< Eksodo 5 >

1 Zitachitika izi, Mose ndi Aaroni anapita kwa Farao ndipo anati, “Yehova Mulungu wa Israeli akuti, ‘Aloleni anthu anga apite, kuti akachite chikondwerero cha Ine mʼchipululu.’”
And afterward Moses and Aaron came, and said to Pharaoh, Thus says Jehovah, the God of Israel, Let my people go, that they may hold a feast to me in the wilderness.
2 Koma Farao anati, “Yehova ndani kuti ine ndimumvere ndi kulola Aisraeli kuti apite? Ine Yehova sindikumudziwa ndipo sindilola kuti Aisraeli apite.”
And Pharaoh said, Who is Jehovah, that I should hearken to his voice to let Israel go? I do not know Jehovah, and moreover I will not let Israel go.
3 Ndipo iwo anati, “Mulungu wa Ahebri anakumana nafe. Chonde tiloleni tipite ulendo wa masiku atatu ku chipululu kuti tikapereke nsembe kwa Yehova Mulungu wathu, ngati sititero iye adzatipweteka ndi miliri kapena lupanga.”
And they said, The God of the Hebrews has met with us. Let us go, we pray thee, three days' journey into the wilderness, and sacrifice to Jehovah our God, lest he fall upon us with pestilence, or with the sword.
4 Koma mfumu ya Igupto inati, “Mose ndi Aaroni, chifukwa chiyani mukuchititsa anthuwa kuti asagwire ntchito zawo? Bwererani ku ntchito zanu!”
And the king of Egypt said to them, Therefore do ye, Moses and Aaron, loose the people from their works? Get you to your burdens.
5 Ndiponso Farao anati, “Taonani, anthuwa mʼdziko muno alipo ochuluka, ndipo inu mukuwaletsa kugwira ntchito.”
And Pharaoh said, Behold, the people of the land are now many, and ye make them rest from their burdens.
6 Pa tsiku lomwelo Farao analamulira akapitawo a thangata ndi anzawo a Chiisraeli amene ankayangʼanira anthu kuti
And the same day Pharaoh commanded the taskmasters of the people, and their officers, saying,
7 “Inu musawapatsenso udzu wopangira njerwa monga mumachitira kale, iwo azipita ndi kukatenga udzu wawo.
Ye shall no more give the people straw to make brick as formerly. Let them go and gather straw for themselves.
8 Koma musawachepetsere chiwerengero cha njerwa chomwe munawalamulira kale kuti aziwumba. Iwowa ndi aulesi. Nʼchifukwa chake akulira kuti, ‘Tiloleni tipite tikapereke nsembe kwa Mulungu wathu.’
And the number of the bricks, which they made formerly, ye shall lay upon them. Ye shall not diminish any of it. For they are idle, therefore they cry, saying, Let us go and sacrifice to our God.
9 Muwakhawulitse ndi ntchito anthu amenewa kuti azitanganidwa, asakhale ndi mpata omvera zabodza.”
Let heavier work be laid upon the men, that they may labor in it, and let them not regard lying words.
10 Choncho akapitawo a thangata ndi anzawo a Chiisraeli amene ankayangʼanira anthu anapita kwa anthu aja nati, “‘Farao akuti sadzakupatsaninso udzu.
And the taskmasters of the people went out, and their officers, and they spoke to the people, saying, Thus says Pharaoh, I will not give you straw.
11 Mʼmalo mwake mupite mukadzimwetere udzu kulikonse kumene mungawupeze. Komabe ntchito yanu sichepetsedwa.’”
Go yourselves, get you straw where ye can find it, for none of your work shall be diminished.
12 Kotero anthuwo anamwazikana mʼdziko lonse la Igupto kukamweta udzu.
So the people were scattered abroad throughout all the land of Egypt to gather stubble for straw.
13 Akapitawo a thangata aja anawafulumiza anthu aja nati, “Malizani kugwira ntchito yanu ya tsiku ndi tsiku monga mmene zinalili pamene munkapatsidwa udzu.”
And the taskmasters were urgent saying, Fulfill your works, your daily tasks, as when there was straw.
14 Akapitawo a thangata a Farao ankawamenya oyangʼanira anzawo a Chiisraeli aja nawapanikiza kuti, “Chifukwa chiyani lero simunawumbe chiwerengero chovomerezeka cha njerwa monga chakale chija?”
And the officers of the sons of Israel, whom Pharaoh's taskmasters had set over them, were beaten, and demanded, Why have ye not fulfilled your task both yesterday and today, in making brick as formerly?
15 Pamenepo oyangʼanira anzawo a Chiisraeli aja anapita kukadandaula kwa Farao kuti, “Chifukwa chiyani mwachitira antchito anu zotere?
Then the officers of the sons of Israel came and cried to Pharaoh, saying, Why do thou deal thus with thy servants?
16 Antchito anu sakupatsidwa udzu, komabe akutiwuza kuti, ‘Umbani njerwa!’ Antchito anu akumenyedwa, koma cholakwa sichili ndi anthu anu.”
There is no straw given to thy servants, and they say to us, Make brick. And, behold, thy servants are beaten, but the fault it in thine own people.
17 Farao anati, “Ulesi, inu ndinu alesi! Nʼchifukwa chake mukumanena kuti, ‘Mutilole tipite kukapereka nsembe kwa Yehova.’
But he said, Ye are idle, ye are idle. Therefore ye say, Let us go and sacrifice to Jehovah.
18 Pitani tsopano kuntchito. Simudzapatsidwanso udzu komabe muyenera kuwumba muyeso wanu wovomerezeka wa njerwa.”
Go therefore now, and work, for there shall no straw be given you, yet ye shall deliver the number of bricks.
19 Oyangʼanira anzawo a Chiisraeli anazindikira kuti ali pa mavuto pamene anawuzidwa kuti, “Musachepetse chiwerengero cha njerwa chimene muyenera kuwumba tsiku lililonse.”
And the officers of the sons of Israel saw that they were in affliction, when it was said, Ye shall not diminish anything from your bricks, your daily tasks.
20 Atachoka pamaso pa Farao, anakumana ndi Mose ndi Aaroni akuwadikira,
And they met Moses and Aaron, who stood in the way, as they came forth from Pharaoh,
21 ndipo iwo anati, “Yehova akupenyeni ndi kukuweruzani popeza mwachititsa Farao ndi nduna zake kuti anyansidwe nafe ndipo mwayika lupanga mʼmanja mwawo kuti atiphe.”
and they said to them, Jehovah look upon you, and judge, because ye have made our fragrance to be abhorred in the eyes of Pharaoh, and in the eyes of his servants, to put a sword in their hand to slay us.
22 Mose anabwerera kwa Yehova ndipo anati, “Chonde Ambuye, chifukwa chiyani mukuzunza anthu anu? Kodi munanditumira zimenezi?
And Moses returned to Jehovah, and said, Lord, why have thou dealt ill with this people? Why is it that thou have sent me?
23 Chipitireni changa kwa Farao kukamuyankhula mʼdzina lanu, iye wakhala akuzunza anthuwa, ndipo inu simunawapulumutse konse anthu anu.”
For since I came to Pharaoh to speak in thy name, he has dealt ill with this people, neither have thou delivered thy people at all.

< Eksodo 5 >