< Eksodo 6 >

1 Yehova anawuza Mose kuti, “Tsopano udzaona zimene ndimuchite Farao: Chifukwa cha dzanja langa lamphamvu adzalola anthu anga kuti atuluke. Chifukwa cha dzanja langa lamphamvu adzawatulutsa mʼdziko lake.”
And Jehovah said to Moses, Now thou shall see what I will do to Pharaoh. For by a strong hand he shall let them go, and by a strong hand he shall drive them out of his land.
2 Mulungu anatinso kwa Mose, “Ine ndine Yehova.
And God spoke to Moses, and said to him, I am Jehovah.
3 Ndinaonekera kwa Abrahamu, kwa Isake ndi kwa Yakobo monga Mulungu Wamphamvuzonse, koma sindinawadziwitse dzina langa kuti ndine Yehova.
And I appeared to Abraham, to Isaac, and to Jacob, as God Almighty, but I was not known by them by my name Jehovah.
4 Ndinakhazikitsa pangano langa ndi iwo kuwalonjeza kuti ndidzawapatsa dziko la Kanaani kumene anakhalako kale ngati alendo.
And I also established my covenant with them, to give them the land of Canaan, the land of their sojourning, in which they sojourned.
5 Ndamvanso kubuwula kwa Aisraeli, amene Aigupto awayesa akapolo ndipo ndakumbukira pangano langa.”
And moreover I have heard the groaning of the sons of Israel, whom the Egyptians keep in bondage, and I have remembered my covenant.
6 “Nʼchifukwa chake nena kwa Aisraeli kuti, ‘Ine ndine Yehova, ndipo ndidzakutulutsani mʼgoli la Aigupto. Ndidzakumasulani mu ukapolo, ndidzakuwombolani ndi dzanja langa lotambasuka ndi kuchita ntchito zachiweruzo.
Therefore say to the sons of Israel, I am Jehovah. And I will bring you out from under the burdens of the Egyptians, and I will rid you out of their bondage, and I will redeem you with an outstretched arm, and with great judgments.
7 Ndidzakutengani kukhala anthu anga, ndipo Ine ndidzakhala Mulungu wanu. Pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova Mulungu wanu amene ndinakutulutsani mʼgoli la Aigupto.
And I will take you to me for a people, and I will be to you a God, and ye shall know that I am Jehovah your God, who brings you out from under the burdens of the Egyptians.
8 Ndipo ndidzakufikitsani ku dziko limene ndinalumbira kuti ndidzalipereka kwa Abrahamu, kwa Isake ndi kwa Yakobo. Ndidzakupatsani dziko limenelo kuti likhale lanu. Ine ndine Yehova.’”
And I will bring you in to the land which I swore to give to Abraham, to Isaac, and to Jacob, and I will give it to you for a heritage. I am Jehovah.
9 Mose anawafotokozera Aisraeli zimenezi, koma iwo sanamumvere chifukwa cha kukhumudwa ndi goli lankhanza.
And Moses spoke so to the sons of Israel, but they did not hearken to Moses for anguish of spirit, and for cruel bondage.
10 Kenaka Yehova anati kwa Mose,
And Jehovah spoke to Moses, saying,
11 “Pita ukawuze Farao mfumu ya Igupto kuti awalole Aisraeli atuluke mʼdziko lake.”
Go in, speak to Pharaoh king of Egypt, that he let the sons of Israel go out of his land.
12 Koma Mose ananena kwa Yehova kuti, “Ngati Aisraeli sanandimvere, Farao akandimvera chifukwa chiyani, pajatu sinditha kuyankhula bwino?”
And Moses spoke before Jehovah, saying, Behold, the sons of Israel have not hearkened to me, how then shall Pharaoh hear me, who am of uncircumcised lips?
13 Ndipo Yehova analamula Mose ndi Aaroni kuti awuze Aisraeli ndi Farao mfumu ya Igupto kuti Aisraeli ayenera kutuluka mʼdziko la Igupto.
And Jehovah spoke to Moses and to Aaron, and gave them an order to the sons of Israel, and to Pharaoh king of Egypt, to bring the sons of Israel out of the land of Egypt.
14 Atsogoleri a mafuko awo anali awa: Ana a Rubeni mwana wachisamba wa Israeli anali Hanoki, Palu, Hezironi ndi Karimi. Awa anali mafuko a Rubeni.
