< 2 Samueli 18 >

1 Davide anasonkhanitsa anthu amene anali naye ndipo anasankha atsogoleri ena olamulira ankhondo 1,000 ndi ena olamulira ankhondo 100.
And David numbered the people who were with him, and set captains of thousands and captains of hundreds over them.
2 Davide anatumiza asilikaliwo atawagawa patatu: gulu loyamba limalamulidwa ndi Yowabu, gulu lachiwiri limalamulidwa ndi Abisai ndipo gulu lachitatu limalamulidwa ndi Itai Mgiti. Mfumu inawuza asilikaliwo kuti, “Inenso ndipita nanu ndithu.”
And David sent forth the people, a third part under the hand of Joab, and a third part under the hand of Abishai the son of Zeruiah, Joab's brother, and a third part under the hand of Ittai the Gittite. And the king said to the people, I will surely go forth with you myself also.
3 Koma anthuwo anati, “Inu musapite nafe. Ngati tidzathamangitsidwa, iwowo sadzasamala za ife. Ngakhale theka la ife litafa, iwo sadzasamalako. Koma inuyo ndinu ofunika kuposa asilikali 10,000. Nʼkwabwino kwambiri kuti inu muzititumizira chithandizo kuchokera ku mzindako.”
But the people said, Thou shall not go forth. For if we flee away, they will not care for us, neither if half of us die, will they care for us, but thou are worth ten thousand of us. Therefore now it is better that thou be ready to help us out of the city.
4 Mfumu inayankha kuti, “Ine ndichita chimene chili chokukomerani.” Kotero mfumu inayima pambali pa chipata pamene ankhondo onse amayenda mʼmagulu a anthu 100 ndi a 1,000.
And the king said to them, What seems best to you I will do. And the king stood by the gate-side, and all the people went out by hundreds and by thousands.
5 Mfumu inalamulira Yowabu, Abisai ndi Itai kuti, “Mumukomere mtima Abisalomu chifukwa cha ine.” Ndipo asilikali onse anamva pamene mfumu imalamula izi za Abisalomu kwa wolamulira aliyense.
And the king commanded Joab and Abishai and Ittai, saying, Deal gently for my sake with the young man, even with Absalom. And all the people heard when the king gave all the captains charge concerning Absalom.
6 Ankhondo anayenda kupita kukachita nkhondo ndi Israeli, ndipo nkhondo inachitika mʼnkhalango ya Efereimu.
So the people went out into the field against Israel, and the battle was in the forest of Ephraim.
7 Aisraeli anagonjetsedwa kumeneko ndi ankhondo a Davide. Tsiku limenelo anaphedwa anthu okwanira 20,000.
And the people of Israel were smitten there before the servants of David, and there was a great slaughter there that day of twenty thousand men.
8 Nkhondo inafalikira ku madera onse akumidzi ndipo anthu akufa chifukwa cha zoopsa za mʼnkhalango anali ambiri tsiku limenelo kuposa akufa ndi lupanga.
For the battle was there spread over the face of all the country, and the forest devoured more people that day than the sword devoured.
9 Tsono zinachitika kuti Abisalomu anakumana ndi asilikali a Davide. Iye anali atakwera bulu ndipo pamene buluyo amadutsa pansi pa nthambi zambiri za mtengo wa thundu, mutu wa Abisalomu unakodwa mu mtengomo. Iye anasiyidwa atatsakamira mʼmalele, pamene bulu amene anakwerapoyo amapitirira.
And Absalom chanced to meet the servants of David. And Absalom was riding upon his mule, and the mule went under the thick boughs of a great oak, and his head caught hold of the oak. And he was taken up between sky and earth, and the mule that was under him went on.
10 Mmodzi mwa asilikali ataona zimenezi, anamuwuza Yowabu kuti, “Ine ndamuona Abisalomu ali lende mu mtengo wa thundu.”
And a certain man saw it, and told Joab, and said, Behold, I saw Absalom hanging in an oak.
11 Yowabu anati kwa munthu amene anamuwuza zimenezi, “Ukuti chiyani! Unamuona? Nʼchifukwa chiyani sunamukanthire pansi pomwepo? Ndipo ine ndikanakupatsa ndalama za siliva khumi ndi lamba wausilikali.”
And Joab said to the man who told him, and, behold, thou saw it, and why did thou not smite him there to the ground? And I would have given thee ten pieces of silver, and a belt.
