< Eksodo 38 >

1 Anapanga guwa lansembe zopsereza lamatabwa amtengo wa mkesha. Linali lofanana mbali zonse. Msinkhu wake masentimita 137, mulitali mwake masentimita 229, mulifupi masentimita 229.
And he made the altar of burnt offering of acacia wood: five cubits was the length of it, and five cubits the breadth of it, foursquare, and three cubits the height of it.
2 Anapanga nyanga imodziimodzi pa ngodya zake zinayizo, kotero kuti nyangazo ndi guwalo zinali chinthu chimodzi, ndipo anakuta guwalo ndi mkuwa.
And he made the horns of it upon the four corners of it. The horns of it were of one piece with it, and he overlaid it with brass.
3 Anapanganso ziwiya zamkuwa izi zogwirira ntchito pa guwalo: miphika, mafosholo, mabeseni owazira magazi, ngowe zokowera nyama ndi zosonkhezera moto.
And he made all the vessels of the altar: the pots, and the shovels, and the basins, the flesh-hooks, and the firepans. All the vessels of it he made of brass.
4 Anapanga sefa yachitsulo chamkuwa ya guwa lansembelo kuti ikhale mmunsi mwa khoma la guwa lansembelo, kuchokera pansi mpaka pakati pa khoma la guwalo.
And he made for the altar a grating of network of brass, under the ledge around it beneath, reaching halfway up.
5 Anapanga mphete zamkuwa zinayi ndipo anazilumikiza ku ngodya zinayi za sefa ija kuti zigwire nsichi zonyamulira.
And he cast four rings for the four ends of the grating of brass, to be places for the staves.
6 Anapanga nsichi zamtengo wa mkesha ndipo anazikuta ndi mkuwa.
And he made the staves of acacia wood, and overlaid them with brass.
7 Iwo analowetsa nsichizo mʼmphetemo mbali zonse ziwiri za guwalo kuti azinyamulira. Guwalo linali lamatabwa ndi logoba mʼkati mwake.
And he put the staves into the rings on the sides of the altar, with which to bear it; he made it hollow with planks.
8 Anapanga beseni lamkuwa lokhala ndi miyendo yamkuwanso kuchokera ku magalasi oyangʼanira nkhope a amayi amene ankatumikira pa chipata cha tenti ya msonkhano.
And he made the laver of brass, and the base of it of brass, from the mirrors of the women who fasted, who fasted by the doors of the tabernacle of witness, in the day in which he set it up.
9 Kenaka anapanga bwalo la chihema. Mbali yakummwera inali yotalika mamita 46 ndipo kunali nsalu yotchinga yofewa yosalala yolukidwa bwino.
And he made the court. For the south side southward the hangings of the court were of fine twined linen, a hundred cubits,
10 Anapanganso mizati makumi awiri, matsinde makumi awiri amkuwa ndi ngowe zasiliva ndi zingwe za mizatiyo.
their pillars were twenty, and their sockets twenty, of brass. The hooks of the pillars and their bands were of silver.
11 Mbali yakumpoto inalinso yotalika mamita 46 ndipo inali ndi mizati makumi awiri, matsinde amkuwa makumi awiri, ngowe zasiliva ndi zingwe za mizatiyo.
And for the north side a hundred cubits, their pillars twenty, and their sockets twenty, of brass, the hooks of the pillars, and their bands, of silver.
12 Mbali yakumadzulo inali yotalika mamita 23 ndipo inali ndi nsalu yotchinga, mizati khumi ndi matsinde khumi. Inalinso ndi ngowe zasiliva ndi zingwe za mizatiyo.
And for the west side were hangings of fifty cubits, their pillars ten, and their sockets ten, the hooks of the pillars, and their bands, of silver.
13 Mbali yakummawa, kotulukira dzuwa, inalinso yotalika mamita 23.
And for the east side eastward fifty cubits.
14 Mbali imodzi yachipata kunali nsalu yotchinga yotalika mamita asanu ndi awiri, mizati itatu ndi matsinde atatu,
The hangings for the one side of the gate were fifteen cubits, their pillars three, and their sockets three,
15 polowera mʼbwalo panali nsalu yotchinga ya mamita asanu ndi awiri pamodzi ndi mizati itatu ndi matsinde atatu.
and so for the other side. On this hand and that hand by the gate of the court were hangings of fifteen cubits, their pillars three, and their sockets three.
16 Katani yonse yotchinga kuzungulira chihema inali yofewa, yosalala ndi yolukidwa bwino.
All the hangings of the court round about were of fine twined linen.
17 Matsinde amizati anali amkuwa. Ngowe ndi zingwe za mizati zinali zasiliva, ndipo pamwamba pa mizatiyo anakutapo siliva. Choncho mizati yonse ya bwalolo inalumikizidwa ndi zingwe zasiliva.
And the sockets for the pillars were of brass, the hooks of the pillars, and their bands, of silver, and the overlaying of their capitals, of silver. And all the pillars of the court were banded with silver.
