< Eksodo 2 >

1 Ndipo munthu wina wa fuko la Levi anakwatira mkazi wa fuko lomwelo.
And there went a man of the house of Levi, and took to wife a daughter of Levi.
2 Mkaziyo anatenga pathupi ndipo anabereka mwana wamwamuna. Ataona kuti mwanayo anali wokongola, anamubisa kwa miyezi itatu.
And the woman conceived, and bore a son. And when she saw him that he was a goodly child, she hid him three months.
3 Koma mwanayo atafika pa msinkhu woti sakanathanso kubisidwa, amayi ake anatenga kadengu kopangidwa ndi bango nakamata phula. Kenaka anayika mwanayo mʼmenemo ndi kukamuyika pa mabango mu mtsinje wa Nailo.
And when she could no longer hide him, she took for him an ark of bulrushes, and daubed it with slime and with pitch. And she put the child in it, and laid it in the reeds by the river's edge.
4 Mlongo wake wa mwanayo anayima pataliko kuti aone chimene chidzamuchitikira mwanayo.
And his sister stood afar off, to know what would be done to him.
5 Mwana wamkazi wa Farao anapita ku mtsinje wa Nailo kukasamba ndipo adzakazi ake ankayenda mʼmbali mwa mtsinjewo. Tsono mwana wa Farao uja anaona kadenguko pakati pa mabango ndipo anatuma mdzakazi wake kuti akakatenge.
And the daughter of Pharaoh came down to bathe at the river, and her maidens walked along by the riverside. And she saw the ark among the reeds, and sent her handmaid to fetch it.
6 Iye atavundukula anaona mwana wamwamuna akungolira. Iye anamva naye chisoni mwana uja, nati, “Ameneyu ndi mmodzi mwa ana a Chihebri.”
And she opened it, and saw the child, and, behold, the babe wept. And she had compassion on him, and said, This is one of the Hebrews' children.
7 Kenaka mlongo wake wa mwanayo anafunsa mwana wa Farao kuti, “Ndingapite kukakupezerani mmodzi mwa amayi a Chihebri kuti azikakulererani mwanayu?”
Then his sister said to Pharaoh's daughter, Shall I go and call a nurse for thee from the Hebrew women, that she may nurse the child for thee?
8 Iye anayankha kuti, “Inde, pita.” Ndipo mtsikanayo anapita nakayitana amayi a mwanayo.
And Pharaoh's daughter said to her, Go. And the maiden went and called the child's mother.
9 Mwana wa Farao anati, “Tengani mwanayu mukandilerere, ndidzakulipirani.” Mayiyo anatenga mwanayo kukamulera.
And Pharaoh's daughter said to her, Take this child away, and nurse it for me, and I will give thee thy wages. And the woman took the child, and nursed it.
10 Mwanayo atakula anakamupereka kwa mwana wa Farao ndipo anakhala mwana wake. Iye anamutcha dzina lake Mose, popeza anati, “Ndinamuvuwula mʼmadzi.”
And the child grew, and she brought him to Pharaoh's daughter, and he became her son. And she called his name Moses, and said, Because I drew him out of the water.
11 Tsiku lina, Mose atakula, anapita kumene kunali anthu a mtundu wake ndipo anawaona akugwira ntchito yowawa. Iye anaona Mwigupto akumenya Mhebri, mmodzi mwa anthu a mtundu wake.
And it came to pass in those days, when Moses was grown up, that he went out to his brothers, and looked on their burdens. And he saw an Egyptian smiting a Hebrew, one of his brothers.
12 Atayangʼana uku ndi uku, naona kuti panalibe wina aliyense, Mose anamupha Mwiguptoyo ndipo anamukwirira mu mchenga.
And he looked this way and that way, and when he saw that there was no man, he smote the Egyptian, and hid him in the sand.
13 Mmawa mwake Mose anapita ndipo anaona anthu awiri a Chihebri akumenyana. Iye anafunsa amene anali wolakwa kuti, “Chifukwa chiyani ukumenya Mhebri mnzako?”
And he went out the second day, and, behold, two men of the Hebrews were striving together. And he said to him who did the wrong, Why do thou smite thy neighbor?
14 Munthu uja anati, “Kodi ndani anakuyika kuti ukhale wotilamulira ndi wotiweruza? Kodi ukufuna kundipha monga momwe unaphera Mwigupto uja?” Mose anachita mantha ndipo anati mu mtima mwake, “Chimene ndinachita chija chadziwika.”
And he said, Who made thee a prince and a judge over us? Do thou think to kill me, as thou killed the Egyptian? And Moses feared, and said, Surely the thing is known.
15 Farao atamva zimenezi anafuna kuti aphe Mose, koma Mose anathawa ndipo anapita kukakhala ku Midiyani. Ali kumeneko, tsiku lina anakhala pansi pafupi ndi chitsime.
Now when Pharaoh heard this thing, he sought to kill Moses. But Moses fled from the face of Pharaoh, and dwelt in the land of Midian, and he sat down by a well.
16 Wansembe wa ku Midiyaniko anali ndi ana aakazi asanu ndi awiri. Iwowa anabwera kudzatunga madzi ndi kudzaza mu zomwera kuti amwetse nkhosa za abambo awo.
Now the priest of Midian had seven daughters. And they came and drew water, and filled the troughs to water their father's flock.
17 Koma kunabwera abusa ena amene anathamangitsa atsikana aja. Ndiye Mose anayimirira nawathandiza atsikana aja ndi kumwetsa nkhosa zawo.
And the shepherds came and drove them away, but Moses stood up and helped them, and watered their flock.
18 Atsikana aja atabwerera kwa abambo awo Reueli, iye anawafunsa kuti, “Chifukwa chiyani lero mwabwera msanga?”
And when they came to Reuel their father, he said, How is it that ye have come so soon today?
19 Atsikanawo anayankha kuti, “Mwigupto wina ndiye watilanditsa kwa abusa. Ndiponso anatitungira madzi ndi kumwetsa ziweto zathu.”
And they said, An Egyptian delivered us out of the hand of the shepherds, and moreover he drew water for us, and watered the flock.
20 Tsono Reueli anafunsa ana ake kuti, “Ndiye ali kuti munthuyo? Chifukwa chiyani mwamusiya? Kamuyitaneni kuti adzadye.”
And he said to his daughters, And where is he? Why is it that ye have left the man? Call him, that he may eat bread.
21 Mose anavomera kukhala ndi Reueli, ndipo anamupatsa Zipora kuti akhale mkazi wake.
And Moses was content to dwell with the man, and he gave Moses Zipporah his daughter.
22 Zipora anabereka mwana wa mwamuna amene Mose anamutcha Geresomu, popeza anati, “Ndakhala mlendo mʼdziko la eni.”
And she bore a son, and he called his name Gershom, for he said, I have been a sojourner in a foreign land.
23 Nthawi yonseyo nʼkuti ana a Israeli akulira chifukwa cha ukapolo wawo uja. Iwo anafuwula kupempha thandizo, ndipo kulira kwawoko kunafika kwa Mulungu.
And it came to pass in the course of those many days, that the king of Egypt died. And the sons of Israel sighed because of the bondage, and they cried, and their cry came up to God because of the bondage.
24 Mulungu anamva kubuwula kwawo ndipo anakumbukira pangano lake ndi Abrahamu, Isake ndi Yakobo.
And God heard their groaning, and God remembered his covenant with Abraham, with Isaac, and with Jacob.
25 Mulungu ataona Aisraeli aja ndi masautso awo, Iye anawamvera chifundo.
And God saw the sons of Israel, and God took knowledge of them.

< Eksodo 2 >