12 Koma munthuyo anayankha kuti, “Ngakhale atandipatsa mʼmanja mwanga ndalama zasiliva 1,000, sindingatambasule dzanja langa kupha mwana wa mfumu. Ife tikumva, mfumu inalamula inu Abisai ndiponso Itai kuti, ‘Mutetezeni mnyamatayo Abisalomu chifukwa cha ine!’
And the man said to Joab, Though I should receive a thousand pieces of silver in my hand, yet I would not put forth my hand against the king's son, for in our hearing the king charged thee and Abishai and Ittai, saying, Beware that none touch the young man Absalom.
13 Ndipo sindikanayika moyo wanga pa chiswe pakuti palibe chimene chimabisika pamaso pa mfumu komanso inu simukanditeteza.”
Otherwise if I had dealt falsely against his life (and there is no matter hid from the king), then thou thyself would have set thyself against me.
14 Yowabu anati, “Ine sinditayanso nthawi ndi iwe.” Ndipo anatenga mikondo itatu mʼmanja mwake ndipo anabaya pamtima pa Abisalomu, Abisalomuyo akanali ndi moyo pa mtengo wa thundu.
Then Joab said, I will not delay thus with thee. And he took three darts in his hand, and thrust them through the heart of Absalom while he was yet alive in the midst of the oak.
15 Ndipo anthu khumi onyamula zida za Yowabu anazungulira Abisalomu, kumubaya ndi kumupha.
And ten young men who bore Joab's armor encompassed about and smote Absalom, and killed him.
16 Kenaka Yowabu analiza lipenga ndipo asilikali analeka kuthamangitsa Israeli pakuti Yowabu anawaletsa.
And Joab blew the trumpet, and the people returned from pursuing after Israel, for Joab held back the people.
17 Iwo anatenga Abisalomu ndi kumuponya mʼdzenje lalikulu mʼchipululumo ndipo anawunjikapo miyala ikuluikulu. Nthawiyi Aisraeli onse anathawa kupita ku nyumba zawo.
And they took Absalom, and cast him into the great pit in the forest, and raised over him a very great heap of stones. And all Israel fled every man to his tent.
18 Abisalomu ali ndi moyo anadzimangira chipilala mʼchigwa cha mfumu, pakuti ankaganiza kuti, “Ine ndilibe mwana wamwamuna amene adzakhale chikumbutso changa.” Chipilalacho anachitchula dzina lake lomwe ndipo mpaka lero chimatchedwa chipilala cha Abisalomu.
Now Absalom in his lifetime had taken and reared up for himself the pillar which is in the king's valley, for he said, I have no son to keep my name in remembrance. And he called the pillar after his own name, and it is called Absalom's monument to this day.
19 Tsono Ahimaazi mwana wa Zadoki anati, “Ndiloleni ndithamange ndi kukapereka uthenga kwa mfumu kuti Yehova wayipulumutsa mʼdzanja la adani ake.”
Then Ahimaaz the son of Zadok said, Let me now run, and bear the king news, how that Jehovah has avenged him of his enemies.
20 Yowabu anamuwuza iye kuti, “Iwe si amene uti ukanene zimenezi lero. Ukapereka uthenga nthawi ina, koma usatero lero, chifukwa mwana wa mfumu wafa.”
And Joab said to him, Thou shall not be the bearer of news this day, but thou shall bear news another day. But this day thou shall bear no news, because the king's son is dead.
21 Kenaka Yowabu anawuza Mkusi kuti, “Pita ukawuze mfumu zimene waona.” Mkusiyo anawerama pamaso pa Yowabu ndipo anathamanga kupita.
Then Joab said to the Cushite, Go, tell the king what thou have seen. And the Cushite bowed himself to Joab, and ran.
22 Ahimaazi mwana wa Zadoki ananenanso kwa Yowabu kuti, “Zivute zitani, chonde mundilole kuti ndipite pambuyo pa Mkusiyo.” Koma Yowabu anayankha kuti, “Mwana wanga, nʼchifukwa chiyani ukufuna kupita? Ulibe nkhani yoti ukalandire nayo mphotho.”
Then Ahimaaz the son of Zadok said yet again to Joab, But come what may, let me, I pray thee, also run after the Cushite. And Joab said, Why will thou run, my son, seeing that thou will have no reward for the news?
23 Iye anati, “Zivute zitani ine ndikufuna kuti ndipite.” Choncho Yowabu anati “Pita!” Ndipo Ahimaazi anathamanga kudzera njira ya ku chigwa ndipo anamupitirira Mkusi uja.
