< Eksodo 1 >

1 Awa ndi mayina a ana a Israeli amene anapita ku Igupto pamodzi ndi Yakobo abambo awo, aliyense ndi banja lake:
Now these are the names of the sons of Israel who came into Egypt (every man and his household who came with Jacob):
2 Rubeni, Simeoni, Levi, Yuda;
Reuben, Simeon, Levi, and Judah,
3 Isakara, Zebuloni, Benjamini;
Issachar, Zebulun, and Benjamin,
4 Dani, Nafutali; Gadi ndi Aseri.
Dan and Naphtali, Gad and Asher.
5 Anthu onse obadwa mwa Yakobo analipo 70. Yosefe nʼkuti ali kale ku Igupto.
And all the souls who came out of the loins of Jacob were seventy souls. And Joseph was in Egypt already.
6 Tsono Yosefe ndi abale ake onse ndiponso mʼbado wawo wonse anamwalira.
And Joseph died, and all his brothers, and all that generation.
7 Koma Aisraeli anaberekana ndi kuchuluka kwambiri nakhala amphamvu kwambiri, kotero kuti anadzaza dzikolo.
And the sons of Israel were fruitful, and increased abundantly, and multiplied, and grew exceedingly mighty, and the land was filled with them.
8 Pambuyo pake mfumu yatsopano imene sinkamudziwa Yosefe, inayamba kulamulira dziko la Igupto.
Now there arose a new king over Egypt, who knew not Joseph.
9 Iyo inati kwa anthu ake, “Taonani, Aisraeli achuluka ndipo ndi amphamvu kwambiri kuposa ife.
And he said to his people, Behold, the people of the sons of Israel are more and mightier than we.
10 Tiyeni tiwachenjerere. Tikapanda kutero adzachuluka kuposa ife, ndipo ngati kutakhala nkhondo, adzadziphatika kwa adani athu nadzamenyana nafe, kenaka nʼkudzachoka mʼdziko muno.”
Come, let us deal craftily with them, lest they multiply, and it come to pass, that, when war happens, they also join themselves to our enemies, and fight against us, and get them up out of the land.
11 Kotero anayika akapitawo kuti aziwazunza ndi kuwagwiritsa ntchito yolemetsa mokakamiza. Iwo anamangira Farao mizinda ya Pitomu ndi Ramesesi kumene ankasungirako chakudya.
Therefore they set taskmasters over them to afflict them with their burdens. And they built store-cities for Pharaoh, Pithom and Rameses.
12 Koma pamene ankawazunza kwambiri, Aisraeli ndiye ankachulukirachulukira mpaka kubalalikira mʼdziko lonse. Kotero Aigupto anayamba kuopa Aisraeliwo
But the more they afflicted them, the more they multiplied and the more they spread out. And they were grieved because of the sons of Israel.
13 ndipo anawagwiritsa ntchito mwankhanza kwambiri.
And the Egyptians made the sons of Israel to serve with rigor.
14 Aigupto anachititsa moyo wa Aisraeli kukhala owawa kwambiri powagwiritsa ntchito yakalavulagaga yowumba njerwa ndi kuponda dothi lomangira, pamodzi ndi ntchito zina zosiyanasiyana zamʼminda. Iwo anakakamiza Aisraeli mwankhanza kuti agwire ntchito yowawayi.
And they made their lives bitter with hard service, in mortar and in brick, and in all manner of service in the field, all their service, with which they made them serve with rigor.
15 Mfumu ya Igupto inati kwa azamba a Chihebri omwe mayina awo anali Sifira ndi Puwa,
And the king of Egypt spoke to the Hebrew midwives, of whom the name of the one was Shiphrah, and the name of the other Puah.
16 “Mukamathandiza amayi a Chihebri pa mwala wochirira, muzionetsetsa kuti akabadwa mwana wamwamuna muzipha, koma akakhala wamkazi muzimuleka akhale ndi moyo.”
And he said, When ye do the office of a midwife to the Hebrew women, and see them upon the birth-stool, if it be a son, then ye shall kill him, but if it be a daughter, then she shall live.
17 Koma azambawo ankaopa Mulungu ndipo sanachite zimene mfumu ya Igupto inawawuza kuti achite. Iwo analeka ana aamuna kuti akhale ndi moyo.
But the midwives feared God, and did not do as the king of Egypt commanded them, but saved the male children alive.
18 Kenaka mfumu ya Igupto inayitanitsa azamba aja ndi kuwafunsa kuti, “Chifukwa chiyani mwachita zimenezi? Bwanji mwasiya ana aamuna kuti akhale ndi moyo?”
And the king of Egypt called for the midwives, and said to them, Why have ye done this thing, and have saved the male children alive?
19 Azambawo anamuyankha Farao kuti, “Amayi a Chihebri sali ngati amayi a Chiigupto; Iwo ndi amphamvu ndipo amachira azamba asanafike.”
And the midwives said to Pharaoh, Because the Hebrew women are not as the Egyptian women, for they are lively, and are delivered before the midwife comes to them.
20 Kotero Mulungu anawakomera mtima azambawo, ndipo Aisraeli anapitirirabe kuchulukana nakhala amphamvu kwambiri.
And God dealt well with the midwives. And the people multiplied, and grew very mighty.
21 Pakuti azambawo ankaopa Mulungu, Iye anawapatsa mabanja awoawo.
And it came to pass, because the midwives feared God, that he made them households.
22 Pamenepo Farao analamulira anthu ake onse kuti, “Mwana wamwamuna aliyense akabadwa, mukamuponye mu mtsinje wa Nailo, koma wamkazi mulekeni akhale ndi moyo.”
And Pharaoh ordered all his people, saying, Every son that is born ye shall cast into the river, and every daughter ye shall save alive.

< Eksodo 1 >