< Deuteronomo 20 >

1 Pamene mukupita kokachita nkhondo ndi adani anu, mukaona akavalo kapena magaleta kapena gulu la ankhondo kuposa inuyo musamaope chifukwa Yehova Mulungu wanu, amene anakutulutsani ku Igupto adzakhala nanu.
When thou go forth to battle against thine enemies, and see horses, and chariots, and a people more than thou, thou shall not be afraid of them, for Jehovah thy God is with thee, who brought thee up out of the land of Egypt.
2 Pamene mwatsala pangʼono kuyamba nkhondo, wansembe azibwera kutsogolo ndipo aziyankhula ku gulu lonse lankhondolo.
And it shall be, when ye draw near to the battle, that the priest shall approach and speak to the people,
3 Iye aziti, “Tamverani inu Aisraeli, mukupita kukachita nkhondo ndi adani anu lero. Musataye mitima kapena kuchita mantha ayi. Musaopsedwe kapena kunjenjemera pamaso pawo,
and shall say to them, Hear, O Israel, ye draw near this day to battle against your enemies. Let not your heart faint. Fear not, nor tremble, neither be ye frightened at them.
4 pakuti Yehova Mulungu wanu ndiye amene apite nanu kukakumenyerani nkhondo ndi kugonjetsa adani anu.”
For Jehovah your God is he who goes with you, to fight for you against your enemies, to save you.
5 Akuluakulu ankhondo adzati kwa gulu la ankhondolo, “Kodi pali wina amene wangomanga nyumba kumene ndipo sanayitsekulire? Ayambe wapita ku mudzi chifukwa mwina akafera ku nkhondoko ndipo wina ndi kudzayitsekulira.
And the officers shall speak to the people, saying, What man is there who has built a new house, and has not dedicated it? Let him go and return to his house, lest he die in the battle, and another man dedicate it.
6 Kodi pali wina amene analima munda wamphesa ndipo sanayambe kudyerera? Ayambe wapita ku mudzi chifukwa mwina akafera ku nkhondo ndipo wina adzadyerera mundawo.
And what man is there who has planted a vineyard, and has not used the fruit of it? Let him go and return to his house, lest he die in the battle, and another man use the fruit of it.
7 Kodi pali amene wachita chinkhoswe ndi mkazi ndipo sanamukwatire mkaziyo? Ayambe wabwerera ku mudzi chifukwa mwina akafera ku nkhondo ndipo wina adzakwatira mkaziyo.”
And what man is there who has betrothed a wife, and has not taken her? Let him go and return to his house, lest he die in the battle, and another man take her.
8 Ndipo akuluakulu ankhondowo akapitirize kuti, “Kodi pali amene akuchita mantha kapena kutaya mtima? Abwerere ku mudzi kuopa kuti abale ake angatayenso mtima.”
And the officers shall speak further to the people, and they shall say, What man is there who is fearful and faint-hearted? Let him go and return to his house, lest his brother's heart melt as his heart.
9 Akuluakuluwo akatsiriza kuyankhula ndi gulu la ankhondolo, adzasankhe olilamulira.
And it shall be, when the officers have made an end of speaking to the people, that they shall appoint captains of armies at the head of the people.
10 Pamene mukuyandikira kuphwanya mzinda, muyambe mwafunsa anthu a mu mzindawo ngati afuna zamtendere.
When thou draw near to a city to fight against it, then proclaim peace to it.
11 Akavomera natsekula zipata zawo, anthu wonse mu mzindawo adzagwidwa ukapolo nakugwirirani ntchito.
And it shall be, if it makes to thee an answer of peace, and opens to thee, then it shall be, that all the people that are found in it shall become tributary to thee, and shall serve thee.
12 Koma akakana za mtendere nachita nanu nkhondo, muwuphwanye mzindawo.
And if it will make no peace with thee, but will make war against thee, then thou shall besiege it.
13 Yehova Mulungu wanu akakupatsani mzindawo, muwaphe amuna onse.
And when Jehovah thy God delivers it into thy hand, thou shall smite every male of it with the edge of the sword,
14 Akazi, ana, ziweto ndi china chilichonse mu mzindamo, mukhoza kuzitenga kuti zikhale zanu monga katundu wolanda ku nkhondo. Katundu wa adani anuyu amene Yehova Mulungu wanu akukupatsani, mukhoza kumugwiritsa ntchito.
but the women, and the little ones, and the cattle, and all that is in the city, even all the spoil of it, thou shall take for a prey to thyself. And thou shall eat the spoil of thine enemies, which Jehovah thy God has given thee.
15 Mizinda yonse yakutali osati ya mitundu yapafupi, muzichita nayo chomwechi.
Thus thou shall do to all the cities which are very far off from thee, which are not of the cities of these nations.
16 Komabe mʼmizinda imene Yehova Mulungu wanu akukupatsani ngati cholowa chanu, musasiyemo chamoyo chilichonse.
But of the cities of these peoples, that Jehovah thy God gives thee for an inheritance, thou shall save alive nothing that breathes,
17 Muwawononge kwathunthu Ahiti, Aamori, Akanaani, Aperezi, Ahivi ndi Ayebusi monga momwe Yehova Mulungu wanu anakulamulirani.
but thou shall utterly destroy them-the Hittite, and the Amorite, the Canaanite, and the Perizzite, the Hivite, and the Jebusite-as Jehovah thy God has commanded thee,
18 Mukapanda kutero adzakuphunzitsani kuti mutengere zinthu zonyansa zimene amachita popembedza milungu yawo ndipo mudzachimwira Yehova Mulungu wanu.
that they not teach you to do after all their abominations, which they have done to their gods, so ye would sin against Jehovah your God.
19 Mukalimbana ndi mzinda nthawi yayitali, kuchita nawo nkhondo pofuna kuwugonjetsa, musawononge podula mitengo yake ndi nkhwangwa, osayidula chifukwa zipatso zakezo mukhoza kudya. Kodi mitengo ya ku munda ndi anthu kuti mukalimbane nayo?
When thou shall besiege a city a long time, in making war against it to take it, thou shall not destroy the trees of it by wielding an axe against them, for thou may eat of them. And thou shall not cut them down, for is the tree of the field a man, that it should be besieged by thee?
20 Komabe mukhoza kudula mitengo imene mukudziwa kuti si ya zipatso ndi kuyigwiritsa ntchito pa nkhondo mpaka mzinda umene mukumenyana nawowo utagwetsedwa.
Only the trees of which thou know that they are not trees for food, thou shall destroy and cut them down. And thou shall build bulwarks against the city that makes war with thee, until it falls.

< Deuteronomo 20 >