< Deuteronomo 19 >

1 Yehova Mulungu wanu akadzawononga anthu amene dziko lawo akukupatsani, ndipo inu mukawapirikitsa ndi kukhazikika mʼmizinda ndi mʼnyumba zawo,
When Jehovah thy God shall cut off the nations, whose land Jehovah thy God gives thee, and thou succeed them, and dwell in their cities, and in their houses,
2 mukapatule mizinda itatu imene ili pakati pa dziko lomwe Yehova Mulungu akukupatsani kukhala lanu.
thou shall set apart three cities for thee in the midst of thy land, which Jehovah thy God gives thee to possess it.
3 Mudzakonze misewu ndi kuligawa patatu dzikolo limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani ngati cholowa chanu, kuti aliyense wopha munthu akhoza kuthawirako.
Thou shall prepare for thee the way, and divide the borders of thy land, which Jehovah thy God causes thee to inherit, into three parts, that every manslayer may flee there.
4 Ili ndi lamulo lokhudza munthu amene wapha mnzake mosazindikira osati mwadala, nathawira kumeneko kupulumutsa moyo wake. Ndi munthu amene wapha mnzake mosazindikira, popanda maganizo oyipa.
And this is the case of the manslayer, who shall flee there and live: Whoever kills his neighbor unawares, and did not hate him in time past,
5 Mwachitsanzo, munthu atapita ku nkhalango ndi mnzake kukadula mitengo, ndiye posamula nkhwangwa kuti adule mtengo, nkhwangwa ikhoza kuguluka nʼkukagwera mnzake uja nʼkumupha. Munthu ameneyo akhoza kuthawira ku umodzi mwa mizindayo napulumutsa moyo wake.
as when a man goes into the forest with his neighbor to hew wood, and his hand fetches a stroke with the axe to cut down the tree, and the head slips from the helve, and lands upon his neighbor, so that he dies, he shall flee to one of these cities and live.
6 Kupanda kutero ndiye kuti wolipsira akhoza kumuthamangitsa mwaukali ndi kumugwira ngati mtunda utalika, ndipo akhoza kumupha ngakhale kuti sanayenera kufa popeza sanaphe mnzake mwadala.
Lest the avenger of blood pursue the manslayer, while his heart is hot, and overtake him, because the way is long, and smite him mortally, whereas he was not worthy of death, inasmuch as he did not hate him in time past.
7 Ichi ndi chifukwa chake ndikukulamulani kuti mudzipatulire nokha mizinda itatu.
Therefore I command thee, saying, Thou shall set apart three cities for thee.
8 Ngati Yehova Mulungu wanu akulitsa malire anu monga analonjezera pa malumbiro ndi makolo anu, nakupatsani dziko lonse monga analonjezera,
And if Jehovah thy God enlarge thy border, as he has sworn to thy fathers, and give thee all the land which he promised to give to thy fathers,
9 chifukwa chotsatira bwino malamulo onse amene ndikukuwuzani lero, kukonda Yehova Mulungu wanu ndi kuyenda mʼnjira zake nthawi zonse, ndiye kuti mukuyenera kupatula mizinda itatu yowonjezera.
if thou shall keep all this commandment to do it, which I command thee this day, to love Jehovah thy God, and to walk ever in his ways, then shall thou add three more cities for thee, besides these three,
10 Muchite zimenezi kuti musakhetse magazi wosalakwa mʼdziko lanu limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani ngati cholowa, ndipo kuti musapezeke ndi mlandu wokhetsa magazi.
that innocent blood not be shed in the midst of thy land, which Jehovah thy God gives thee for an inheritance, and so blood be upon thee.
11 Koma ngati munthu adana ndi mnzake namubisalira panjira nʼkumuvulaza mpaka kumupha, nathawira ku umodzi mwa mizindayi,
But if any man hates his neighbor, and lies in wait for him, and rises up against him, and smites him mortally so that he dies, and he flees into one of these cities,
12 akuluakulu a mu mzinda wake akamugwire ndi kumubwezera ku mzinda wake namupereka kwa wolipsira kuti aphedwe.
then the elders of his city shall send and fetch him from there, and deliver him into the hand of the avenger of blood, that he may die.
13 Osamumvera chisoni. Muyenera kuchotsa tchimo lokhetsa magazi wosalakwa mu Israeli kuti zinthu zizikuyenderani bwino.
Thine eye shall not pity him, but thou shall put away the innocent blood from Israel, that it may go well with thee.
14 Musamasunthe mwala wa malire anu ndi mnzanu amene anayikidwa ndi makolo anu pa cholowa chimene mulandire mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani.
Thou shall not remove thy neighbor's landmark, which they of old time have set, in thine inheritance which thou shall inherit, in the land that Jehovah thy God gives thee to possess it.
15 Mboni imodzi siyokwanira kupeza munthu kuti ndi wolakwa pa mlandu uliwonse umene wapalamula. Nkhani itsimikizike ndi umboni wa anthu awiri kapena atatu.
One witness shall not rise up against a man for any iniquity, or for any sin, in any sin that he sins. At the mouth of two witnesses, or at the mouth of three witnesses, shall a matter be established.
16 Ngati mboni yonama ifuna kunamizira munthu mlandu,
If an unrighteous witness rises up against any man to testify against him of wrong-doing,
17 anthu awiri okhudzidwa ndi mlanduwo ayenera kuyima pamaso pa Yehova pali ansembe ndi oweruza amene ali pa ntchito pa nthawiyo.
then both the men, between whom the controversy is, shall stand before Jehovah, before the priests and the judges that shall be in those days,
18 Oweruza afufuze bwinobwino, ndipo ngati zatsimikizika kuti mboniyo ndi yabodza, yopereka umboni wonama pa mʼbale wake,
and the judges shall make diligent inquiry. And, behold, if the witness is a false witness, and has testified falsely against his brother,
19 ndiye kuti amuchitire iyeyo zimene anafuna kuchitira mʼbale wakezo. Muyenera kuchotsa choyipa pakati panu.
then ye shall do to him, as he had thought to do to his brother. So shall thou put away the evil from the midst of thee.
20 Anthu ena onse adzamva zimenezi nachita mantha, ndipo choyipa choterechi sichidzachitikanso pakati panu.
And those who remain shall hear, and fear, and shall henceforth commit no more any such evil in the midst of thee.
21 Osachita chisoni, moyo uzilipira moyo, diso kulipira diso, dzino kulipira dzino, dzanja kulipira dzanja ndi phazi kulipira phazi.
And thine eyes shall not pity: life for life, eye for eye, tooth for tooth, hand for hand, foot for foot.

< Deuteronomo 19 >