But come what may, he said, I will run. And he said to him, Run. Then Ahimaaz ran by the way of the Plain, and outran the Cushite.
24 Nthawi imeneyo nʼkuti Davide atakhala pakati pa zipata ziwiri, chakubwalo ndi chamʼkati. Mlonda anakwera pa khoma nakayimirira pa denga la chipata. Anati atayangʼana, anaona munthu akuthamanga yekhayekha.
Now David was sitting between the two gates. And the watchman went up to the roof of the gate to the wall, and lifted up his eyes, and looked, and, behold, a man running alone.
25 Mlonda uja anapita kwa mfumu ndipo anafotokoza. Mfumu inati, “Ngati ali yekha ali ndi nkhani yabwino” Ndipo munthuyo anayandikira.
And the watchman cried, and told the king. And the king said, If he is alone, there is news in his mouth. And he came apace, and drew near.
26 Mlonda uja anaonanso munthu wina akuthamanga, ndipo anayitana woyangʼanira pa chipata, “Taona, munthu winanso akuthamanga ali yekha!” Mfumu inati, “Iye akubweretsanso nkhani yabwino.”
And the watchman saw another man running. And the watchman called to the porter, and said, Behold, another man running alone. And the king said, He also brings news.
27 Mlonda uja anati, “Munthu akuthamanga patsogoloyo, kathamangidwe kake kakufanafana ndi mmene amathamangira Ahimaazi, mwana wa Zadoki.” Mfumu inati, “Ameneyo ndi munthu wabwino, ndipo akubwera ndi nkhani yabwino.”
And the watchman said, I think the running of the foremost is like the running of Ahimaaz the son of Zadok. And the king said, He is a good man, and comes with good news.
28 Ndipo Ahimaazi anafuwula kwa mfumu, “Zonse zili bwino!” Iye anagwada pamaso pa mfumu nkhope yake atagunditsa pansi ndipo anati, “Yehova Mulungu wathu alemekezedwe! Iye wapereka mʼdzanja lathu anthu amene anawukira inu mbuye wanga mfumu.”
And Ahimaaz called, and said to the king, All is well. And he bowed himself before the king with his face to the earth, and said, Blessed be Jehovah thy God, who has delivered up the men who lifted up their hand against my lord the king.
29 Mfumu inafunsa, “Kodi mnyamata uja Abisalomu watetezedwa?” Ahimaazi anayankha, “Pamene Yowabu amati azindituma ine mtumiki wanu ndinaona chipiringu cha anthu, koma sindikudziwa chinali chiyani.”
And the king said, Is it well with the young man Absalom? And Ahimaaz answered, When Joab sent the king's servant, even me thy servant, I saw a great tumult, but I knew not what it was.
30 Mfumu inati, “Ima apo ndipo udikire.” Kotero iye anapita pa mbali nayima pamenepo.
And the king said, Turn aside, and stand here. And he turned aside, and stood still.
31 Kenaka Mkusi uja anafika ndipo anati, “Mbuye wanga mfumu imvani nkhani yabwino! Yehova wakupulumutsani inu lero kwa onse amene anakuwukirani.”
And, behold, the Cushite came. And the Cushite said, News for my lord the king, for Jehovah has avenged thee this day of all those who rose up against thee.
32 Mfumu inafunsa Mkusiyo kuti, “Kodi mnyamata uja Abisalomu watetezedwa?” Mkusiyo anayankha kuti, “Adani anu mbuye wanga mfumu, pamodzi ndi anthu onse amene amakuwukirani, ziwaonekere zomwe zamuonekera mnyamatayo.”
And the king said to the Cushite, Is it well with the young man Absalom? And the Cushite answered, The enemies of my lord the king, and all who rise up against thee to do thee hurt, be as that young man is.
33 Mfumu inanthunthumira. Inapita ku chipinda cha mmwamba cha pa chipata kukalira. Pamene imapita, inkati: “Iwe mwana wanga Abisalomu! Mwana wanga! Mwana wanga Abisalomu! Zikanakhala bwino ndikanafa ndine mʼmalo mwako! Iwe Abisalomu, mwana wanga, mwana wanga!”
And the king was much moved, and went up to the chamber over the gate, and wept. And as he went, thus he said, O my son Absalom, my son, my son Absalom! Would I had died for thee, O Absalom, my son, my son!

< 2 Samueli 18 >