< Eksodo 33 >

1 Ndipo Yehova anati, “Chokani pa malo ano, iwe ndi anthu amene unawatulutsa mʼdziko la Igupto. Pitani ku dziko limene ine ndinalonjeza ndi lumbiro kwa Abrahamu, Isake ndi Yakobo kuti, ‘Ine ndidzalipereka kwa zidzukulu zanu.’
And Jehovah spoke to Moses, Depart, go up from here, thou and the people that thou have brought up out of the land of Egypt, to the land of which I swore to Abraham, to Isaac, and to Jacob, saying, To thy seed will I give it.
2 Ndipo ndidzatumiza mngelo patsogolo panu kuthamangitsa Akanaani, Aamori, Ahiti, Aperezi, Ahivi ndi Ayebusi.
And I will send an agent before thee, and I will drive out the Canaanite, the Amorite, and the Hittite, and the Perizzite, the Hivite, and the Jebusite-
3 Pitani ku dziko loyenda mkaka ndi uchi. Koma ine sindidzapita nanu, chifukwa anthu inu ndinu nkhutukumve ndipo nditha kukuwonongani mʼnjiramo.”
to a land flowing with milk and honey. For I will not go up in the midst of thee, for thou are a stiff-necked people, lest I consume thee on the way.
4 Anthu atamva mawu owopsawa, anayamba kulira ndipo palibe anavala zodzikometsera.
And when the people heard these evil tidings, they mourned, and no man put his ornaments on him.
5 Pakuti Yehova anali atanena kwa Mose kuti, “Awuze Aisraeli kuti, ‘Inu ndinu nkhutukumve.’ Ngati ine ndipita ndi inu kwa kanthawi, nditha kukuwonongani. Tsopano vulani zodzikometsera zanu ndipo ine ndidzaganiza choti ndichite nanu.”
And Jehovah said to Moses, Say to the sons of Israel, Ye are a stiff-necked people. If I go up into the midst of thee for one moment, I shall consume thee. Therefore now put off thy ornaments from thee, that I may know what to do to thee.
6 Kotero Aisraeli anavula zodzikometsera zawo pa phiri la Horebu.
And the sons of Israel stripped themselves of their ornaments from mount Horeb onward.
7 Tsono Mose ankatenga tenti ndi kukayimanga kunja kwa msasa chapatalipo, ndipo ankayitcha “tenti ya msonkhano.” Aliyense wofuna kukafunsa kanthu kwa Yehova amapita ku tenti ya msonkhano kunja kwa msasa.
Now Moses used to take the tent and to pitch it outside the camp, afar off from the camp, and he called it, The tent of meeting. And it came to pass, that everyone who sought Jehovah went out to the tent of meeting, which was outside the camp.
8 Ndipo nthawi ina iliyonse imene Mose amapita ku tenti anthu onse amanyamuka ndi kuyimirira pa makomo amatenti awo, kumuyangʼana Mose mpaka atalowa mu tentimo.
And it came to pass, when Moses went out to the tent, that all the people rose up, and stood, every man at his tent door, and looked after Moses, until he was gone into the tent.
9 Mose akamalowa mu tenti, chipilala cha mtambo chimatsika ndi kukhala pa khomo pamene Yehova amayankhula ndi Mose.
And it came to pass, when Moses entered into the tent, the pillar of cloud descended, and stood at the door of the tent, and Jehovah spoke with Moses.
10 Nthawi zonse anthu akaona chipilala cha mtambo chitayima pa khomo la tentiyo amayimirira ndi kupembedza, aliyense ali pa khomo la tenti yake.
And all the people saw the pillar of cloud stand at the door of the tent. And all the people rose up and worshiped, every man at his tent door.
11 Yehova amayankhula ndi Mose maso ndi maso ngati mmene munthu amayankhulira ndi bwenzi lake. Kenaka Mose amabwerera ku msasa koma womuthandiza wake, Yoswa, mwana wa Nuni samachoka pa tentiyo.
