< Eksodo 11 >

1 Tsopano Yehova anati kwa Mose, “Ine ndidzalanga Farao pamodzi ndi Aigupto onse ndi mliri umodzi wotsiriza. Zikadzachitika izi iye adzakulolani kuti mutuluke mʼdziko lino. Ndithu pamene azidzakutulutsani adzachita ngati akukuyingitsani.
And Jehovah said to Moses, Yet one plague more I will bring upon Pharaoh, and upon Egypt, afterwards he will let you go from here. When he shall let you go, he shall surely thrust you out from here altogether.
2 Awuze anthu kuti mwamuna aliyense ndi mkazi aliyense apemphe kwa mnansi wake ziwiya zasiliva ndi golide.”
Speak now in the ears of the people, and let them ask every man of his neighbor, and every woman of her neighbor, jewels of silver, and jewels of gold.
3 Tsono Yehova anachititsa Aigupto kuti akomere mtima Aisraeli. Komanso Mose anali wotchuka kwambiri mʼdziko la Igupto, pamaso pa nduna za Farao ndi anthu onse.
And Jehovah gave the people favor in the sight of the Egyptians. Moreover the man Moses was very great in the land of Egypt, in the sight of Pharaoh's servants, and in the sight of the people.
4 Tsono Mose anawuza Farao kuti, “Pakati pa usiku, Yehova adzayenda pakati pa anthu a ku Igupto.
And Moses said, Thus says Jehovah, About midnight I will go out into the midst of Egypt,
5 Ndipo mwana aliyense wamwamuna wachisamba adzafa, kuyambira mwana wamwamuna wa Farao amene amakhala pa mpando waufumu, mpaka mwana wamwamuna wachisamba wa mdzakazi wake amene ali naye pa mtondo, komanso ana oyamba a ziweto.
and all the firstborn in the land of Egypt shall die, from the firstborn of Pharaoh who sits upon his throne, even to the firstborn of the maid-servant that is behind the mill, and all the firstborn of cattle.
6 Kudzakhala kulira kwakukulu mʼdziko lonse la Igupto, kumene sikunachitikepo ndipo sikudzachitikanso.
And there shall be a great cry throughout all the land of Egypt, such as there has not been, nor shall be any more.
7 Koma pakati pa Aisraeli, ngakhale galu sadzawuwa munthu aliyense kapena chiweto!” Kotero mudzadziwa kuti Yehova ndiye wasiyanitsa pakati pa Igupto ndi Israeli.
But against any of the sons of Israel shall not a dog move his tongue, against man or beast, that ye may know how that Jehovah makes a distinction between the Egyptians and Israel.
8 Nduna zanu zonse zidzabwera kwa ine, kugwada pamaso panga ndi kunena kuti, “Pita iwe ndi anthu ako onse amene akukutsatirawa! Zimenezi zikadzachitika ine ndidzachoka.” Ndipo Mose anachoka kwa Farao atakwiya kwambiri.
And all these thy servants shall come down to me, and bow themselves down to me, saying, Get thee out, and all the people who follow thee. And after that I will go out. And he went out from Pharaoh in hot anger.
9 Yehova ananena kwa Mose kuti, “Farao adzakana kukumvera, kuti zodabwitsa zanga zichuluke mʼdziko la Igupto.”
And Jehovah said to Moses, Pharaoh will not hearken to you, that my wonders may be multiplied in the land of Egypt.
10 Mose ndi Aaroni anachita zodabwitsa zonsezi pamaso pa Farao koma Yehova anawumitsa mtima wa Farao, ndipo sanalole kuti Aisraeli atuluke mʼdziko lake.
And Moses and Aaron did all these wonders before Pharaoh. And Jehovah hardened Pharaoh's heart, and he did not let the sons of Israel go out of his land.

< Eksodo 11 >