< Mlaliki 8 >

1 Ndani angafanane ndi munthu wanzeru? Ndani angadziwe kutanthauzira zinthu? Nzeru imabweretsa chimwemwe pa nkhope ya munthu ndipo imasintha maonekedwe ake awukali.
Who is as the wise man? And who knows the interpretation of a thing? A man's wisdom makes his face to shine, and the hardness of his face is changed.
2 Ine ndikuti, mvera lamulo la mfumu, chifukwa unalumbira pamaso pa Mulungu.
I say, Keep the king's command, and that because of the oath of God.
3 Usafulumire kuchoka pamaso pa mfumu. Usawumirire chinthu choyipa, pakuti mfumu idzachita chilichonse chomwe imasangalatsidwa nacho.
Be not hasty to go out of his presence. Persist not in an evil matter, for he does whatever pleases him.
4 Popeza mawu a mfumu ali ndi mphamvu, ndani anganene kwa mfumuyo kuti, “Kodi mukuchita chiyani?”
For the king's word has power, and who may say to him, What are thou doing?
5 Aliyense amene amamvera lamulo lake sadzapeza vuto lililonse, ndipo munthu wanzeru amadziwa nthawi yoyenera ndi machitidwe ake.
He who keeps a commandment shall know no evil thing. And a wise man's heart discerns the time and decision.
6 Pakuti pali nthawi yoyenera ndiponso machitidwe a chinthu chilichonse, ngakhale kuti mavuto ake a munthu amupsinja kwambiri.
For to every purpose there is a time and decision, although the distress of man is great upon him.
7 Popeza palibe munthu amene amadziwa zamʼtsogolo, ndani angamuwuze zomwe zidzachitika mʼtsogolo?
For he knows not that which shall be, for who can tell him how it shall be?
8 Palibe munthu amene ali ndi mphamvu yolamulira mpweya wa moyo kuti athe kuwusunga, choncho palibe amene ali ndi mphamvu pa tsiku la imfa yake. Nkhondo sithawika; tsono anthu ochita zoyipa, kuyipa kwawoko sikudzawapulumutsa.
There is no man who has power over the spirit to retain the spirit, nor has he power over the day of death. And there is no discharge in war. Neither shall wickedness deliver him who is given to it.
9 Zonsezi ndinaziona pamene ndinalingalira mu mtima mwanga, zonse zimene zimachitika pansi pano. Ilipo nthawi imene ena amalamulira anzawo mwankhanza.
All this I have seen, and applied my heart to every work that is done under the sun. There is a time in which one man has power over another to his hurt.
10 Kenaka, ndinaona anthu oyipa akuyikidwa mʼmanda, iwo amene ankalowa ndi kumatuluka mʼmalo opatulika ndipo ankatamandidwa mu mzindawo pamene ankachita zimenezi. Izinso ndi zopandapake.
So I saw the wicked buried, who had come and gone from the place of the holy, and they were praised in the city where they had so done. This also is vanity.
11 Pamene chigamulo cha anthu opalamula mlandu chikuchedwa, mitima ya anthu imadzaza ndi malingaliro ochita zolakwa.
Because sentence against an evil work is not executed speedily, therefore the heart of the sons of men is fully set in them to do evil.
12 Ngakhale munthu woyipa apalamule milandu yambirimbiri, nʼkumakhalabe ndi moyo wautali, ine ndikudziwa kuti anthu owopa Mulungu zinthu zidzawayendera bwino, omwe amapereka ulemu pamaso pa Mulungu.
Though a sinner does evil a hundred times, and prolongs his days, yet surely I know that it shall be well with those who fear God, who fear before him.
13 Koma popeza oyipa saopa Mulungu zinthu sizidzawayendera bwino, ndipo moyo wawo sudzakhalitsa monga mthunzi.
But it shall not be well with a wicked man, neither shall he prolong his days, which are as a shadow, because he did not fear before God.
14 Palinso chinthu china chopanda phindu chomwe chimachitika pa dziko lapansi: anthu olungama amalangidwa ngati anthu osalungama. Pamene oyipa amalandira zabwino ngati kuti ndi anthu abwino.
There is a vanity which is done upon the earth, that there are righteous men to whom it happens according to the work of the wicked, again, there are wicked men to whom it happens according to the work of the righteous. I said that this also is vanity.
15 Nʼchifukwa chake ndikuti munthu azikondwerera moyo, pakuti munthu alibe chinanso chabwino pansi pano choposa kudya, kumwa ndi kumadzikondweretsa. Akamatero, munthuyo adzakhala ndi chimwemwe pa ntchito yake masiku onse a moyo wake amene Mulungu wamupatsa pansi pano.
Then I commended joy, because a man has no better thing under the sun, than to eat, and to drink, and to be cheerful. For that shall abide with him in his labor all the days of his life which God has given him under the sun.
16 Pamene ndinayikapo mtima wanga kuti ndidziwe nzeru ndi kuonetsetsa ntchito za munthu pa dziko lapansi, osapeza tulo usana ndi usiku,
When I applied my heart to know wisdom, and to see the business that is done upon the earth (for also there is he who sees sleep with his eyes neither day nor night),
17 pamenepo ndinaona zonse zimene Mulungu anazichita. Palibe munthu amene angathe kuzimvetsa zonse zimene zimachitika pansi pano. Ngakhale munthu ayesetse kuzifufuza, sangathe kupeza tanthauzo lake. Ngakhale munthu wanzeru atanena kuti iye amadziwa, sangathe kuzimvetsetsa zinthuzo.
then I beheld all the work of God, that man cannot find out the work that is done under the sun. Because however much a man labors to seek it out, yet he shall not find it. Yea moreover, though a wise man thinks to know it, yet he shall not be able to find it.

< Mlaliki 8 >