of the living creature was in the wheels.
22 Pamwamba pa mitu ya zamoyozo panali chinthu chonga thambo, lowala ndipo kunyezimira kwake ngati galasi loyangʼanitsa ku dzuwa, loyalidwa pamwamba pa mitu yake.
And over the head of the living creature there was the likeness of a firmament, like awesome crystal to look upon, stretched forth over their heads above.
23 Zamoyozo zinatambalitsa mapiko ake mʼmunsi mwa thambo lija, mapiko ake ena kumakhudzana, mapiko awiri kumaphimba thupi lake.
And under the firmament their wings were straight, the one toward the other. Each one had two which covered their bodies on this side, and each one had two which covered on that side.
24 Pamene zamoyo zimayenda ndimamva phokoso la mapiko ake, ngati mkokomo wa madzi ambiri, ngati liwu la Wamphamvuzonse, ngati phokoso la gulu lankhondo. Zimati zikayima zinkagwetsa mapiko ake.
And when they went, I heard the noise of their wings like the noise of great waters, like the voice of the Almighty, a noise of tumult like the noise of a host. When they stood, they let down their wings.
25 Ndipo panamveka mawu kuchokera pamwamba pa thambo la pa mitu ya zamoyo zija. Nthawi iyi nʼkuti zamoyozo zitayima ndi kugwetsa pansi mapiko ake.
And there was a voice above the firmament that was over their heads. When they stood, they let down their wings.
26 Pamwamba pa thambo la pa mitu yake panali chinthu chimene chimaoneka ngati mpando waufumu wopangidwa ndi mwala wa safiro, ndipo pamwamba pa mpando waufumuwo panali chinthu chooneka ngati munthu.
And above the firmament that was over their heads was the likeness of a throne, as the appearance of a sapphire stone. And upon the likeness of the throne was a likeness as the appearance of a man upon it above.
27 Ndinaona kuti mmwamba mwa chiwuno chake munali ngati chitsulo chowala konsekonse ngati moto. Mʼmunsi mwa chiwuno chake munalinso ngati moto wokhawokha. Kuwala kwa mphamvu kunamuzungulira munthuyo.
And I saw as it were glowing metal, as the appearance of fire within it round about, from the appearance of his loins and upward. And from the appearance of his loins and downward I saw as it were the appearance of fire. And there was brightness round about him.
28 Kuwalako kunali ndi maonekedwe a utawaleza mʼmitambo tsiku limene kwagwa mvula. Umu ndi mmene ulemerero wa Yehova umaonekera. Pamene ndinawuona ndinagwa pansi ndipo ndinamva mawu akundiyankhula.
As the appearance of the bow that is in the cloud in the day of rain, so was the appearance of the brightness round about. This was the appearance of the likeness of the glory of Jehovah. And when I saw it, I fell upon my face, and I heard a voice speaking.

< Ezekieli 1 >