These are the heads of their fathers' houses. The sons of Reuben the firstborn of Israel: Hanoch, and Pallu, Hezron, and Carmi, these are the families of Reuben.
15 Ana a Simeoni anali Yemueli, Yamini, Ohadi, Yakini, Zohari ndi Saulo mwana wa kwa mkazi wa Chikanaani. Awa anali mafuko a Simeoni.
And the sons of Simeon: Jemuel, and Jamin, and Ohad, and Jachin, and Zohar, and Shaul the son of a Canaanite woman, these are the families of Simeon.
16 Mayina a ana a Levi pamodzi ndi zidzukulu zawo anali awa: Geresoni, Kohati ndi Merari. Levi anakhala ndi moyo kwa zaka 137.
And these are the names of the sons of Levi according to their generations: Gershon, and Kohath, and Merari. And the years of the life of Levi were a hundred thirty-seven years.
17 Ana a Geresoni, mwa mafuko awo, anali Libini ndi Simei.
The sons of Gershon: Libni and Shimei, according to their families.
18 Ana a Kohati anali Amramu, Izihari, Hebroni ndi Uzieli. Kohati anakhala ndi moyo zaka 133.
And the sons of Kohath: Amram, and Izhar, and Hebron, and Uzziel. And the years of the life of Kohath were a hundred thirty-three years.
19 Ana a Merari anali Mali ndi Musi. Awa anali mafuko a Levi monga mwa mibado yawo.
And the sons of Merari: Mahli and Mushi. These are the families of the Levites according to their generations.
20 Amramu anakwatira Yokobedi mlongo wa abambo ake, amene anabereka Aaroni ndi Mose. Amramu anakhala ndi moyo kwa zaka 137.
And Amram took him Jochebed his father's sister to wife, and she bore him Aaron and Moses. And the years of the life of Amram were a hundred and thirty-seven years.
21 Ana a Izihari anali Kora, Nefegi ndi Zikiri.
And the sons of Izhar: Korah, and Nepheg, and Zichri.
22 Ana a Uzieli anali Misaeli, Elizafani ndi Sitiri.
And the sons of Uzziel: Mishael, and Elzaphan, and Sithri.
23 Aaroni anakwatira Eliseba, mwana wamkazi wa Aminadabu, mlongo wa Nasoni ndipo Iye anabereka Nadabu, Abihu, Eliezara ndi Itamara.
And Aaron took him Elisheba, the daughter of Amminadab, the sister of Nahshon, to wife, and she bore him Nadab and Abihu, Eleazar and Ithamar.
24 Ana a Kora anali Asiri, Elikana ndi Abiasafu. Awa ndiwo mafuko a Kora.
And the sons of Korah: Assir, and Elkanah, and Abiasaph. These are the families of the Korahites.
25 Eliezara mwana wa Aaroni anakwatira mmodzi mwa ana aakazi a Putieli, ndipo anabereka Finehasi. Awa anali atsogoleri a mabanja a Levi, monga mwa mafuko awo.
And Eleazar Aaron's son took to him one of the daughters of Putiel to wife, and she bore to him Phinehas. These are the heads of the fathers of the Levites according to their families.
26 Aaroni ndi Mose ndi aja amene Yehova anawawuza kuti, “Tulutsani Aisraeli mu Igupto mʼmagulu awo.”
These are that Aaron and Moses, to whom Jehovah said, Bring out the sons of Israel from the land of Egypt according to their armies.
27 Mose ndi Aaroni ndiwo amene anayankhula ndi Farao mfumu ya Igupto kuti atulutse Aisraeli mu Igupto.
These are those who spoke to Pharaoh king of Egypt, to bring out the sons of Israel from Egypt. These are that Moses and Aaron.
28 Tsopano pamene Yehova anayankhula kwa Mose mu Igupto,
And it came to pass on the day when Jehovah spoke to Moses in the land of Egypt,
29 anati, “Ine ndine Yehova. Umuwuze Farao mfumu ya Igupto zonse zimene Ine ndikuwuze iwe.”
that Jehovah spoke to Moses, saying, I am Jehovah. Speak thou to Pharaoh king of Egypt all that I speak to thee.
30 Koma Mose anati kwa Yehova, “Farao akandimvera bwanji, pakuti ine sinditha kuyankhula bwino?”
And Moses said before Jehovah, Behold, I am of uncircumcised lips, and how shall Pharaoh hearken to me?

< Eksodo 6 >