18 Nsalu yotchinga ya pa chipata inali yamtundu wa mtambo, yapepo ndi yofiira, yofewa yosalala ndi yopangidwa ndi anthu aluso. Nsaluyo inali yotalika mamita asanu ndi anayi, molingana ndi nsalu zotchinga bwalo. Msinkhu wake unali masentimita 229,
And the screen for the gate of the court was the work of the embroiderer, of blue, and purple, and scarlet, and fine twined linen. And twenty cubits was the length, and the height in the breadth was five cubits, answerable to the hangings of the court.
19 pamodzi ndi mizati yake inayi ndi matsinde amkuwa anayi. Ngowe ndi zingwe zake zinali za siliva, ndipo pamwamba pake pa mzati anakutapo ndi siliva.
And their pillars were four, and their sockets four, of brass, their hooks of silver, and the overlaying of their capitals, and their bands, of silver.
20 Zikhomo za chihema ndi zina zonse zozungulira chihemacho zinali zamkuwa.
And all the pegs of the tabernacle, and of the court round about, were of brass.
21 Chiwerengero cha zipangizo zimene anagwiritsa ntchito popanga chihema, chihema chaumboni, zimene Mose analamulira Alevi kuti alembe motsogozedwa ndi Itamara mwana wa Aaroni, wansembe, chinali ichi:
This is the sum of the tabernacle, even the tabernacle of the testimony, as they were counted, according to the commandment of Moses, for the service of the Levites, by the hand of Ithamar, the son of Aaron the priest.
22 Bezaleli mwana wa Uri, mwana wa Huzi wa fuko la Yuda anapanga chilichonse Yehova analamulira Mose,
And Bezalel the son of Uri, the son of Hur, of the tribe of Judah, made all that Jehovah commanded Moses.
23 pamodzi ndi Oholiabu mwana wa Ahisamaki, wa fuko la Dani, wa luso la zopangapanga ndi kulemba mapulani, ndi wopanga nsalu zolukidwa bwino za mtundu wa mtambo, yapepo ndi zofiira, zofewa ndi zosalala.
And with him was Oholiab, the son of Ahisamach, of the tribe of Dan, an engraver, and a skilful workman, and an embroiderer in blue, and in purple, and in scarlet, and in fine linen.
24 Golide yense wochokera ku nsembe yoweyula amene anagwiritsa ntchito pa ntchito yonse yopanga malo wopatulika anali wolemera makilogalamu 1,000 potsata miyeso ya kumalo wopatulika.
All the gold that was used for the work in all the work of the sanctuary, even the gold of the offering, was twenty-nine talents, and seven hundred and thirty shekels, after the shekel of the sanctuary.
25 Siliva wochokera ku gulu lonse la anthu anali wolemerera makilogalamu 3,430, potsata miyeso ya ku malo wopatulika.
And the silver from those who were numbered of the congregation was a hundred talents, and a thousand seven hundred and seventy-five shekels, after the shekel of the sanctuary,
26 Munthu aliyense amapereka beka imodzi, kufanana ngati makilogalamu 6, potsata muyeso wa ku malo wopatulika. Kuchokera kwa aliyense amene anawerengedwa kuyambira zaka 20 kapena kuposerapo, amuna onse analipo 603,550.
a beka a head, that is, half a shekel, after the shekel of the sanctuary, for everyone who passed over to those who were numbered, from twenty years old and upward, for six hundred and three thousand and five hundred and fifty men.
27 Anagwiritsa ntchito siliva wolemera makilogalamu 3,400 kupanga matsinde 100 a ku malo wopatulika ndi makatani, ndipo makilogalamu 34 kupanga tsinde limodzi.
And the hundred talents of silver were for casting the sockets of the sanctuary, and the sockets of the veil, a hundred sockets for the hundred talents, a talent for a socket.
28 Makilogalamu otsalawo anagwiritsa ntchito popanga ngowe zamzati kukutira pamwamba pa mizati ndiponso kupanga zingwe zake.
And of the thousand seven hundred seventy-five shekels he made hooks for the pillars, and overlaid their capitals, and made bands for them.
29 Mkuwa ochokera ku nsembe yoweyula unali makilogalamu 2,425.
And the brass of the offering was seventy talents, and two thousand and four hundred shekels.
30 Iwo anawugwiritsa ntchito popanga matsinde a pa chipata cha tenti ya msonkhano, guwa la mkuwa pamodzi ndi sefa yake ndiponso ziwiya zonse,
And with it he made the sockets to the door of the tent of meeting, and the brazen altar, and the brazen grating for it, and all the vessels of the altar,
31 matsinde ozungulira bwalo ndiponso a pa chipata pake, ndi zikhomo zonse za tentiyo ndi matsinde a malo wozungulirapo.
and the sockets of the court round about, and the sockets of the gate of the court, and all the pegs of the tabernacle, and all the pegs of the court round about.

< Eksodo 38 >