< Mlaliki 11 >

1 Ponya chakudya chako pa madzi, udzachipezanso patapita masiku ambiri.
Cast thy bread upon the waters, for thou shall find it after many days.
2 Ndalama zako uzisungitse kwa anthu asanu ndi awiri, inde kwa anthu asanu ndi atatu, pakuti sudziwa ndi tsoka lanji limene likubwera pa dziko.
Give a portion to seven, yea, even to eight, for thou know not what evil shall be upon the earth.
3 Ngati mitambo yadzaza ndi madzi, imagwetsa mvula pa dziko lapansi. Mtengo ukagwera cha kummwera kapena cha kumpoto, ndiye kuti udzagonera kumene wagwerako.
If the clouds are full of rain, they empty themselves upon the earth, and if a tree falls toward the south, or toward the north, in the place where the tree falls, there shall it be.
4 Amene amayangʼana mphepo sadzadzala; amene amayangʼana mitambo sadzakolola.
He who observes the wind shall not sow, and he who regards the clouds shall not reap.
5 Momwe sudziwira mayendedwe a mphepo, kapena momwe mzimu umalowera mʼthupi la mwana mʼmimba mwa amayi, momwemonso sungathe kudziwa ntchito za Mulungu, Mlengi wa zinthu zonse.
As thou know not what is the way of the wind, nor how the bones grow in the womb of her who is with child, even so thou know not the work of God who does all.
6 Dzala mbewu zako mmawa ndipo madzulo usamangoti manja lobodo, pakuti sudziwa chimene chidzapindula, mwina ichi kapena icho, kapena mwina zonse ziwiri zidzachita bwino.
In the morning sow thy seed, and in the evening withhold not thy hand, for thou know not which shall prosper, whether this or that, or whether they both shall be alike good.
7 Kuwala nʼkwabwino, ndipo maso amasangalala kuona dzuwa.
Truly the light is sweet, and a pleasant thing it is for the eyes to behold the sun.
8 Munthu akakhala wa zaka zambiri, mulekeni akondwerere zaka zonsezo, koma iye azikumbukira masiku a mdima, pakuti adzakhala ochuluka. Chilichonse chimene chikubwera ndi chopanda phindu.
Yea, if a man lives many years, let him rejoice in them all. But let him remember the days of darkness, for they shall be many. All that comes is vanity.
9 Kondwera mnyamata iwe, pamene ukanali wamngʼono, ndipo mtima wako usangalale pa nthawi ya unyamata wako. Tsatira zimene mtima wako ukufuna, ndiponso zimene maso ako akuona, koma dziwa kuti pa zinthu zonsezo Mulungu adzakuweruza.
Rejoice, O young man, in thy youth, and let thy heart cheer thee in the days of thy youth, and walk in the ways of thy heart, and in the sight of thine eyes. But know thou, that for all these things God will bring thee into judgment.
10 Choncho uchotse zokusautsa mu mtima mwako, upewe zokupweteka mʼthupi mwako, pakuti unyamata ndi ubwana ndi zopandapake.
Therefore remove sorrow from thy heart, and put away evil from thy flesh, for youth and the dawn of life are vanity.

< Mlaliki 11 >