And Jehovah spoke to Moses face to face, as a man speaks to his friend, and he turned again into the camp. But his minister Joshua, the son of Nun, a young man, did not depart out of the tent.
12 Mose anati kwa Yehova, “Inu mwakhala mukundiwuza kuti, ‘Tsogolera anthu awa,’ koma simunandiwuze amene mudzamutuma kuti apite pamodzi nane. Inu mwanena kuti, ‘Ndikukudziwa bwino kwambiri ndipo wapeza chisomo pamaso panga.’
And Moses said to Jehovah, See, thou say to me, Bring up this people, and thou have not let me know whom thou will send with me. Yet thou have said, I know thee by name, and thou have also found favor in my sight.
13 Ngati mwakondwera nane ndiphunzitseni njira zanu kuti ndikudziweni ndi kupitiriza kupeza chisomo pamaso panu. Kumbukirani kuti mtundu uwu ndi anthu anu.”
Now therefore, I pray thee, if I have found favor in thy sight, show me now thy ways, that I may know thee, to the end that I may find favor in thy sight. And consider that this nation is thy people.
14 Yehova anayankha kuti, “Ine ndemwe ndidzapita pamodzi ndi iwe, ndipo ndidzakupatsa mpumulo.”
And he said, My presence shall go with thee, and I will give thee rest.
15 Kenaka Mose anati kwa Yehova, “Ngati inu simupita nafe, musatitumize kuti tipite, kutichotsa pano.
And Moses said to him, If thy presence go not, do not carry us up from here.
16 Kodi wina adzadziwa bwanji kuti inu mwandikomera mtima pamodzi ndi anthu awa ngati simupita nafe? Kodi nʼchiyani chomwe chidzatisiyanitse pakati pa anthu onse amene ali pa dziko lapansi?”
For how shall it now be known that I have found favor in thy sight, I and thy people? Is it not in that thou go with us, so that we are separated, I and thy people, from all the people that are upon the face of the earth?
17 Ndipo Yehova anati kwa Mose, “Ine ndidzachita zimene iwe wandipempha chifukwa Ine ndikukondwera nawe, ndikukudziwa bwino lomwe.”
And Jehovah said to Moses, I will do this thing also that thou have spoken, for thou have found favor in my sight, and I know thee by name.
18 Kenaka Mose anati, “Tsopano ndionetseni ulemerero wanu.”
And he said, Show me, I pray thee, thy glory.
19 Ndipo Yehova anati, “Ine ndidzakuonetsa ulemerero wanga wonse ndipo ndidzatchula dzina langa lakuti Yehova pamaso pako. Ine ndidzachitira chifundo amene ndikufuna kumuchitira chifundo ndipo ndidzakomera mtima amene ndikufuna kumukomera mtima.”
And he said, I will make all my goodness pass before thee, and will proclaim the name of Jehovah before thee. I will be merciful to whom I may be merciful, and I will be compassionate to whomever I may be compassionate.
20 Iye anati, “Koma iwe sungaone nkhope yanga, pakuti palibe munthu amene amaona Ine nakhala ndi moyo.”
And he said, Thou cannot see my face, for man shall not see me and live.
21 Ndipo Yehova anati, “Pali malo pafupi ndi ine pomwe ungathe kuyima pa thanthwe.
And Jehovah said, Behold, there is a place by me, and thou shall stand upon the rock.
22 Pamene ulemerero wanga udutsa, ndidzakuyika mʼphanga la thanthwe ndi kukuphimba ndi dzanja langa mpaka nditadutsa.
And it shall come to pass, while my glory passes by, that I will put thee in a cleft of the rock, and will cover thee with my hand until I have passed by.
23 Kenaka ine ndidzachotsa dzanja langa ndipo iwe udzaona msana wanga, koma nkhope yanga sidzaoneka.”
And I will take away my hand, and thou shall see my back, but my face shall not be seen.

< Eksodo 33 >